Yobu 33 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 33:1-33

1“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga;

mutcherere khutu zonse zimene ndinene.

2Tsopano ndiyamba kuyankhula;

mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.

3Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama;

pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.

4Mzimu wa Mulungu wandiwumba,

mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.

5Mundiyankhe ngati mungathe;

konzekani tsopano kuti munditsutse.

6Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu;

nanenso ndinachokera ku dothi.

7Musachite mantha ndipo musandiope ayi,

Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.

8“Koma inu mwayankhula ine ndikumva,

ndamva mawu anuwo onena kuti,

9‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo;

ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.

10Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo;

Iye akundiyesa ngati mdani wake.

11Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo,

akulonda mayendedwe anga onse.’

12“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi,

pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.

13Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye

kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?

14Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana,

ngakhale munthu sazindikira zimenezi.

15Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku,

pamene anthu ali mʼtulo tofa nato

pamene akungosinza chabe pa bedi,

16amawanongʼoneza mʼmakutu

ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,

17kumuchotsa munthu ku zoyipa,

ndi kuthetseratu kunyada kwake,

18kumulanditsa munthu ku manda,

kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.

19“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake,

nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,

20kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya,

ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.

21Thupi lake limawonda

ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.

22Munthuyo amayandikira ku manda,

moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.

23“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi,

mmodzi mwa ambirimbiri oterewa,

adzafotokoza zimene zili zoyenera,

24kudzamukomera mtima ndi kunena kuti,

‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda;

ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’

25pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana;

ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.

26Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa.

Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe

ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.

27Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti,

‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama,

koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.

28Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda,

ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’

29“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu

kawirikawiri,

30kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda,

kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.

31“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere;

khalani chete kuti ndiyankhule.

32Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni;

yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.

33Koma ngati sichoncho, mundimvere;

khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

Het Boek

Job 33:1-33

Elihu wijst Job terecht

1‘Luister alstublieft naar wat ik te zeggen heb, Job.

2Laat mij uitspreken, nu ik eenmaal het woord heb genomen.

3Ik zal in alle oprechtheid de waarheid spreken.

4De Geest van God heeft mij namelijk gemaakt en de adem van de Almachtige geeft mij leven.

5Aarzel niet mij een antwoord te geven als u dat kunt.

6Voor God ben ik volkomen gelijk aan u. Ik ben ook uit de aarde gevormd, net als u.

7U hoeft niet bang voor mij te zijn. Ik ben er niet de man naar u in het nauw te drijven.

8Ik heb u steeds weer horen zeggen:

9“Ik ben rein, ik heb niet gezondigd, ik ben onschuldig.

10En toch heeft God aanmerkingen op mij en beschouwt mij als zijn vijand.

11Hij legt ketens om mijn enkels en kijkt scherp naar elke beweging die ik maak.”

12Juist hierin hebt u ongelijk, dat u op deze wijze over God spreekt. Want God is veel groter dan de mens.

13Waarom klaagt u bij God dat Hij niet antwoordt?

14God spreekt wel degelijk—nu op de ene, dan op de andere wijze—hoewel de mens dat misschien niet opmerkt.

15Bijvoorbeeld in dromen en in nachtelijke visioenen als een diepe slaap komt over mensen die op bed liggen.

16Op zulke ogenblikken opent Hij hun oren en waarschuwt Hij hen

17-18 zodat zij van gedachten veranderen en ervoor zorgen niet trots te worden. Zij worden gewaarschuwd voor de straf op de zonde en leren goed op te letten dat zij niet op een of andere manier omkomen.

19God kan een mens echter ook terechtwijzen door een ziekte, zodat hij met voortdurende pijn in zijn botten in bed moet blijven

20en hij zijn eetlust verliest en zelfs voor het heerlijkste gerecht zijn neus optrekt.

21-22 Hij wordt broodmager en komt steeds dichter bij de afgrond en de machten van de dood.

23-24 Maar als een boodschapper uit de hemel aanwezig is die als voorspraak dient, een uit duizend die het als een vriend voor hem opneemt, dan zal Hij Zich over hem ontfermen en zeggen: “Maak hem vrij, hij zal niet sterven. Er is voor hem een losgeld betaald.”

25Dan zal zijn lichaam weer zo gezond worden als dat van een kind, fris en jeugdig.

26En als hij tot God bidt, zal God naar hem luisteren en hem antwoorden. Hij zal vreugde ervaren als hij het gezicht van de Here weer ziet en zijn rechtvaardigheid weer terugkrijgt.

27Tegen zijn vrienden zal hij later zeggen: “Ik had gezondigd, maar God gaf mij niet de straf die ik had verdiend.

28Hij liet mij niet sterven. Ik zal voortaan leven en veel meer van het licht genieten.”

29Ja, God doet vaak zulke dingen met de mens,

30tweemaal, zelfs driemaal zijn ziel terughalen uit de grafkuil, zodat hij het levenslicht kan blijven genieten.

31Let daar goed op, Job. Luister naar wat ik nog meer te zeggen heb.

32Maar als u nu al iets wilt zeggen, ga uw gang. Want ik zou zo graag willen dat uw onschuld wordt bewezen.

33Maar zo niet, luister dan naar mij. Houdt u stil, terwijl ik u wijsheid leer!’