Yobu 40 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 40:1-24

1Yehova anati kwa Yobu:

2“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse?

Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”

3Pamenepo Yobu anayankha Yehova:

4“Ine sindili kanthu konse,

kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.

5Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho,

ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”

6Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,

7“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna;

ndikufunsa mafunso

ndipo iwe undiyankhe.

8“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama?

Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?

9Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu,

ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?

10Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola,

ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.

11Tsanula ukali wako wosefukirawo,

uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,

12Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse,

uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.

13Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi;

ukulunge nkhope zawo mʼmanda.

14Ukatero Ine ndidzakuvomereza

kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.

15“Taganiza za mvuwu,

imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe,

ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.

16Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri,

thupi lake ndi lanyonga kwambiri!

17Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza;

mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.

18Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa,

nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.

19Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu,

komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.

20Imapeza chakudya chake ku mtunda

ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.

21Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta,

imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.

22Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta;

imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.

23Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha,

iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.

24Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza

kapena kuyikola mu msampha?

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Job 40:1-24

1El Señor dijo también a Job:

2«¿Corregirá al Todopoderoso quien contra él contiende?

¡Que le responda a Dios quien se atreve a acusarlo!»

3Entonces Job le respondió:

4«¿Qué puedo responderte, si soy tan indigno?

¡Me tapo la boca con la mano!

5Hablé una vez, y no voy a responder;

hablé otra vez, y no voy a insistir».

6El Señor respondió a Job desde la tempestad. Le dijo:

7«Prepárate a hacerme frente.

Yo te preguntaré, y tú me responderás.

8»¿Vas acaso a invalidar mi justicia?

¿Me harás quedar mal para que tú quedes bien?

9¿Tienes acaso un brazo como el mío?

¿Puede tu voz tronar como la mía?

10Si es así, cúbrete de gloria y esplendor;

revístete de honra y majestad.

11Da rienda suelta a la furia de tu ira;

mira a los orgullosos, y humíllalos;

12mira a los soberbios, y somételos;

aplasta a los malvados donde se hallen.

13Entiérralos a todos en el polvo;

amortaja sus rostros en la fosa.

14Yo, por mi parte, reconoceré

que en tu mano derecha está la salvación.

15»Mira a Behemot,40:15 Behemot. Posiblemente se trata del hipopótamo o del elefante. criatura mía igual que tú,

que se alimenta de hierba, como los bueyes.

16¡Cuánta fuerza hay en sus lomos!

¡Su poder está en los músculos de su vientre!

17Su rabo se mece como un cedro;

los tendones de sus muslos se entrelazan.

18Sus huesos son como barras de bronce;

sus piernas parecen barrotes de hierro.

19Entre mis obras ocupa el primer lugar,

solo yo, su Hacedor, puedo acercarme a él con la espada.

20Los montes le brindan sus frutos;

allí juguetean todos los animales salvajes.

21Debajo de los cañaverales se tiende a descansar;

se oculta entre los juncos del pantano.

22Los lotos le brindan su sombra;

los álamos junto al río lo envuelven.

23No se alarma si brama el río;

vive tranquilo aunque el Jordán le llegue al hocico.

24¿Quién ante sus ojos se atreve a capturarlo?

¿Quién puede atraparlo y perforarle la nariz?