Yobu 17 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 17:1-16

1“Mtima wanga wasweka,

masiku anga atha,

manda akundidikira.

2Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira;

maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.

3“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna.

Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?

4Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu;

choncho simudzawalola kuti apambane.

5Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma,

ana ake sadzaona mwayi.

6“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense,

munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.

7Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni;

ndawonda ndi mutu womwe.

8Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi;

anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.

9Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo,

ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.

10“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo,

sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.

11Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka,

pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.

12Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana,

nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’

13Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda,

ngati ndiyala bedi langa mu mdima,

14ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’

ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’

15tsono chiyembekezo changa chili kuti?

Ndani angaone populumukira panga?

16Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse,

polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.”

Hoffnung für Alle

Hiob 17:1-16

Ich habe keine Hoffnung mehr!

1»Meine Kraft ist gebrochen,

meine Tage schwinden,

und auf mich wartet nur das Grab.

2Ich muss mit ansehen,

wie man mich verspottet;

von allen Seiten werde ich bedrängt.

3O Gott, bürge du selbst für mich!

Ich habe sonst keinen, der für mich eintritt!

4Meinen Freunden hast du jede Einsicht verschlossen,

darum wirst du sie nicht triumphieren lassen.

5Sie gleichen jenem Mann im Sprichwort,

der sein Vermögen an viele Freunde verteilt

und seine eigenen Kinder hungern lässt.

6Ich bin dem Spott der Leute preisgegeben,

ja, man spuckt mir ins Gesicht!

7Schmerz und Trauer haben mich fast blind gemacht;

ich bin nur noch ein Schatten meiner selbst.

8Darüber sind aufrichtige Menschen hell entsetzt;

sie, die ein reines Gewissen haben, denken über mich:

›Wie gottlos muss der sein!‹

9Und doch gehen sie ihren geraden Weg unbeirrbar weiter;

sie, die schuldlos sind, bekommen neue Kraft.

10Kommt nur alle wieder her, ihr Freunde,

ich finde dennoch keinen Weisen unter euch!

11Ach, meine Tage sind verflogen,

durchkreuzt sind alle Pläne,

die einst mein Herz erfüllten!

12Meine Freunde erklären meine Nacht zum Tag!

›Das Licht ist nahe!‹, sagen sie,

während ich ins Finstere starre!

13Ich habe nur noch das Grab zu erwarten;

in der dunklen Welt der Toten muss ich liegen.

14Das Grab werde ich bald als ›Vater‹ begrüßen.

Die Verwesung nenn ich ›meine Mutter, liebe Schwester‹.

15Wo ist meine Hoffnung geblieben, wo denn?

Sieht jemand von ihr auch nur einen Schimmer?

16O nein, auch sie versinkt mit mir im Tode,

gemeinsam werden wir zu Staub!«