Yobu 3 – CCL & TCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 3:1-26

Mawu a Yobu

1Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa. 2Ndipo Yobu anati:

3“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe

ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’

4Tsiku limenelo lisanduke mdima;

Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso;

kuwala kusaonekenso pa tsikulo.

5Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli;

mtambo uphimbe tsikuli;

mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.

6Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani;

usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka,

kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.

7Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino;

kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.

8Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo,

iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.

9Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima;

tsikulo liyembekezere kucha pachabe

ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.

10Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga

ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.

11“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa

ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?

12Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo

ndi mawere woti andiyamwitsepo?

13Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere;

ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo

14pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi,

amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,

15pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide,

amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.

16Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale,

ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?

17Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto,

ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.

18A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere;

sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.

19Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko,

ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.

20“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto,

ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,

21kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera,

amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,

22amene amakondwa ndi kusangalala

akamalowa mʼmanda?

23Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu

amene njira yake yabisika,

amene Mulungu wamuzinga ponseponse?

24Mʼmalo moti ndidye, ndimalira,

ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.

25Chimene ndinkachiopa chandigwera;

chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.

26Ndilibe mtendere kapena bata,

ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”

Tagalog Contemporary Bible

Job 3:1-26

Nagsalita si Job

1Kinalaunan, nagsalita si Job at isinumpa niya ang araw na isinilang siya. 2Sinabi niya, 3“Isinusumpa ko ang araw na akoʼy ipinanganak. 4Naging madilim na lang sana ang araw na iyon at hindi na sinikatan ng araw. Kinalimutan na lang sana ng Dios sa langit ang araw na iyon. 5Nanatili na lang sana itong madilim o natatakpan ng makapal na ulap, at nilukuban na lang sana ng kadiliman ang kaliwanagan. 6Kinuha na lang sana ng kadiliman ang gabing iyon nang akoʼy isilang, at hindi na sana napabilang sa kalendaryo. 7Hindi na nga lang sana ako ipinanganak ng gabing iyon, at wala rin sanang kasayahan noon. 8Sumpain nawa ang gabing iyon ng mga manunumpa na alam kung paano pakilusin ang Leviatan.3:8 Leviatan: Maaaring dambuhalang hayop, buwaya, ahas, o balyena. 9Hindi na sana sumikat ang tala sa umaga ng araw na iyon, at hindi na sana dumating ang bukang-liwayway. 10Isinusumpa ko ang araw na iyon dahil hindi niya pinigilan ang pagsilang sa akin, nang hindi ko na sana naranasan ang ganitong paghihirap.

11“Mabuti pang namatay na lang ako sa sinapupunan ng aking ina. 12Bakit pa ako kinalingaʼt pinasuso ng aking ina? 13Kung namatay na sana ako noon, tahimik na sana ako ngayong natutulog at nagpapahinga 14kasama ng mga hari at mga pinuno ng mundo na nagtayo ng mga palasyo3:14 palasyo: o, gusali. na giba na ngayon.3:14 giba na ngayon: o, na muling itatayo. 15Nagpapahinga na rin sana ako kasama ng mga pinuno na ang mga tahanan ay puno ng mga gintoʼt pilak. 16Mas mabuti pang akoʼy naging katulad ng mga batang patay na nang ipinanganak at hindi na nakakita ng liwanag. 17Doon sa lugar ng mga patay, ang masama ay hindi na gumagawa ng kasamaan at ang mga pagod ay nagpapahinga na. 18Doon, ang mga bihag ay nagpapahinga rin at hindi na nila naririnig ang sigaw ng taong pumipilit sa kanila na magtrabaho. 19Naroon ang lahat ng uri ng tao, tanyag man o hindi. At ang mga alipin ay malaya na sa kanilang amo.

20“Bakit pa pinapayagang mabuhay ang taong nagtitiis at nagdurusa? 21Nagnanais silang mamatay pero hindi pa rin sila namamatay. Hangad nila ang kamatayan ng higit pa sa isang taong naghahanap ng nakatagong kayamanan. 22Mas sasaya sila kapag namatay na at nailibing. 23Bakit kaya niloob pa ng Dios na mabuhay ang tao nang hindi man lamang pinapaalam ang kanyang kahahantungan? 24Hindi ako makakain dahil sa labis na pagdaramdam at walang tigil ang aking pagdaing. 25Ang kinatatakutan koʼy nangyari sa akin. 26Wala akong kapayapaan at katahimikan. Wala akong kapahingahan, pawang kabagabagan ang nararanasan ko.”