Yobu 10 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 10:1-22

1“Ine ndatopa nawo moyo wanga;

choncho ndidzanena zodandaula zanga momasuka

ndipo ndidzayankhula mwa kuwawidwa mtima kwanga.

2Ndidzati kwa Mulungu wanga: Musandiweruze kuti ndine wolakwa,

koma mundiwuze chifukwa chimene Inu mukukanganira ndi ine.

3Kodi mumakondwera mukamandizunza,

kunyoza ntchito ya manja anu,

chonsecho mukusekerera ndi zochita za anthu oyipa?

4Kodi maso anu ali ngati a munthu?

Kodi mumaona zinthu monga momwe amazionera munthu?

5Kodi masiku anu ali ngati masiku a munthu,

kapena zaka zanu ngati zaka za munthu,

6kuti Inu mufufuze zolakwa zanga

ndi kulondola tchimo langa,

7ngakhale mukudziwa kuti sindine wolakwa

ndiponso kuti palibe amene angandilanditse mʼdzanja lanu?

8“Munandiwumba ndi kundipanga ndi manja anu.

Kodi tsopano Inu mudzatembenuka ndi kundiwononga?

9Kumbukirani kuti munandipanga ndi dothi,

kodi tsopano mundibwezeranso ku fumbi?

10Suja munapatsa abambo anga mphamvu zoti andibale,

suja munandikuza bwino mʼmimba mwa amayi anga?

11Munandikuta ndi khungu ndi mnofu

ndi kundilumikiza pamodzi ndi mafupa ndi mitsempha?

12Munandipatsa moyo ndi kundionetsa chifundo chanu,

ndipo munasamalira bwino moyo wanga.

13“Koma izi ndi zimene munabisa mu mtima mwanu,

ndipo ndikudziwa kuti zinali mʼmaganizo anu:

14Kuti ngati ndingachimwe mudzakhala mukundipenyetsetsa

ndipo kuti simudzalola kuti ndisalangidwe chifukwa cha kulakwa kwanga.

15Ngati ndili wolakwa, tsoka langa!

Koma ngakhale ndili wosalakwa sindingathe kutukula mutu wanga,

pakuti ndagwidwa ndi manyazi

ndipo ndamizidwa mʼmavuto anga.

16Ndipo ndikatukula mutu wanga, Inu mumandisaka ngati mkango

ndiponso mumandiopseza ndi mphamvu yanu.

17Mumabweretsa mboni zatsopano potsutsana nane

ndipo mkwiyo wanu pa ine umanka nukulirakulira ndi

magulu anu olimbana nane amanka nachulukirachulukira.

18“Chifukwa chiyani Inu munalola kuti ndibadwe?

Ndi bwino ndikanafa diso lililonse lisanandione.

19Ndikanapanda kubadwa,

kapena akanangonditenga nditabadwa kupita nane ku manda!

20Kodi masiku anga owerengeka sali pafupi kutha?

Ndilekeni kuti ndipumule pangʼono pokha

21ndisanapite ku malo amene munthu sabwererako

ku dziko la imfa ndi kwa mdima wandiweyani,

22ku dziko la mdima wandiweyani

ndi chisokonezo,

kumene kuwala kumakhala ngati mdima.”

La Bible du Semeur

Job 10:1-22

Dieu, pourquoi t’en prends-tu à moi ?

1Je suis dégoûté de la vie,

je ne retiendrai plus mes plaintes,

je veux exprimer l’amertume ╵qui remplit tout mon être.

2Et je veux dire à Dieu : ╵Ne me traite pas en coupable,

fais-moi savoir pourquoi ╵tu me prends à partie.

3Trouves-tu bien de m’accabler, ╵de mépriser ta créature, ╵produite par tes mains, ╵et de favoriser, ╵les desseins des méchants ?

4As-tu des yeux de chair,

et ne vois-tu ╵qu’à la façon des hommes ?

5Ta vie serait-elle aussi courte ╵que celle des humains,

et tes années passeraient-elles ╵comme celles d’un homme,

6pour que tu recherches ma faute

et pour que tu enquêtes ╵sur mon iniquité10.6 Autre traduction : pour que tu me poursuives en justice et que tu cherches à me faire payer ma faute. ?

7Pourtant tu le sais bien, ╵je ne suis pas coupable,

et il n’y a personne ╵pour me délivrer de ta main !

8Tes mains m’ont façonné, ╵ensemble elles m’ont fait ╵moi tout entier, ╵et tu me détruirais10.8 Hébreu difficile. Autre traduction, d’après l’ancienne version grecque : Tes mains m’ont façonné, elles m’ont fait, mais après cela, tu as changé d’avis et tu me détruis. !

9Oh, souviens-toi, je t’en supplie, ╵que tu m’as façonné ╵comme avec de l’argile.

Voudrais-tu à présent ╵me faire retourner ╵à la poussière ?

10Tu m’as coulé comme du lait,

puis fait cailler en fromage.

11Oui, tu m’as revêtu ╵de peau, de chair,

tu m’as tissé d’os et de nerfs.

12C’est toi qui m’as donné la vie, ╵tu m’as accordé ta faveur10.12 Autre traduction : c’est toi qui m’as accordé la grâce de la vie.,

et tes soins vigilants ╵ont préservé mon souffle.

13Mais voilà donc ╵ce que tu cachais dans ton cœur

et je sais maintenant ╵ce que tu méditais :

14me surveiller, ╵voir si je pèche,

ne me laisser passer ╵aucune faute,

15et si je suis coupable, ╵malheur à moi !

Si je suis juste, ╵je ne puis cependant ╵marcher la tête haute,

moi qui suis rassasié ╵de honte et de misère.

16Car si je me relève, ╵tu me pourchasses comme un lion,

et tu ne cesses d’accomplir ╵tes hauts faits contre moi.

17Sans cesse tu dépêches ╵de nouveaux témoins contre moi10.17 D’autres comprennent, en modifiant légèrement le texte hébreu : Tu renouvelles constamment ton hostilité contre moi.,

ta fureur envers moi s’accroît,

tes troupes se succèdent ╵pour m’assaillir.

18Pourquoi donc m’as-tu fait sortir ╵du ventre maternel ?

J’aurais péri alors ╵et aucun œil ne m’aurait vu.

19Je serais comme ceux ╵qui n’ont jamais été,

j’aurais été porté ╵du sein maternel au tombeau.

20Il me reste si peu de jours, ╵ils touchent à leur fin10.20 Autre traduction : Qu’il cesse donc..

Que ne me laisse-t-il, ╵que je respire un peu,

21avant de partir sans retour ╵au pays des ténèbres

et de l’obscurité profonde,

22terre plongée dans une nuit obscure, ╵où règnent d’épaisses ténèbres ╵et soumise au désordre, ╵où la lumière ╵est comme une nuit noire.