Yobu 3 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 3:1-26

Mawu a Yobu

1Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa. 2Ndipo Yobu anati:

3“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe

ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’

4Tsiku limenelo lisanduke mdima;

Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso;

kuwala kusaonekenso pa tsikulo.

5Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli;

mtambo uphimbe tsikuli;

mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.

6Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani;

usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka,

kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.

7Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino;

kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.

8Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo,

iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.

9Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima;

tsikulo liyembekezere kucha pachabe

ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.

10Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga

ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.

11“Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa

ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?

12Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo

ndi mawere woti andiyamwitsepo?

13Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere;

ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo

14pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi,

amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,

15pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide,

amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.

16Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale,

ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?

17Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto,

ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.

18A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere;

sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.

19Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko,

ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.

20“Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto,

ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,

21kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera,

amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,

22amene amakondwa ndi kusangalala

akamalowa mʼmanda?

23Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu

amene njira yake yabisika,

amene Mulungu wamuzinga ponseponse?

24Mʼmalo moti ndidye, ndimalira,

ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.

25Chimene ndinkachiopa chandigwera;

chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.

26Ndilibe mtendere kapena bata,

ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”

Hoffnung für Alle

Hiob 3:1-26

Auseinandersetzung zwischen Hiob und seinen Freunden

(Kapitel 3–28)

Warum muss ich noch leben?

1Dann erst begann Hiob zu sprechen. Er verfluchte den Tag seiner Geburt 2und sagte:

3»Ausgelöscht sei der Tag,

an dem ich geboren wurde,

und auch die Nacht,

in der man sagte: ›Es ist ein Junge!‹.

4Jener Tag versinke in tiefer Finsternis –

kein Licht soll ihn erhellen!

Selbst Gott da oben vergesse ihn!

5Ja, der Tod soll ihn holen – diesen Tag!

Ich wünschte, dass sich dunkle Wolken auf ihn legten

und die Finsternis sein Licht erstickte!

6Für immer soll sie dunkel bleiben –

die Nacht meiner Geburt!

Ausgelöscht sei sie aus dem Jahreskreis,

nie wieder erscheine sie auf dem Kalender!

7Stumm und öde soll sie sein,

eine Nacht, in der sich keiner mehr freut!

8Verfluchen sollen sie die Zauberer,

die Tag und Nacht verwünschen können

und die den Leviatan3,8 Bildhafte Redeweise für gottfeindliche Schicksalsmächte., dieses Ungeheuer, wecken!

9Jene Nacht soll finster bleiben,

ohne alle Sternenpracht!

Vergeblich warte sie aufs Sonnenlicht,

die Strahlen des Morgenrots sehe sie nicht!

10Denn sie ließ zu, dass meine Mutter mich empfing,

die Mühen des Lebens hat sie mir nicht erspart.

11Warum bin ich nicht bei der Geburt gestorben,

als ich aus dem Leib meiner Mutter kam?

12Wozu hat sie mich auf den Knien gewiegt

und an ihrer Brust gestillt?

13Wenn ich tot wäre,

dann läge ich jetzt ungestört,

hätte Ruhe und würde schlafen,

14so wie die Könige und ihre Berater,

die sich hier prachtvolle Paläste bauten – längst zu Ruinen zerfallen –,

15und wie die Herrscher,

die Gold und Silber besaßen

und ihre Häuser damit füllten.

16Warum wurde ich nicht wie eine Fehlgeburt verscharrt,

wie Totgeborene, die nie das Tageslicht sahen?

17Bei den Toten können die Gottlosen nichts mehr anrichten,

und ihre Opfer haben endlich Ruhe.

18Auch die Gefangenen lässt man dort in Frieden;

sie hören nicht mehr das Geschrei des Aufsehers.

19Ob groß oder klein: Dort sind alle gleich,

und der Sklave ist seinen Herrn los.

20Warum nur lässt Gott die Menschen leben?

Sie mühen sich ab, sind verbittert und ohne Hoffnung.

21Sie sehnen sich den Tod herbei –

aber er kommt nicht!

Sie suchen ihn mehr als verborgene Schätze,

22und erst wenn sie endlich im Grab ruhen,

empfinden sie die größte Freude!

23Warum muss ich noch leben?

Gott hat mich eingepfercht;

ich sehe nur noch Dunkelheit!

24Schmerzensschreie sind mein tägliches Brot,

und das Stöhnen bricht aus mir heraus.

25Meine schlimmsten Befürchtungen sind eingetroffen,

und wovor mir immer graute – das ist jetzt da!

26Ohne Ruhe und Frieden lebe ich dahin,

getrieben von endloser Qual!«