Yobu 27 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 27:1-23

1Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:

2“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama,

Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,

3nthawi zonse pamene ndili ndi moyo,

mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,

4pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa,

lilime langa silidzayankhula zachinyengo.

5Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona;

mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.

6Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere;

chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.

7“Mdani wanga akhale ngati woyipa,

wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!

8Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa,

pamene Mulungu achotsa moyo wake?

9Kodi Mulungu amamva kulira kwake

pamene zovuta zamugwera?

10Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse?

Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?

11“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo

sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.

12Inu mwadzionera nokha zonsezi.

Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?

13“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa,

cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.

14Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo

zidzukulu zake zidzasowa zakudya.

15Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri,

ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.

16Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi,

ndi kukundika zovala ngati mchenga,

17zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale,

ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.

18Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche,

ili ngati msasa umene mlonda amamanga.

19Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko;

akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.

20Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula;

mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.

21Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo

imamuchotsa pamalo pake.

22Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni,

pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.

23Mphepoyo imamuwomba ndithu

ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”

Nova Versão Internacional

Jó 27:1-23

1E Jó prosseguiu em seu discurso:

2“Pelo Deus vivo, que me negou justiça,

pelo Todo-poderoso, que deu amargura à minha alma,

3enquanto eu tiver vida em mim,

o sopro de Deus em minhas narinas,

4meus lábios não falarão maldade,

e minha língua não proferirá nada que seja falso.

5Nunca darei razão a vocês!

Minha integridade não negarei jamais, até a morte.

6Manterei minha retidão e nunca a deixarei;

enquanto eu viver, a minha consciência não me repreenderá.

7“Sejam os meus inimigos como os ímpios,

e os meus adversários como os injustos!

8Pois, qual é a esperança do ímpio, quando é eliminado,

quando Deus lhe tira a vida?

9Ouvirá Deus o seu clamor

quando vier sobre ele a aflição?

10Terá ele prazer no Todo-poderoso?

Chamará a Deus a cada instante?

11“Eu os instruirei sobre o poder de Deus;

não esconderei de vocês os caminhos do Todo-poderoso.

12Pois a verdade é que todos vocês já viram isso.

Então por que essa conversa sem sentido?

13“Este é o destino que Deus determinou para o ímpio,

a herança que o mau recebe do Todo-poderoso:

14Por mais filhos que o ímpio tenha,

o destino deles é a espada;

sua prole jamais terá comida suficiente.

15A epidemia sepultará aqueles que lhe sobreviverem,

e as suas viúvas não chorarão por eles.

16Ainda que ele acumule prata como pó

e amontoe roupas como barro,

17o que ele armazenar ficará para os justos,

e os inocentes dividirão sua prata.

18A casa que ele constrói é como casulo de traça,

como cabana feita pela sentinela.

19Rico ele se deita, mas nunca mais o será!

Quando abre os olhos, tudo se foi.

20Pavores vêm sobre ele como uma enchente;

de noite a tempestade o leva de roldão.

21O vento oriental o leva, e ele desaparece;

arranca-o do seu lugar.

22Atira-se contra ele sem piedade,

enquanto ele foge às pressas do seu poder.

23Bate palmas contra ele

e com assobios o expele do seu lugar.