Yobu 7 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 7:1-21

1“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi?

Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?

2Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo,

kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,

3choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe,

ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.

4Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’

Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.

5Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera,

khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.

6“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu,

ndipo amatha wopanda chiyembekezo.

7Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya;

sindidzaonanso masiku achisangalalo.

8Amene akundiona tsopano akundiona;

mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.

9Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka,

momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera.

10Iye sadzabweranso ku nyumba kwake

ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.

11“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete;

ndidzayankhula mopsinjika mtima,

ndidzadandaula mowawidwa mtima.

12Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja

kuti inu mundiyikire alonda?

13Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga

ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,

14ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto

ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,

15kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa,

kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.

16Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse.

Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.

17“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere,

kuti muzisamala zochita zake,

18kuti muzimusanthula mmawa uliwonse

ndi kumamuyesa nthawi yonse?

19Kodi simudzaleka kumandizonda

kuti ndipezeko mpata wopumula?

20Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu,

Inu wopenyetsetsa anthu?

Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu?

Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?

21Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga

ndi kundichotsera machimo anga?

Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda;

mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”

La Bible du Semeur

Job 7:1-21

Pourquoi la souffrance ?

1Le sort de l’homme sur la terre ╵est celui d’un soldat

et ses jours sont semblables ╵à ceux d’un mercenaire.

2Il est comme un esclave ╵qui soupire après l’ombre7.2 C’est-à-dire le soir, qui apporte fraîcheur et repos après le travail du jour.

et comme un ouvrier ╵qui attend son salaire.

3J’ai reçu en partage ╵des mois de déception,

j’ai trouvé dans mon lot ╵des nuits de peine amère.

4Dès que je suis couché, je dis : ╵« Quand vais-je me lever ? »

Sitôt levé, je pense : ╵« Quand donc viendra le soir7.4 Sitôt levé… le soir: d’après l’ancienne version grecque ; le texte hébreu traditionnel a : le soir tarde à venir. ? »

Et, jusqu’au crépuscule, ╵je suis agité de douleurs.

5Mon corps est couvert de vermine ╵et de croûtes terreuses,

ma peau s’est crevassée, ╵partout, mes plaies suppurent.

6Mes jours se sont enfuis ╵plus rapides que la navette ╵d’un tisserand habile.

Ils tirent à leur fin ╵sans qu’il y ait d’espoir.

7Rappelle-toi, ô Dieu, ╵que ma vie n’est qu’un souffle

et que jamais mes yeux ╵ne reverront plus le bonheur.

8Oui, l’œil qui me regarde ╵ne pourra plus me voir,

tes yeux me chercheront ╵et j’aurai disparu.

9Tout comme une nuée ╵qui se dissipe et passe,

l’homme va dans la tombe7.9 Autre traduction : dans le séjour des morts. ╵pour n’en plus remonter.

10Il ne reviendra plus ╵dans sa maison

et sa demeure même ╵ne le reconnaît plus.

11C’est pourquoi je ne veux ╵plus réfréner ma langue,

je parlerai ╵dans ma détresse,

je me lamenterai ╵car mon cœur est amer.

12Suis-je donc une mer ╵ou un monstre marin

pour que tu établisses ╵contre moi, une garde7.12 Le monstre marin: image des puissances souvent hostiles à Dieu et pourtant domptées par le Seigneur (voir 3.8 et note). ?

13Si je me dis : ╵« Mon lit m’apaisera,

ma couche m’aidera ╵à porter ma douleur »,

14alors tu m’épouvantes ╵par d’affreux cauchemars

et tu me terrifies ╵par des visions nocturnes.

15J’aimerais mieux être étranglé,

la mort vaudrait bien mieux ╵que vivre dans ces os.

16Je suis plein de dégoût ! ╵Je ne durerai pas toujours.

Laisse-moi donc tranquille : ╵ma vie est si fragile.

17Qu’est-ce que l’homme, ╵pour que tu fasses ╵un si grand cas de lui,

et pour que tu lui prêtes ╵une telle attention,

18pour que tu l’examines ╵matin après matin,

et pour qu’à chaque instant ╵tu viennes l’éprouver ?

19Quand détourneras-tu ╵enfin tes yeux de moi ?

Ne lâcheras-tu pas ╵un instant ton étreinte, ╵ne fût-ce que le temps ╵d’avaler ma salive ?

20Et puis même si j’ai péché, ╵que t’ai-je fait, à toi, ╵censeur des hommes ?

Pourquoi donc m’as-tu pris pour cible ?

Suis-je devenu une charge7.20 D’après quelques manuscrits du texte hébreu traditionnel, une ancienne tradition de copistes et l’ancienne version grecque. La plupart des manuscrits du texte hébreu traditionnel ont : je suis devenu une charge pour moi-même. ?

21Pourquoi ne veux-tu pas ╵pardonner mon offense

et ne passes-tu pas ╵sur mon iniquité ?

Bientôt j’irai dormir ╵au sein de la poussière

et tu me chercheras, ╵mais je ne serai plus.