Yobu 4 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 4:1-21

Mawu a Elifazi

1Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

2“Ngati wina atakuyankha, kodi ungakhumudwe?

Koma ndani angakhale chete wosayankhula?

3Taganiza momwe iwe walangizira anthu ambiri,

momwe walimbitsira anthu ofowoka.

4Mawu ako analimbitsa anthu ofuna kugwa;

unachirikiza anthu wotha mphamvu.

5Koma tsopano mavuto akufikira ndipo wataya mtima,

zakukhudza ndipo uli ndi mantha.

6Kodi kuopa Mulungu kwako sindiko kulimbika mtima kwako?

Ndipo moyo wako wosalakwa ndiye chiyembekezo chako?

7“Ganiza bwino tsopano: Kodi munthu wosalakwa anawonongekapo nʼkale lonse?

Nʼkuti kumene munthu wolungama mtima anaphedwa?

8Monga ndaonera ine, anthu amene amatipula zoyipa,

ndi iwo amene amadzala mavuto, amakolola zomwezo.

9Iwo amaphedwa ndi mpweya wa Mulungu;

amawonongeka ndi mpweya waukali wa mkwiyo wake.

10Mikango imabangula ndi kulira,

komabe mano a mikango yamphamvu amathyoledwa.

11Mkango umafa chifukwa chosowa nyama,

ndipo ana amkango amamwazikana.

12“Mawu anabwera kwa ine mwamseri,

makutu anga anamva kunongʼona kwake.

13Mʼkati mwa maloto ochititsa mantha usiku,

nthawi imene anthu amagona tulo tofa nato,

14ndinagwidwa ndi mantha, ndi kuyamba kunjenjemera

ndipo mafupa anga onse anaweyeseka.

15Pamenepo mzimu unadutsa pamaso panga,

ndipo ubweya wa pa thupi langa unayima kuti njoo.

16Chinthucho chinayimirira

koma sindinathe kuzindikira kuti chinali chiyani.

Chinthu chinayima patsogolo panga,

kunali zii ndipo ndinamva mawu akuti,

17‘Kodi munthu angathe kukhala wolungama kupambana Mulungu?

Kodi munthu angathe kukhala wangwiro kupambana Mlengi wake?

18Ngati Mulungu sakhulupirira atumiki ake omwe,

ngati Iye amawapeza angelo ake ndi cholakwa,

19nanga kuli bwanji ndi iwo amene amakhala mʼnyumba zadothi,

amene maziko awo ndi fumbi,

amene amathudzuka mosavuta ngati kadziwotche!

20Mmawa ali moyo, pofika madzulo afa;

mwakachetechete, amawonongeka kwamuyaya.

21Kodi zonse zimene ali nazo sizimatheratu,

kotero kuti amafa osadziwa nʼkanthu komwe?’

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 4:1-21

以利法的责难

1提幔以利法回答说:

2“若有人向你进言,

你会厌烦吗?

可是,谁能忍住不说呢?

3你曾教导许多人,

使无力的手强壮。

4你的话使人免于跌倒,

你使颤抖的膝硬朗。

5但现在苦难一来,

你便灰心丧胆;

灾祸来临,

你便惊慌失措。

6你敬畏上帝还没有信心吗?

你行为纯全还没有盼望吗?

7你想一想,

哪有无辜的人灭亡?

哪有正直的人遭殃?

8据我所见,

播恶收恶,

种祸得祸。

9他们被上帝的气息所毁,

被上帝的怒气所灭。

10狮子咆哮,猛狮吼叫,

壮狮的牙齿被敲掉。

11雄狮因无食而死,

母狮的幼崽离散。

12“有信息暗暗地传给我,

一声低语传入我耳中。

13夜间人们沉睡的时候,

在搅扰思绪的异象中,

14恐惧袭来,

令我战栗不已,

全身发抖。

15有灵从我脸上拂过,

使我毛骨悚然。

16那灵停住,

我无法辨认其模样。

眼前出现一个形状,

寂静中听见有声音说,

17‘在上帝面前,世人岂算得上公义?

在创造主面前,凡人岂算得上纯洁?

18连上帝的仆人都无法令祂信任,

连祂的天使都被祂找出过错,

19更何况源自尘土、

住在土造的躯壳里、

脆弱如蛾的世人呢?

20早晚之间,他们便被毁灭,

永远消逝,无人察觉。

21他们帐篷的绳索被拔起,

他们毫无智慧地死去。’