Yohane 2 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 2:1-25

Yesu Asandutsa Madzi Kukhala Vinyo

1Pa tsiku lachitatu munali ukwati mu Kana wa ku Galileya. Amayi ake a Yesu anali komweko, 2ndipo Yesu ndi ophunzira ake anayitanidwanso ku ukwatiwo. 3Vinyo atatha, amayi a Yesu anati kwa Iye, “Wawathera vinyo.”

4Yesu anayankha kuti, “Amayi, chifukwa chiyani mukundiwuza Ine? Nthawi yanga sinakwane.”

5Amayi ake anati kwa antchito, “Inu muchite chilichonse chimene akuwuzeni.”

6Pamenepo panali mitsuko yamiyala yothiramo madzi isanu ndi umodzi, imene Ayuda amagwiritsa ntchito pa mwambo wodziyeretsa. Uliwonse unali ndi malita 100 kapena kupitirirapo.

7Yesu anati kwa antchitowo, “Dzazani madzi mʼmitsukoyi,” ndipo iwo anadzaza ndendende.

8Ndipo Iye anatinso kwa iwo, “Tsopano tungani ndipo kaperekeni kwa mkulu waphwando.”

Iwo anachita momwemo. 9Mkulu waphwando analawa madziwo amene anasandulika vinyo, ndipo sanazindikire kumene vinyoyo anachokera, ngakhale kuti antchito amene anatunga madziwo amadziwa. Kenaka anayitanira mkwati pambali 10ndipo anati, “Aliyense amatulutsa vinyo wokoma kwambiri poyambirira ndipo kenaka vinyo wosakoma pamene oyitanidwa atamwa kale wambiri; koma iwe wasunga wokoma mpaka tsopano.”

11Ichi chinali chizindikiro chodabwitsa choyamba chimene Yesu anachita ku Kana wa ku Galileya. Potero Iye anawulula ulemerero wake, ndipo ophunzira ake anamukhulupirira Iye.

Yesu Ayeretsa Nyumba ya Mulungu

12Zitatha izi Iye anatsikira ku Kaperenawo pamodzi ndi amayi ake, abale ake ndi ophunzira ake. Iwo anakhala kumeneko masiku owerengeka.

13Nthawi ya Paska ya Ayuda itayandikira, Yesu anapita ku Yerusalemu. 14Mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu Iye anapeza anthu akugulitsa ngʼombe, nkhosa ndi nkhunda ndipo ena akusintha ndalama pa matebulo. 15Chifukwa cha zimenezi Iye anapanga chikwapu cha zingwe ndipo anatulutsa onse mʼbwalo la Nyumbayo, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe; Iye anamwaza ndalama zawo ndi kugudubuza matebulo. 16Kwa amene amagulitsa nkhunda, Iye anati, “Tulutsani izi muno! Osasandutsa Nyumba ya Atate anga msika!”

17Ophunzira ake anakumbukira kuti zinalembedwa kuti, “Kudzipereka kwanga ku nyumba yanu kudzandiphetsa.”

18Kenaka Ayuda anamufunsa Yesu kuti, “Kodi mungationetse chizindikiro chodabwitsa chotani chotsimikizira ulamuliro wanu wochitira izi?”

19Yesu anawayankha kuti, “Gwetsani Nyumba ya Mulunguyi ndipo Ine ndidzayimanganso mʼmasiku atatu.”

20Ayuda anayankha kuti, “Zinatenga zaka makumi anayi kumanga Nyumbayi, kodi Inu mungayimange masiku atatu?” 21Koma Nyumba ya Mulungu imene amanena linali thupi lake. 22Iye ataukitsidwa kwa akufa, ophunzira ake anakumbukira zimene Iye ananena ndipo anakhulupirira Malemba ndi mawu amene Yesu anayankhula.

23Tsopano Iye ali mu Yerusalemu pa phwando la Paska, anthu ambiri anaona zizindikiro zodabwitsa zimene amachita ndipo anakhulupirira dzina lake. 24Koma Yesu sanawakhulupirire iwo, pakuti amadziwa anthu onse. 25Iye sanafune umboni wa wina aliyense popeza amadziwa zomwe zinali mʼmitima mwa anthu.

King James Version

John 2:1-25

1And the third day there was a marriage in Cana of Galilee; and the mother of Jesus was there: 2And both Jesus was called, and his disciples, to the marriage. 3And when they wanted wine, the mother of Jesus saith unto him, They have no wine. 4Jesus saith unto her, Woman, what have I to do with thee? mine hour is not yet come. 5His mother saith unto the servants, Whatsoever he saith unto you, do it. 6And there were set there six waterpots of stone, after the manner of the purifying of the Jews, containing two or three firkins apiece. 7Jesus saith unto them, Fill the waterpots with water. And they filled them up to the brim. 8And he saith unto them, Draw out now, and bear unto the governor of the feast. And they bare it. 9When the ruler of the feast had tasted the water that was made wine, and knew not whence it was: (but the servants which drew the water knew;) the governor of the feast called the bridegroom, 10And saith unto him, Every man at the beginning doth set forth good wine; and when men have well drunk, then that which is worse: but thou hast kept the good wine until now. 11This beginning of miracles did Jesus in Cana of Galilee, and manifested forth his glory; and his disciples believed on him.

12¶ After this he went down to Capernaum, he, and his mother, and his brethren, and his disciples: and they continued there not many days.

13¶ And the Jews’ passover was at hand, and Jesus went up to Jerusalem, 14And found in the temple those that sold oxen and sheep and doves, and the changers of money sitting: 15And when he had made a scourge of small cords, he drove them all out of the temple, and the sheep, and the oxen; and poured out the changers’ money, and overthrew the tables; 16And said unto them that sold doves, Take these things hence; make not my Father’s house an house of merchandise. 17And his disciples remembered that it was written, The zeal of thine house hath eaten me up.

18¶ Then answered the Jews and said unto him, What sign shewest thou unto us, seeing that thou doest these things? 19Jesus answered and said unto them, Destroy this temple, and in three days I will raise it up. 20Then said the Jews, Forty and six years was this temple in building, and wilt thou rear it up in three days? 21But he spake of the temple of his body. 22When therefore he was risen from the dead, his disciples remembered that he had said this unto them; and they believed the scripture, and the word which Jesus had said.

23¶ Now when he was in Jerusalem at the passover, in the feast day, many believed in his name, when they saw the miracles which he did. 24But Jesus did not commit himself unto them, because he knew all men, 25And needed not that any should testify of man: for he knew what was in man.