Yobu 35 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 35:1-16

1Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,

2“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza?

Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’

3Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani,

ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’

4“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu

pamodzi ndi abwenzi anu omwe.

5Yangʼanani kumwamba ndipo muone

mitambo imene ili kutali ndi inuyo.

6Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani?

Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?

7Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani?

Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?

8Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo,

ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.

9“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa;

akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.

10Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga,

amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,

11amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi

ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’

12Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye

chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.

13Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake;

Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.

14Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti

Iye saona zimene zikuchitika.

Iye adzaweruza molungama ngati

inu mutamudikira

15ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango,

zoyipa zambiri zimene anthu amachita,

16abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake,

mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约伯记 35:1-16

1以利户又说:

2“你在上帝面前自以为义,

你认为这合理吗?

3你还说,‘这与我何干?

我不犯罪又有何益处?’

4我要答复你和你的朋友。

5要抬头观看诸天,

瞻望头顶的穹苍。

6你若犯罪,与上帝何妨?

你若罪恶累累,对祂有何影响?

7你若为人公义,与祂何益?

祂从你手上能得什么好处?

8你的罪恶只能伤害你的同类,

你的公义只能令世人受益。

9“人们因饱受压迫而呼求,

因强权者的压制而求救。

10但无人问,‘创造我的上帝在哪里?

祂使人夜间欢唱,

11使我们比地上的走兽聪明,

比天上的飞鸟有智慧。’

12他们因恶人的嚣张而呼求,

上帝却不回答。

13上帝必不垂听虚妄的呼求,

全能者必不理会。

14更何况你说你看不见祂,

你的案子已呈上,在等祂裁决。

15你还说祂没有发怒降罚,

也不理会罪恶。

16约伯啊,这尽是虚言,

是一大堆无知的话。”