Yobu 15 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 15:1-35

Mawu a Elifazi

1Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

2“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere,

kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?

3Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake,

kapena kuyankhula mawu opanda phindu?

4Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu

ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.

5Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo;

ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.

6Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga;

milomo yakoyo ikukutsutsa.

7“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa?

Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?

8Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu?

Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?

9Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa?

Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?

10Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu,

anthu amvulazakale kupambana abambo ako.

11Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira,

mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?

12Chifukwa chiyani ukupsa mtima,

ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,

13moti ukupsera mtima Mulungu

ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?

14“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima

kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?

15Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake,

ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,

16nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota,

amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.

17“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera;

ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,

18zimene anandiphunzitsa anthu anzeru,

sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.

19(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa

pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).

20Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake,

munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.

21Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake,

pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.

22Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa;

iyeyo ndi woyenera kuphedwa.

23Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya;

amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.

24Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri;

zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,

25chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu

ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.

26Amapita mwa mwano kukalimbana naye

atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.

27“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa

ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,

28munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka

ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu,

nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.

29Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa,

ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.

30Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo;

lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake,

ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.

31Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe,

pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.

32Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane,

ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.

33Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse,

adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.

34Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala

ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.

35Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa;

mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”

Hoffnung für Alle

Hiob 15:1-35

Elifas: Du zerstörst die Ehrfurcht vor Gott!

1Da antwortete Elifas aus Teman:

2»Und du willst ein weiser Mann sein, Hiob?

Leere Worte! Du machst nichts als leere Worte!15,2 Wörtlich: Darf ein Weiser mit windigem Wissen antworten und seinen Bauch mit Ostwind füllen?

3Kein Weiser würde so reden wie du!

Wie du dich wehrst und zurückschlägst!

Das ist doch völlig nutzlos!

Was du sagst, hat keinen Wert!

4Wenn du so weitermachst,

wird niemand mehr Ehrfurcht vor Gott haben,

niemand wird sich noch auf ihn besinnen.

5Hinter vielen Worten willst du deine Schuld verstecken,

listig lenkst du von ihr ab!

6Ich muss dich gar nicht schuldig sprechen –

du selbst tust es;

jedes deiner Worte klagt dich an.

7Bist du als erster Mensch geboren worden,

noch ehe Gott die Berge schuf?

8Hast du etwa Gottes geheime Beratungen belauscht und kennst seine Pläne?

Du meinst wohl, du hast die Weisheit gepachtet!

9Was weißt du denn, das wir nicht auch schon wüssten;

was du begriffen hast, begreifen wir schon längst!

10Hinter uns stehen alte, weise Männer,

die älter wurden als dein Vater.

11Hiob, Gott will dich trösten!

Ist dir das gar nichts wert?

Durch uns redet er dich freundlich an.

12Was erlaubst du dir!

Du lässt dich vom Ärger mitreißen,

aus deinen Augen sprüht der Zorn;

13so ziehst du gegen Gott zu Felde

und klagst ihn erbittert an!

14Welcher Mensch ist wirklich schuldlos,

wer kann vor Gott bestehen?

15Selbst seinen Engeln vertraut Gott nicht,

in seinen Augen ist sogar der Himmel unvollkommen.

16Wie viel mehr die Menschen:

Abscheulich und verdorben sind sie,

am Unrecht trinken sie sich satt,

als wäre es Wasser!

17Hör mir zu, Hiob!

Ich will dir etwas erklären, was ich aus eigener Erfahrung weiß,

18es stimmt auch mit den Worten der alten, weisen Männer überein.

Sie wiederum haben es von ihren Vätern gelernt,

19denen damals das Land ganz allein gehörte,

von jedem fremden Einfluss unberührt15,19 Wörtlich: kein Fremder war unter ihnen umhergezogen..

20Sie sagten: Der Gewalttäter zittert vor Angst,

er, der von Gott nichts wissen wollte,

hat nicht mehr lange zu leben.

21Schreckensrufe gellen ihm in den Ohren,

mitten im Frieden wird ihn der Attentäter überfallen.

22Er glaubt nicht mehr,

dass er der Finsternis entkommen wird.

Das Schwert des Mörders wartet schon auf ihn.

23Auf der Suche nach Nahrung irrt er umher,

aber findet nichts.

Er weiß, dass bald sein letztes Stündlein schlägt.

24Ihn packt das Grauen,

Verzweiflung überfällt ihn wie ein König,

der zum Angriff bläst.

25Denn er hat Gott mit der Faust gedroht

und wagte es, den Allmächtigen zu bekämpfen.

26Starrköpfig, wie er war,

rannte er gegen Gott an

mit seinem runden, dicken Schild.

27Ja, er fühlte sich stark,

wurde selbstsicher und überheblich,15,27 Wörtlich: Er hat sein Gesicht mit Fett bedeckt und an den Hüften Fett angesetzt.

28aber er wird an verwüsteten Orten hausen,

in halb zerfallenen Häusern,

in denen es keiner mehr aushält,

die bald nur noch Ruinen sind.

29Dieser Mensch wird seinen Reichtum nicht behalten,

und sein Besitz ist nur von kurzer Dauer.

30Der Finsternis wird er nicht entrinnen;

er ist wie ein Baum,

dessen Zweige das Feuer versengt.

Gott spricht nur ein Wort,

und schon ist er nicht mehr da.

31Wenn er auf Werte vertraut,

die nicht tragen,

betrügt er sich selbst,

nur Enttäuschung wird sein Lohn sein.

32Früher, als er denkt,

wird Gottes Vergeltung ihn treffen.

Dann verwelkt er und wird nie wieder grünen.

33Er gleicht einem Weinstock,

der die Trauben verliert,

und einem Ölbaum,

der seine Blüten abwirft.

34So geht es allen, die Gott missachten:

Über kurz oder lang sterben sie aus.

Mit Bestechungsgeldern bauen sie ihr Haus,

aber ein Feuer wird alles verwüsten.

35Sie tragen sich mit bösen Plänen,

Gemeinheiten brüten sie aus

und setzen Unheil in die Welt.«