Yohane 4 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 4:1-54

Yesu Acheza ndi Mayi wa ku Samariya

1Yesu atazindikira kuti Afarisi amva zoti Iye ankapeza ndi kubatiza ophunzira ambiri kupambana Yohane, 2(ngakhale kuti Yesuyo sankabatiza, koma ophunzira ake). 3Iye anachoka ku Yudeya ndi kubwereranso ku Galileya.

4Ndipo Iye anayenera kudutsa mu Samariya. 5Iye anafika mʼmudzi wa Asamariya wotchedwa Sukari, pafupi ndi malo amene Yakobo anapatsa mwana wake Yosefe. 6Chitsime cha Yakobo chinali pamenepo ndipo Yesu atatopa ndi ulendo anakhala pansi pambali pa chitsimecho. Nthawi inali pafupifupi ora lachisanu ndi chimodzi masana.

7Mayi wa Chisamariya atabwera kudzatunga madzi, Yesu anati kwa iye, “Kodi ungandipatse madzi akumwa.” 8(Ophunzira ake nʼkuti atapita mʼmudzi kukagula chakudya).

9Mayiyo anati kwa Iye, “Inu ndinu Myuda ndipo ine ndine Msamariya. Bwanji mukundipempha madzi akumwa?” (Popeza Ayuda ndi Asamariya sankayanjana).

10Yesu anamuyankha kuti, “Koma iwe ukanadziwa mphatso ya Mulungu ndi Iye amene akukupempha madzi akumwa, ukanamupempha ndipo akanakupatsa madzi amoyo.”

11Mayiyo anati, “Ambuye, Inu mulibe kanthu kotungira madzi ndipo chitsime ndi chakuya. Kodi madzi amoyowo mungawatenge kuti? 12Kodi Inu ndinu wamkulu kuposa kholo lathu Yakobo, amene anatipatsa chitsimechi ndipo iye ankamwanso monga anachita ana ake ndi ziweto zake?”

13Yesu anayankha kuti, “Aliyense amene amamwa madzi awa amamvanso ludzu, 14koma aliyense amene adzamwa madzi amene Ine ndidzamupatsa sadzamvanso ludzu. Ndithudi, madzi amene ndidzamupatsa adzakhala kasupe wamadzi wotumphukira ku moyo wosatha.”

15Mayiyo anati kwa Iye, “Ambuye, patseni madzi amenewo kuti ndisadzamvenso ludzu ndi kumabwerabe kuno kudzatunga madzi.”

16Iye anamuwuza kuti, “Pita kayitane mwamuna wako ndipo ubwere naye.”

17Iye anayankha kuti, “Ine ndilibe mwamuna.”

Yesu anati kwa iye, “Wakhoza ponena kuti ulibe mwamuna. 18Zoona nʼzakuti iwe wakhala pa banja ndi amuna asanu, ndipo mwamuna amene uli naye tsopano si wako. Zimene wanenazi ndi zoona.”

19Mayiyo anati, “Ambuye, ine ndazindikira kuti Inu ndinu mneneri. 20Makolo athu ankapembedza mʼphiri ili koma inu Ayuda mumati malo amene tiyenera kupembedzera ali ku Yerusalemu.”

21Yesu anati, “Mayi inu khulupirira Ine. Nthawi ikubwera pamene inu simudzapembedza Atate mʼphiri ili kapena mu Yerusalemu. 22Inu Asamariya mumapembedza chimene simukuchidziwa. Ife timapembedza chimene tikuchidziwa, pakuti chipulumutso nʼchochokera kwa Ayuda. 23Koma nthawi ikubwera ndipo yafika kale tsopano pamene opembedza woona adzapembedza Atate mu mzimu ndi mʼchoonadi, pakuti opembedza otere ndiwo amene Atate akuwafuna. 24Mulungu ndi Mzimu, ndipo omupembedza Iye ayenera kumupembedza mu mzimu ndi mʼchoonadi.”

25Mayiyo anati, “Ine ndikudziwa kuti Mesiya (wotchedwa Khristu) akubwera. Akabwera, Iye adzafotokoza zonse kwa ife.”

26Ndipo Yesu anamuwuza kuti, “Amene ndikukuyankhulane, ndine amene.”

Ophunzira Abweranso kwa Yesu

27Pa nthawi yomweyo ophunzira ake anabwerera ndipo anadabwa kupeza Iye akuyankhula ndi mayi. Koma palibe amene anamufunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” kapena, “Nʼchifukwa chiyani mukuyankhula naye?”

28Kenaka mayiyo anasiya mtsuko wamadzi, nabwerera ku mzinda ndipo anati kwa anthu, 29“Tiyeni mukaone munthu amene wandiwuza ine zilizonse zimene ndinazichita. Kodi ameneyu sangakhale Khristu?” 30Iwo anatuluka mʼmudziwo ndi kupita kumene kunali Iye.

31Pa nthawi imeneyi ndi kuti ophunzira ake akumukakamiza kuti, “Rabi idyani.”

32Koma Iye anawawuza kuti, “Ine ndili ndi chakudya choti ndidye chimene inu simukuchidziwa.”

33Ndipo ophunzira ake anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi alipo wina amene anamubweretsera Iye chakudya?”

34Yesu anati, “Chakudya changa ndikuchita chifuniro cha Iye amene anandituma Ine ndi kumaliza ntchito yake. 35Kodi inu simunena kuti, ‘Kwatsala miyezi inayi ndipo kenaka kukolola?’ Ine ndikukuwuzani kuti, tsekulani maso anu ndipo muyangʼane mʼminda! Mbewu zacha kale kuti zikololedwe. 36Ngakhale tsopano amene akukolola akulandira malipiro ake, ndipo akututa mbewu ku moyo wosatha kuti wofesa ndi wokolola asangalale pamodzi. 37Nʼchifukwa chake mawu akuti, ‘Wina amafesa ndipo wina amakolola’ ndi woona. 38Ine ndinakutumani kukakolola zimene simunagwirire ntchito. Ena anagwira ntchito yolemetsa ndipo inu mwatuta phindu la ntchito yawo.”

Asamariya Ambiri Akhulupirira

39Asamariya ambiri ochokera mʼmudziwo anakhulupirira Iye chifukwa cha umboni wa mayiyo wakuti, “Iye anandiwuza ine zonse ndinazichita.” 40Choncho Asamariya atabwera kwa Iye, anamuwumiriza Iye kuti akhale nawo, ndipo Iye anakhala nawo masiku awiri. 41Ndipo chifukwa cha mawu ake, ena ambiri anakhulupirira.

42Iwo anati kwa mayiyo, “Ife sitikukhulupirira chifukwa cha mawu ako okha, koma tsopano ife tadzimvera tokha, ndipo tikudziwa kuti munthu uyu ndithu ndi Mpulumutsi wa dziko lapansi.”

Yesu Achiritsa Mwana wa Nduna ya Mfumu

43Patatha masiku awiri Iye anachoka napita ku Galileya. 44(Tsopano Yesu mwini ananena kale kuti mneneri salandira ulemu mʼdziko lake). 45Iye atafika ku Galileya, Agalileya anamulandira. Iwo anali ataona zonse zimene anazichita mu Yerusalemu pa phwando la Paska, pakuti iwonso anali komweko.

46Iye anakafikanso ku Kana wa ku Galileya, kumene anasanduliza madzi kukhala vinyo. Ndipo kumeneko kunali nduna ina ya mfumu imene mwana wake wamwamuna anali chigonere akudwala ku Kaperenawo. 47Munthu uyu atamva kuti Yesu wafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya, anapita kwa Iye, namupempha kuti apite akachiritse mwana wakeyo, amene anali pafupi kufa.

48Yesu anawawuza iwo kuti, “Anthu inu pokhapokha mutaona zizindikiro zodabwitsa, simudzakhulupirira.”

49Nduna ya mfumuyo inati, “Ambuye tiyeni mwana wanga asanafe.”

50Yesu anayankha kuti, “Pita. Mwana wako adzakhala ndi moyo.”

Munthuyo anakhulupirira mawu a Yesu ndipo ananyamuka. 51Iye ali pa njira, antchito ake anakumana naye, namuwuza kuti mwana wanu uja wachira. 52Iye atafunsa kuti ndi nthawi yanji imene mwana wake anapeza bwino, iwo anati kwa iye, “Malungo anamusiya iye dzulo pa ora lachisanu ndi chiwiri.”

53Ndipo bamboyo anazindikira kuti iyi inali nthawi yomweyo imene Yesu anati kwa iye, “Mwana wako adzakhala ndi moyo.” Choncho iye ndi onse a pa banja lake anakhulupirira.

54Ichi ndiye chinali chizindikiro chodabwitsa chachiwiri chimene Yesu anachita atafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya.

Thai New Contemporary Bible

ยอห์น 4:1-54

พระเยซูทรงสนทนากับหญิงชาวสะมาเรีย

1พวกฟาริสีได้ยินว่าพระเยซูทรงมีสาวกและให้บัพติศมามากกว่ายอห์น 2อันที่จริงไม่ใช่พระเยซูแต่สาวกของพระองค์ต่างหากที่ให้บัพติศมา 3เมื่อพระเยซูทรงทราบเช่นนี้ก็เสด็จจากแคว้นยูเดียกลับไปยังแคว้นกาลิลีอีก

4พระองค์ต้องเสด็จผ่านแคว้นสะมาเรีย 5จึงเสด็จมายังเมืองหนึ่งในแคว้นสะมาเรียชื่อสิคาร์ ใกล้ที่ดินแปลงที่ยาโคบยกให้โยเซฟบุตรชายของเขา 6บ่อน้ำของยาโคบอยู่ที่นั่น และพระเยซูทรงเหน็ดเหนื่อยจากการเดินทางจึงประทับนั่งข้างๆ บ่อ ขณะนั้นเป็นเวลาประมาณเที่ยง

7เมื่อหญิงชาวสะมาเรียคนหนึ่งมาตักน้ำ พระเยซูตรัสกับนางว่า “ขอน้ำให้เราดื่มหน่อยได้ไหม?” 8(สาวกของพระองค์เข้าไปซื้ออาหารในเมือง)

9หญิงชาวสะมาเรียทูลว่า “ท่านเป็นยิว ส่วนดิฉันเป็นหญิงชาวสะมาเรีย ท่านมาขอน้ำจากดิฉันได้อย่างไร?” (เพราะชาวยิวไม่คบหากับชาวสะมาเรีย4:9 หรือไม่ใช้ภาชนะที่ชาวสะมาเรียเคยใช้)

10พระเยซูตรัสตอบนางว่า “ถ้าเจ้ารู้จักของที่พระเจ้าประทานและรู้จักผู้ที่ขอน้ำจากเจ้า เจ้าคงจะขอจากผู้นั้นและผู้นั้นจะให้น้ำซึ่งให้ชีวิตแก่เจ้า”

11หญิงนั้นทูลว่า “ท่านเจ้าข้า ท่านไม่มีอะไรที่จะใช้ตักน้ำและบ่อก็ลึก ท่านจะได้น้ำซึ่งให้ชีวิตมาจากไหน? 12ท่านยิ่งใหญ่กว่ายาโคบบรรพบุรุษของเราผู้ซึ่งให้บ่อนี้แก่เราหรือ? และยาโคบเองกับลูกหลานตลอดจนฝูงสัตว์ก็ดื่มน้ำจากบ่อนี้”

13พระเยซูตรัสตอบว่า “ทุกคนที่ดื่มน้ำนี้จะกระหายอีก 14แต่ผู้ใดดื่มน้ำที่เราให้จะไม่กระหายอีกเลย อันที่จริงน้ำซึ่งเราให้เขานั้นจะกลายเป็นน้ำพุในตัวเขาพลุ่งขึ้นสู่ชีวิตนิรันดร์”

15หญิงนั้นทูลพระองค์ว่า “ท่านเจ้าข้า โปรดให้น้ำนั้นแก่ดิฉันเพื่อดิฉันจะไม่กระหายอีกและไม่ต้องกลับมาตักน้ำที่นี่เสมอๆ”

16พระเยซูตรัสบอกนางว่า “จงไปเรียกสามีของเจ้ามา”

17นางทูลว่า “ดิฉันไม่มีสามี”

พระเยซูตรัสกับนางว่า “เจ้าพูดถูกที่ว่าไม่มีสามี 18อันที่จริงเจ้ามีสามีห้าคนแล้ว และชายคนที่เจ้าอยู่ด้วยขณะนี้ก็ไม่ใช่สามีของเจ้า สิ่งที่เจ้าเพิ่งพูดไปนั้นก็ออกจะจริงทีเดียว”

19หญิงนั้นทูลว่า “ท่านเจ้าข้า ดิฉันเห็นแล้วว่าท่านเป็นผู้เผยพระวจนะ 20บรรพบุรุษของเรานมัสการที่ภูเขานี้ แต่พวกท่านชาวยิวอ้างว่าเราต้องนมัสการที่กรุงเยรูซาเล็ม”

21พระเยซูประกาศว่า “หญิงเอ๋ย เชื่อเราเถิด ใกล้ถึงเวลาแล้ว เมื่อพวกท่านจะนมัสการพระบิดาไม่ใช่ที่ภูเขานี้หรือที่กรุงเยรูซาเล็ม 22พวกท่านชาวสะมาเรียนมัสการสิ่งที่ท่านไม่รู้จัก ส่วนเรานมัสการสิ่งที่เรารู้จักเพราะความรอดมาจากพวกยิว 23กระนั้นก็ใกล้ถึงเวลาแล้ว และบัดนี้ก็ถึงเวลาแล้วที่ผู้นมัสการอย่างถูกต้องจะนมัสการพระบิดาด้วยจิตวิญญาณและความจริง เพราะพวกเขาเป็น ผู้นมัสการแบบที่พระบิดาทรงแสวงหา 24พระเจ้าทรงเป็นพระวิญญาณ ผู้ที่นมัสการพระองค์ต้องนมัสการด้วยจิตวิญญาณและความจริง”

25หญิงนั้นทูลว่า “ดิฉันรู้ว่าพระเมสสิยาห์ (ที่เรียกว่าพระคริสต์) กำลังเสด็จมา เมื่อพระองค์เสด็จมาแล้ว จะทรงอธิบายทุกสิ่งแก่เรา”

26แล้วพระเยซูทรงประกาศว่า “เราที่พูดอยู่กับเจ้าคือผู้นั้น”

เหล่าสาวกกลับมาสมทบกับพระเยซู

27ขณะนั้นเองเหล่าสาวกก็กลับมาถึง และพากันประหลาดใจที่พบพระองค์ทรงสนทนาอยู่กับผู้หญิง แต่ไม่มีใครทูลถามว่า “พระองค์ทรงประสงค์สิ่งใด?” หรือ “ทำไมพระองค์ทรงสนทนากับนาง?”

28แล้วหญิงนั้นก็ทิ้งหม้อน้ำ กลับเข้าเมือง และบอกกับผู้คนว่า 29“มาเถิด มาดูชายผู้หนึ่งซึ่งบอกทุกสิ่งที่ดิฉันเคยทำ ท่านผู้นี้จะเป็นพระคริสต์4:29 หรือพระเมสสิยาห์ได้ไหม?” 30พวกเขาจึงออกจากเมืองมุ่งหน้ามาหาพระองค์

31ขณะนั้นเหล่าสาวกทูลรบเร้าพระองค์ว่า “รับบี รับประทานอาหารบ้างเถิด”

32แต่พระองค์ตรัสกับพวกเขาว่า “เรามีอาหารรับประทานซึ่งพวกท่านไม่รู้”

33เหล่าสาวกจึงพูดกันว่า “มีใครเอาอาหารมาถวายพระองค์แล้วหรือ?”

34พระเยซูตรัสว่า “อาหารของเราคือการทำตามพระประสงค์ของพระองค์ผู้ทรงส่งเรามา และทำพระราชกิจของพระองค์ให้สำเร็จ 35ท่านพูดไม่ใช่หรือว่าอีกสี่เดือนก็จะถึงฤดูเก็บเกี่ยว? เราบอกท่านว่าจงลืมตาดูท้องนาเถิด! ข้าวสุกพร้อมจะเก็บเกี่ยวแล้ว 36เวลานี้ผู้เกี่ยวก็กำลังรับค่าจ้าง เวลานี้เขากำลังเก็บเกี่ยวพืชผลสำหรับชีวิตนิรันดร์ เพื่อผู้หว่านและผู้เกี่ยวจะยินดีด้วยกัน 37ดังนี้จึงเป็นจริงตามคำกล่าวที่ว่า ‘คนหนึ่งหว่านและอีกคนหนึ่งเกี่ยว’ 38เราส่งพวกท่านไปเก็บเกี่ยวสิ่งที่พวกท่านไม่ได้ลงแรง คนอื่นได้ตรากตรำทำงานหนัก และพวกท่านได้เก็บเกี่ยวผลประโยชน์จากการลงแรงของเขา”

ชาวสะมาเรียมากมายเชื่อพระเยซู

39ชาวสะมาเรียมากมายจากเมืองนั้นเชื่อในพระองค์เพราะคำพยานของหญิงนั้นที่ว่า “พระองค์ทรงบอกทุกสิ่งที่ดิฉันเคยทำ” 40ฉะนั้นเมื่อชาวสะมาเรียมาหาพระองค์ พวกเขาจึงรบเร้าให้พระองค์ประทับอยู่กับพวกเขา พระองค์ก็ทรงอยู่ที่นั่นสองวัน 41และเนื่องด้วยพระดำรัสของพระองค์คนอื่นๆ อีกมากมายได้หันมาเชื่อในพระองค์

42พวกเขาบอกหญิงนั้นว่า “ตั้งแต่นี้ไป เราไม่ได้เชื่อเพียงเพราะคำพูดของเจ้า เดี๋ยวนี้เราได้ยินด้วยตัวของเราเอง และเรารู้ว่าพระองค์นี่แหละคือพระผู้ช่วยให้รอดของโลกจริงๆ”

พระเยซูทรงรักษาบุตรชายของข้าราชการ

43หลังจากสองวันนั้น พระเยซูเสด็จจากที่นั่นไปยังแคว้นกาลิลี 44(พระองค์เองทรงชี้ให้เห็นว่าผู้เผยพระวจนะไม่ได้รับเกียรติในบ้านเมืองของตนเอง) 45เมื่อพระองค์มาถึงแคว้นกาลิลี ชาวกาลิลีก็ต้อนรับพระองค์ พวกเขาเคยเห็นสิ่งสารพัดที่ทรงกระทำในกรุงเยรูซาเล็มเมื่อเทศกาลปัสกาเพราะพวกเขาอยู่ที่นั่นด้วย

46พระองค์เสด็จมายังหมู่บ้านคานาในแคว้นกาลิลีอีกครั้งหนึ่ง หมู่บ้านนี้คือที่ซึ่งพระองค์ได้ทรงเปลี่ยนน้ำให้เป็นเหล้าองุ่น และมีข้าราชการคนหนึ่งซึ่งบุตรชายของเขานอนป่วยอยู่ที่เมืองคาเปอรนาอุม 47เมื่อชายผู้นี้ได้ยินว่าพระเยซูเสด็จจากแคว้นยูเดียมาถึงแคว้นกาลิลีแล้ว จึงมาทูลอ้อนวอนพระเยซูให้ไปรักษาลูกชายของเขาซึ่งใกล้จะตายแล้ว

48พระเยซูตรัสกับเขาว่า “ถ้าพวกท่านไม่เห็นหมายสำคัญและปาฏิหาริย์ พวกท่านก็ไม่มีวันเชื่อ”

49ข้าราชการผู้นั้นทูลว่า “ท่านเจ้าข้า โปรดมาก่อนที่บุตรของข้าพเจ้าจะตาย”

50พระเยซูตรัสตอบว่า “กลับไปเถิด บุตรของท่านจะรอดชีวิต”

ชายคนนั้นเชื่อคำที่พระเยซูตรัสและลากลับไป 51ขณะที่พวกเขายังอยู่ระหว่างทาง ก็พบกับคนรับใช้ของเขาที่มาบอกข่าวว่าลูกชายของเขารอดชีวิต 52เมื่อเขาถามถึงเวลาที่บุตรชายของเขาอาการดีขึ้น คนเหล่านั้นบอกว่า “เขาหายไข้เมื่อวานนี้ตอนบ่ายโมง”

53แล้วบิดาจึงตระหนักว่าเป็นเวลาเดียวกันกับที่พระเยซูตรัสกับเขาว่า “บุตรของท่านจะรอดชีวิต” ดังนั้นเขาและคนในครัวเรือนของเขาทั้งหมดจึงเชื่อ

54นี่คือหมายสำคัญครั้งที่สองซึ่งพระเยซูได้ทรงกระทำ เมื่อเสด็จจากแคว้นยูเดียมายังแคว้นกาลิลี