Yohane 20 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 20:1-31

Yesu Auka kwa Akufa

1Mmamawa tsiku loyamba la sabata, kukanali kamdimabe, Mariya wa ku Magadala anapita ku manda ndipo anaona kuti mwala unali utachotsedwa pa khomo la manda. 2Choncho anabwerera akuthamanga kwa Simoni Petro ndi wophunzira winayo, amene Yesu anamukonda, ndipo anati, “Iwo amuchotsa Ambuye mʼmanda, ndipo ife sitikudziwa kumene iwo amuyika Iye!”

3Choncho Petro ndi wophunzira winayo ananyamuka kupita ku manda. 4Onse awiri anathamanga pamodzi koma wophunzira winayo anamupitirira Petro, nafika ku manda moyambirira. 5Ndipo mmene anawerama nasuzumira mʼkati mwa manda anaona nsalu zili potero koma sanalowemo. 6Kenaka Simoni Petro, amene anali pambuyo pake, anafika ndi kulowa mʼmanda. Iye anaona nsaluzo zili pamenepo, 7pamodzinso ndi nsalu imene anakulungira nayo mutu wa Yesu. Nsaluyi inali yopindidwa pa yokha yosiyanitsidwa ndi inayo. 8Pomaliza wophunzira winayo, amene anafika ku manda moyambirira, analowanso mʼkati, iye anaona ndi kukhulupirira. 9(Iwo sanazindikire kuchokera mʼmalemba kuti Yesu anayanera kuuka kuchokera kwa akufa).

Yesu Aonekera kwa Mariya wa ku Magadala

10Kenaka ophunzira anabwerera ku nyumba zawo, 11koma Mariya anayima kunja kwa manda akulira. Pamene akulira, anawerama ndi kusuzumira mʼmanda 12ndipo anaona angelo awiri atavala zoyera, atakhala pamene panali mtembo wa Yesu, mmodzi kumutu ndi wina kumapazi.

13Iwo anamufunsa iye kuti, “Amayi, nʼchifukwa chiyani mukulira?”

Iye anati, “Amuchotsa Mbuye wanga, ndipo ine sindikudziwa kumene iwo amuyika.” 14Atanena izi, iye anatembenuka ndipo anaona Yesu atayima potero koma iye sanazindikire kuti anali Yesu.

15Iye anati, “Amayi, mukulira chifukwa chiyani? Ndani amene mukumufunafuna?”

Poganiza kuti anali mwini munda, iye anati, “Bwana, ngati inu mwamuchotsa, ndiwuzeni kumene mwamuyika, ndipo ine ndikamutenga.”

16Yesu anati kwa iye, “Mariya.”

Anatembenukira kwa Iye nafuwula mu Chiaramaiki kuti, “Raboni!” (kutanthauza Mphunzitsi).

17Yesu anati, “Usandigwire Ine, pakuti sindinapite kwa Atate. Mʼmalo mwake pita kwa abale anga ndikukawawuza kuti, ndikupita kwa Atate ndi kwa Atate anunso, kwa Mulungu wanga ndi Mulungu wanunso.”

18Mariya wa ku Magadala anapita kwa ophunzira ndi uthenga wakuti, “Ndamuona Ambuye!” Iye anawawuza iwo kuti Yesu ananena zinthu izi kwa iye.

Yesu Aonekera kwa Ophunzira ake Tomasi Palibe

19Madzulo a tsiku limenelo limene linali loyamba la Sabata ophunzira ake ali pamodzi, atatseka ndi kukhoma zitseko chifukwa choopa Ayuda, Yesu anabwera ndi kuyima pakati pawo nati, “Mtendere ukhale nanu!” 20Iye atatha kunena izi, anawaonetsa manja ake ndi mʼnthiti mwake. Ophunzira anasangalala kwambiri pamene anaona Ambuye.

21Yesu anatinso, “Mtendere ukhale nanu! Monga Atate anandituma Ine, Inenso ndikukutumani.” 22Ndi mawu amenewo Iye anawapumira ndipo anati, “Landirani Mzimu Woyera. 23Ngati mukhululukira aliyense machimo ake, iwo akhululukidwa; ngati simuwakhululukira, iwo sanakhululukidwe.”

Yesu Aonekera kwa Tomasi

24Koma Tomasi (otchedwa Didimo), mmodzi wa khumi ndi awiriwo, sanali ndi ophunzira pamene Yesu anabwera. 25Ophunzira enawo atamuwuza Tomasi kuti iwo anaona Ambuye, iye ananenetsa kuti, “Pokhapokha nditaona zizindikiro za misomali mʼmanja ake ndi kuyikamo chala changa mʼmene munali misomali ndi kukhudza dzanja langa mʼnthiti mwake, ine sindidzakhulupirira.”

26Patapita sabata, ophunzira ake analinso mʼnyumbamo ndipo Tomasi anali nawo. Ngakhale makomo anali otsekedwa, Yesu anabwera nayima pakati pawo, ndipo anati, “Mtendere ukhale nanu!” 27Kenaka anati kwa Tomasi, “Ika chala chako apa; ona manja anga. Tambasula dzanja lako ndi kukhudza mʼnthiti mwanga. Leka kukayika, khulupirira.”

28Tomasi anati kwa Iye, “Ambuye wanga ndi Mulungu wanga!”

29Kenaka Yesu anamuwuza kuti, “Kodi wakhulupirira chifukwa wandiona Ine? Ndi odala amene amakhulupirira ngakhale asanaone.”

Cholinga cha Uthenga Wabwino wa Yohane

30Yesu anachita zodabwitsa zambiri pamaso pa ophunzira ake zimene sizinalembedwe mʼbuku lino. 31Koma izi zalembedwa kuti mukhulupirire kuti Yesu ndi Khristu, Mwana wa Mulungu, ndi kuti mukakhulupirira mukhale nawo moyo mʼdzina lake.

Slovo na cestu

Jan 20:1-31

Ježíš vstává z mrtvých

1První den po sobotě, ještě před rozedněním, přišla k Ježíšovu hrobu Marie Magdaléna. Uviděla, že kamenný uzávěr hrobky je odsunut. 2Běžela k Petrovi a k učedníkovi, kterého měl Ježíš tolik rád, a oznámila jim: „Našeho Pána vzali z hro-bu a nevíme, kam ho položili.“

3-4Ti dva se zvedli a spěchali ke hrobu. Druhý učedník Petra předběhl a byl tam první. 5Do hrobu však jenom nahlédl a uviděl prázdné plátno. 6Ale tu přiběhl Petr, který vešel dovnitř a kromě plátna nalezl 7i šátek, jímž byla ovázána Ježíšova hlava; ten byl svinutý a položený zvlášť. 8-9Za Petrem vstoupil do hrobu i druhý učedník, všechno si prohlédl a uvěřil, že Ježíš vstal z mrtvých. Až dosud to totiž stejně jako ostatní nechápal.

Ježíš se zjevuje Marii z Magdaly

10Oba učedníci se vrátili zpět, 11ale Marie zůstala u hrobu a plakala. 12Náhle spatřila v hrobce dva anděly v bílém; seděli na obou koncích kamenné lavice, na níž předtím spočívalo Ježíšovo tělo.

13„Ženo, proč pláčeš?“ zeptali se jí.

„Vzali mého Pána a nevím, kam ho uložili.“

14Když to řekla, obrátila se a spatřila, že za ní někdo stojí. 15Neznámý ji oslovil: „Ženo, proč pláčeš? Koho hledáš?“

Myslela, že je to zahradník, a odpověděla: „Pane, jestli jsi ho odnesl, řekni mi, kam jsi ho uložil, a já ho pochovám.“

16Ježíš jí řekl: „Marie!“

Pohlédla na něj a řekla: „Můj Mistře!“ a poklekla před ním.

17„Nedotýkej se mne!“ varoval ji Ježíš, „ještě jsem se nevrátil k svému Otci. Běž a pověz bratřím, že odcházím k svému i vašemu Bohu a Otci.“ 18Marie Magdaléna vyhledala učedníky a řekla jim: „Viděla jsem Pána,“ a sdělila jim, co jí uložil.

Ježíš se zjevuje učedníkům za zavřenými dveřmi

19Téhož dne večer byli učedníci pohromadě za zamčenými dveřmi, protože se báli, že teď přijdou Židé na ně. Pojednou stál Ježíš mezi nimi a řekl: „Pokoj vám!“ 20Potom jim ukázal rány v rukou a v boku.

To byla radost pro učedníky, že zase vidí svého Pána! 21Ježíš opakoval: „Pokoj vám!“ a pokračoval: „Otec vyslal mne a já vysílám vás.“ 22Dýchl na ně a řekl: „Přijměte svatého Ducha! 23Komu budete zvěstovat odpuštění hříchů a kdo je přijme, tomu bude odpuštěno. Komu tu zvěst zadržíte, zůstává ve svém hříchu.“

Ježíš se zjevuje učedníkům včetně Tomáše

24Toho večera chyběl mezi učedníky Tomáš, kterému přezdívali Dvojče. 25Ostatní mu o setkání s Ježíšem vyprávěli, ale on pochyboval: „Neuvěřím, dokud neuvidím a neohmatám rány na jeho rukou a boku.“

26Po týdnu byli učedníci znovu spolu a tentokrát byl s nimi i Tomáš. Dveře byly zase zamčeny, když se Ježíš mezi ně postavil a oslovil je: „Pokoj vám!“ 27Potom se obrátil k Tomášovi: „Podívej se a sáhni si na mé rány! Už nepochybuj, ale věř!“

28Tomáš přesvědčen vyznal: „Jsi můj Pán a můj Bůh!“

29Ježíš mu na to řekl: „Viděl jsi mne, a proto věříš. Cennější však je nevidět a uvěřit.“

30-31Za dobu svého působení Ježíš před zraky učedníků vykonal mnoho dalších mocných činů, které nejsou v této knize zaznamenány. Ty činy, které jsou zaznamenány, ve vás mají vzbudit víru v Ježíše jako Božího Syna a zajistit vám tak věčný život.