Yohane 3 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 3:1-36

Yesu Aphunzitsa Nekodimo za Kubadwa Kwatsopano

1Ndipo panali Mfarisi wotchedwa Nekodimo, wa mʼgulu lolamulira la Ayuda. 2Iye anabwera kwa Yesu usiku ndipo anati, “Rabi, ife tikudziwa kuti ndinu aphunzitsi wochokera kwa Mulungu, pakuti palibe amene angachite zizindikiro zodabwitsa zimene Inu mukuchita ngati Mulungu sali naye.”

3Poyankha Yesu ananena kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti, ngati munthu sabadwanso mwatsopano sangathe kuona ufumu wa Mulungu.”

4Nekodimo anati, “Kodi munthu angabadwenso bwanji atakalamba? Kodi angalowe kachiwiri mʼmimba ya amayi ake kuti abadwenso?”

5Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti ngati munthu sabadwa mwa madzi ndi Mzimu Woyera, sangalowe mu ufumu wa Mulungu. 6Thupi limabereka thupi, koma Mzimu amabereka mzimu. 7Iwe usadabwe chifukwa ndakuwuza kuti, ‘Uyenera kubadwanso.’ 8Mphepo imawomba kulikonse kumene ikufuna. Ungathe kumva kuwomba kwake, koma sungathe kudziwa kumene ikuchokera kapena kumene ikupita. Nʼchimodzimodzi ndi amene abadwa ndi Mzimu Woyera.”

9Nekodimo anafunsa kuti, “Kodi izi zingatheke bwanji?”

10Yesu anati, “Iwe mphunzitsi wa Israeli, kodi sukuzindikira zimenezi? 11Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti ife tiyankhula zimene tikuzidziwa ndi kuchitira umboni zimene taziona, komabe inu simuvomereza umboni wathu. 12Ine ndikuyankhula kwa iwe zinthu za dziko lapansi ndipo sukukhulupirira. Nanga kodi udzakhulupirira bwanji ngati nditayankhula zinthu zakumwamba? 13Palibe wina aliyense anapita kumwamba, koma yekhayo amene watsika kuchokera kumwamba, Mwana wa Munthu. 14Tsono monga Mose anapachika njoka mʼchipululu, moteronso Mwana wa Munthu ayenera kupachikidwa, 15kuti aliyense amene akhulupirira Iye akhale ndi moyo wosatha.

16“Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi, kotero anapereka Mwana wake wobadwa yekha, kuti aliyense wokhulupirira Iye asatayike koma akhale ndi moyo wosatha. 17Pakuti Mulungu sanatume Mwana wake ku dziko lapansi, kuti akaweruze, koma kuti akapulumutse dziko lapansi. 18Aliyense wokhulupirira Iye saweruzidwa, koma aliyense wosakhulupirira waweruzidwa kale chifukwa sanakhulupirire dzina la Mwana wobadwa yekha wa Mulungu. 19Ndipo chiweruzo ndi ichi: kuwunika kunabwera mʼdziko lapansi, koma anthu anakonda mdima mʼmalo mwa kuwunikako, chifukwa ntchito zawo zinali zoyipa. 20Aliyense wochita zoyipa amadana ndi kuwunika, ndipo sabwera poyera chifukwa cha mantha kuti ntchito zake zingaonekere. 21Koma aliyense wokhala mu choonadi amabwera ku kuwunika, kuti zionekere poyera zimene iye wachita zachitika kudzera mwa Mulungu.”

Yohane Mʼbatizi Achita Umboni za Yesu

22Zitatha izi, Yesu ndi ophunzira ake anapita mʼmadera a ku midzi ya ku Yudeya, kumene Iye anakhala kanthawi akubatiza. 23Ndipo Yohane amabatizanso ku Ainoni kufupi ndi Salimu, chifukwa kumeneko kunali madzi ambiri ndipo anthu amabwererabwererabe kudzabatizidwa. 24(Apa nʼkuti Yohane asanatsekeredwe mʼndende). 25Mkangano unabuka pakati pa ophunzira ena a Yohane ndi Ayuda ena pa zamwambo wodziyeretsa wa Ayuda. 26Iwo anabwera kwa Yohane anati, “Rabi, munthu uja munali naye mbali inayo ya mu mtsinje wa Yorodani, amene munamuchitira umboni, taonani naye akubatizanso, ndipo aliyense akupita kwa Iye.”

27Atamva zimenezi, Yohane anayankha kuti, “Munthu amalandira chokhacho chapatsidwa kwa iye kuchokera kumwamba. 28Inuyo ndinu mboni zanga kuti ine ndinati, ‘Ine sindine Khristu koma ndatumidwa patsogolo pa Iye.’ 29Mwini wake wa mkwatibwi ndi mkwati. Ndipo bwenzi lamkwati limadikira ndi kumvetsera iye, ndipo amakondwa akamva mawu a mkwatiyo. Ine changa ndi chimwemwe ndipo ndine wosangalala kwambiri. 30Nʼkoyenera kuti Iyeyo akule, ine ndichepe.

31“Iye wochokera kumwamba ndi wapamwamba pa onse: iye wochokera mʼdziko lapansi ndi wa dziko lapansi, ndipo amayankhula monga mmodzi wa adziko lapansi. Iye wochokera kumwamba ndi wopambana onse. 32Iye achita umboni pa zimene waziona ndi kuzimva, koma palibe avomereza umboni wake. 33Munthu amene amawulandira akutsimikizira kuti Mulungu ndi woona. 34Pakuti amene Mulungu wamutuma amayankhula mawu a Mulungu; Mulungu wamupatsa Mzimu Woyera mopanda malire. 35Atate amakonda Mwana ndipo apereka zonse mʼmanja mwake. 36Aliyense wokhulupirira Mwanayo ali ndi moyo wosatha, koma iye amene samvera Mwanayo sadzawuona moyo, pakuti mkwiyo wa Mulungu umakhala pa iye.”

New Serbian Translation

Јован 3:1-36

Разговор с Никодимом

1Био неки човек, фарисеј, по имену Никодим, један од водећих људи међу Јеврејима. 2Он је дошао к Исусу по ноћи и рекао му: „Учитељу, знамо да си ти учитељ кога је Бог послао. Нико, наиме, не може чинити ове знаке која ти чиниш ако Бог није са њим.“

3Исус му одговори: „Заиста, заиста ти кажем: нико не може видети Царство Божије ако се наново3,3 Или: од горе. не роди.“

4Никодим га упита: „Како одрастао човек може да се наново роди? Може ли да уђе у утробу своје мајке и да се поново роди?“

5Исус му одговори: „Заиста, заиста ти кажем: нико не може ући у Царство Божије ако се не роди водом и Духом. 6Тело рађа тело, а од Духа се рађа дух. 7Не чуди се што ти кажем: треба да се наново родите. 8Ветар дува где хоће. Његов хук чујеш, али не знаш откуд долази и куда одлази. Тако је са сваким који је рођен од Духа.“

9Никодим упита Исуса: „Како то може да се догоди?“

10Исус му одговори: „Ти си учитељ израиљског народа, а не знаш то? 11Заиста, заиста ти кажем: ми говоримо оно што знамо и сведочимо о ономе што смо видели, али ви не прихватате наше сведочанство. 12Не верујете ми кад вам говорим о земаљским стварима, како ћете веровати ако вам будем говорио о небеским? 13Нико никада није узашао на небо, осим Сина Човечијег који је сишао са неба. 14Као што је Мојсије подигао на штап змију од бронзе, тако и Син Човечији треба да буде подигнут, 15да свако ко поверује у њега има вечни живот.

16Јер Бог је тако заволео свет, да је свог јединорођеног Сина дао, да ко год поверује у њега, не пропадне, него да има вечни живот. 17Бог, наиме, није послао Сина да суди свету, него да се свет спасе његовим посредством. 18Ко верује у њега, томе се не суди; а ко не верује, већ је осуђен, јер није поверовао у име јединороднога Сина Божијег. 19Бог суди овако: светлост је дошла на свет, али људи више заволеше таму него светлост, јер су њихова дела зла. 20Ко чини што не ваља, мрзи светлост и не излази на светлост, да се не открију његова дела. 21Ко чини што је по истини, долази на светлост, да се покаже да су његова дела учињена у послушности према Богу.3,21 Неки сматрају да стихови 16-21 представљају глас наратора.

Сведочанство Јована Крститеља

22После овога је Исус са својим ученицима отишао у Јудеју. Тамо је боравио са њима и крштавао. 23И Јован Крститељ је крштавао у Енону код Салима, јер је тамо било много воде, те су људи долазили и крштавали се. 24Јован тада још није био бачен у тамницу. 25Између Јованових ученика и неког Јеврејина дође до расправе око обредног прања. 26Ученици дођу к Јовану и обрате му се: „Учитељу, онај што је био с тобом с оне стране Јордана, о коме си говорио, ено га крштава и народ одлази к њему.“

27Јован им одговори: „Нико не може присвојити себи нешто ако му то није дано с неба. 28Сами сте ми сведоци да сам рекао: ’Ја нисам Христос, него сам послат пред њим.’ 29Младожења је онај коме млада припада, а кум стоји са стране и слуша, радујући се кад чује глас младожењин. Према томе, моја радост је потпуна. 30Он треба да расте, а ја да се умањујем.“

31Ко долази од горе, над свима је; а ко је са земље, припада земљи и говори о земаљским стварима. Али онај који је са неба, над свима је. 32Он говори оно што је видео и чуо, али његову поруку нико не прихвата. 33Ко прихвата његову поруку, потврђује да је Бог истинит. 34Онај кога је Бог послао, Божију поруку преноси, јер Бог свога Духа у изобиљу даје. 35Отац воли Сина и све је предао у његове руке. 36Ко верује у Сина, има вечни живот; а ко је непокоран Сину, неће искусити живот, него ће гнев Божији остати на њему.