Yobu 20 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 20:1-29

Mawu a Zofari

1Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti

2“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe

chifukwa ndasautsidwa kwambiri.

3Ndikumva kudzudzula kondinyoza,

ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.

4“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale,

kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,

5kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha,

chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.

6Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba

ndipo mutu wake uli nengʼaa,

7iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe;

iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’

8Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso,

adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.

9Diso limene linamuona silidzamuonanso;

sadzapezekanso pamalo pake.

10Ana ake adzabwezera zonse

zimene iyeyo analanda anthu osauka;

11Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake

zidzagona naye limodzi mʼfumbi.

12“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake

ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,

13ngakhale salola kuzilavula,

ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,

14koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake;

chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.

15Adzachisanza chuma chimene anachimeza;

Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.

16Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo

ululu wa mphiri udzamupha.

17Sadzasangalala ndi timitsinje,

mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.

18Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya;

sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.

19Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo;

iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.

20“Chifukwa choti umbombo wake sutha,

sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.

21Palibe chatsala kuti iye adye;

chuma chake sichidzachedwa kutha.

22Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera;

mavuto aakulu adzamugwera.

23Akadya nʼkukhuta,

Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto

ngati mvula yosalekeza.

24Ngakhale athawe mkondo wachitsulo,

muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.

25Muviwo adzawutulutsira ku msana,

songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake.

Adzagwidwa ndi mantha aakulu;

26mdima wandiweyani ukudikira chuma chake.

Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza

ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.

27Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake;

dziko lapansi lidzamuwukira.

28Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake,

katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.

29Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa,

mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約伯記 20:1-29

瑣法再度發言

1拿瑪瑣法回答說:

2「我感到煩躁不安,

心中有話不吐不快。

3我聽見你侮辱我的斥責,

我的理智催促我回答。

4難道你不知道,從古至今,

自從世上有人以來,

5惡人得勢不會長久,

不信上帝者的快樂轉瞬即逝?

6雖然他傲氣沖天,

把頭挺到雲端,

7終必如自己的糞便永遠消亡,

見過他的人都不知他在何處。

8他如夢消逝,蹤影杳然;

如夜間的異象,飛逝而去。

9見過他的人不會再見到他,

他將從家鄉消失無蹤。

10他的兒女要向窮人乞憐,

他要親手償還不義之財。

11他的筋骨依然強健,

卻要隨他葬入塵土。

12「他以邪惡為甘飴,

將其藏在舌下,

13含在口中,

慢慢品味。

14這食物在腹中變酸,

變成了蛇的毒液。

15他要吐出所吞下的財富,

上帝要倒空他腹中之物。

16他吸吮蛇的毒液,

被蛇的舌頭害死。

17他無法享用流淌不盡的奶與蜜。

18他留不住勞碌的成果,

無法享用所賺的財富。

19他欺壓、漠視窮人,

強佔別人的房屋。

20他貪慾無度,

不放過任何喜愛之物。

21他吞掉一切所有,

他的福樂不能長久。

22他在富足時將陷入困境,

各種災禍將接踵而至。

23上帝的怒火如雨降在他身上,

填滿他的肚腹。

24他躲過了鐵刃,

卻被銅箭射穿。

25利箭穿透他的後背,

閃亮的箭頭刺破他的膽囊,

恐怖籠罩著他。

26他的財寶消失在幽冥中,

天火20·26 天火」希伯來文是「非人手點燃的火」。要吞噬他,

焚毀他帳篷中殘留的一切。

27天要揭露他的罪惡,

地要站出來指控他。

28在上帝發烈怒的日子,

洪流將席捲他的家產。

29這便是上帝為惡人定下的結局,

為他們預備的歸宿。」