Mawu a Yobu
1Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2“Ndithudi inuyo ndinu anthu
ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu;
ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga,
ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha.
Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka.
Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere,
ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino,
amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa,
kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa,
kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa
kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse,
ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11Kodi khutu sindiye limene limamva mawu
monga mmene lilime limalawira chakudya?
12Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba?
Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu;
uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso.
Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma;
akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana;
munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17Iye amalanda aphungu nzeru zawo
ndipo amapusitsa oweruza.
18Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo
ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo
ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika
ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21Iye amanyoza anthu otchuka
ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima
ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso;
amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi;
amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira;
Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
Ответ Иова
Иов утверждает, что он так же мудр, как и его друзья
1Тогда Иов ответил:
2– Ну, конечно же, только вы люди,
и мудрость умрет вместе с вами!
3Но у меня есть ум, как у вас;
я ничем не хуже вас,
да и кто же всего этого не знает?
4Я стал для друзей посмешищем,
а ведь я к Богу взывал, и Он мне отвечал!
Я, праведный и безупречный,
стал посмешищем!
5Кто, находясь в благополучии, презирает несчастного,
тот вскоре и сам поскользнется.
6Шатры грабителей в безопасности,
и те, кто гневит Бога, спокойны,
словно держат Бога в руках12:6 Смысл этого места в еврейском тексте неясен..
Бог дал разумение всему творению
7Но спроси у животных, они научат тебя,
у небесных птиц, они тебе скажут.
8Побеседуй с землей, она наставит тебя,
и рыбы морские тебе возвестят.
9Кто среди них не знает,
что все это сделала рука Господня?
10Жизнь всякой твари в Его руке,
как и дыхание всякого человека.
11Разве не ухо различает слова,
и не язык распознает вкус пищи?
12Разве не у старейших мудрость?
Разве долгая жизнь не приносит разум?
Все в руках Бога
13У Бога – мудрость и сила;
совет и разум – Его.
14Что Он разрушил, не восстановится,
заключенные Им не выйдут на волю.
15Он удержит воды, и будет засуха,
отпустит – они затопят землю.
16У Него всесилие и премудрость;
в Его власти и обманутый, и обманщик.
17Советчиков Он гонит босыми
и глупцами делает судей.
18У царей Он развязывает пояса мантии,
и обвязывает им бедра повязкой раба.
19Священников Он гонит босыми,
и низвергает сильных.
20Он лишает речи искусных советников
и отбирает разум у старцев.
21Он покрывает позором знатных
и лишает оружия могучих.
22Он открывает глубины тьмы
и выводит на свет тень смертную.
23Он возвышает и губит народы,
умножает их и рассеивает.
24Он лишает рассудка земных владык
и шлет их в пустыню, где нет пути.
25Бредут они на ощупь в темноте, без света,
и шатаются, словно пьяные.