Yesaya 7 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 7:1-25

Yesaya Achenjeza Ahazi

1Pamene Ahazi mwana wa Yotamu, mdzukulu wa Uziya anali mfumu ya Yuda, Rezini mfumu ya Siriya ndi Peka mwana wa Remaliya, mfumu ya Israeli anabwera kudzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu, koma sanathe kuwugonjetsa.

2Tsono nyumba ya Davide inawuzidwa kuti, “Dziko la Siriya lagwirizana ndi Efereimu.” Choncho mfumu Ahazi ndi anthu ake ananjenjemera, monga momwe mitengo ya mʼnkhalango imagwedezekera ndi mphepo.

3Pamenepo Yehova anawuza Yesaya kuti, “Tuluka, iwe ndi mwana wako Seariyasubu, mupite mukakumane ndi Ahazi kumapeto kwa ngalande yamadzi yochokera ku Dziwe Lakumtunda, pa msewu wopita ku Munda wa mmisiri wochapa nsalu. 4Ukamuwuze kuti, ‘Chenjera, khala phee ndipo usaope. Usataye mtima chifukwa cha zitsa ziwiri zomwe zikufuka, chifukwa cha ukali woopsa wa Rezini ndi Siriya, ndiponso wa Peka mwana wa Remaliya. 5Mfumu ya Siriya, Efereimu ndi mwana wa Remaliya apangana kuti akuchitire choyipa. Akunena kuti, 6‘Tiyeni tikalimbane ndi Yuda. Tiyeni tiliwononge ndi kuligawa; tiligawane pakati pathu, ndipo tilonge ufumu mwana wa Tabeeli kumeneko.’ 7Komabe zimene akunena Ambuye Yehova ndi izi:

“ ‘Zimenezo sizidzatheka,

sizidzachitika konse,

8pakuti Siriya amadalira Damasiko,

ndipo Damasiko amadalira mfumu Rezini basi.

Zisanathe zaka 65

Efereimu adzawonongedwa kotheratu, sadzakhalanso mtundu wa anthu.

9Dziko la Efereimu limadalira Samariya

ndipo Samariya amadalira mwana wa Remaliya basi.

Mukapanda kulimbika pa chikhulupiriro chanu,

ndithu simudzalimba konse.’ ”

10Yehova anayankhulanso ndi Ahazi, 11“Pempha chizindikiro kwa Yehova Mulungu wako, chikhale chozama ngati manda kapena chachitali ngati mlengalenga.”

12Koma Ahazi anati, “Ine sindipempha; sindikufuna kuyesa Yehova.”

13Apo Yesaya anati, “Imva tsopano, iwe nyumba ya Davide! Kodi sikokwanira kutopetsa anthu? Kodi mudzayeseranso kutopetsa Mulungu wanga? 14Nʼchifukwa chake Ambuye mwini adzakupatsani chizindikiro: Onani, namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli. 15Azidzadya chambiko ndi uchi, mpaka atadziwa kukana choyipa ndi kusankha chabwino. 16Koma nthawi yokana choyipa ndi kusankha chabwino kwa mwanayo isanafike, mayiko a mafumu awiri amene amakuopsaniwo adzakhala atasanduka bwinja. 17Yehova adzabweretsa pa inu, pa anthu anu ndiponso pa nyumba ya bambo wanu masiku a mavuto woti sanakhalepo kuyambira tsiku limene Efereimu anapatukana ndi Yuda. Yehova adzabweretsa mfumu ya ku Asiriya.”

18Tsiku limenelo Yehova adzalizira likhweru ntchentche zochokera ku mitsinje yakutali ku Igupto, ndiponso njuchi zochokera ku dziko la Asiriya. 19Onsewo adzafika ndi kudzakhazikika mu zigwa zozama, mʼmingʼalu ya matanthwe ndi mʼzitsamba zonse zaminga ndiponso ponse pamene pali malo omwetsera ziweto. 20Tsiku limenelo Ambuye adzalemba ganyu ometa ochokera kutsidya kwa Mtsinje, ndiye mfumu ya ku Asiriya, kudzameta tsitsi lanu la ku mutu ndi la mʼmiyendo ndi ndevu zomwe. 21Tsiku limenelo adzangosunga ngʼombe yayikazi yayingʼono ndi mbuzi ziwiri. 22Ndipo chifukwa cha kuchuluka kwa mkaka umene ziwetozi zidzapereka, munthuyo azidzadya chambiko. Aliyense amene adzatsalire mʼdzikomo azidzadya chambiko ndi uchi. 23Tsiku limenelo, paliponse pamene panali mitengo ya mpesa 1,000 ndipo mtengo wake ndi wokwana masekeli asiliva 1,000, padzamera mkandankhuku ndi minga. 24Anthu adzapita kumeneko kukachita uzimba ali ndi uta ndi mivi, popeza kuti mʼdziko monsemo mudzakhala mkandankhuku ndi minga. 25Ndipo mʼmapiri monse mʼmene kale munkalimidwa ndi khasu, simudzapitamo kuopa mkandankhuku ndi minga; malowo adzasanduka odyetserako ngʼombe ndi nkhosa.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

以賽亞書 7:1-25

給亞哈斯王的信息

1烏西雅的孫子、約坦的兒子亞哈斯猶大王時,亞蘭利迅利瑪利的兒子以色列比加來攻打耶路撒冷,卻無法攻破。 2亞蘭以色列結盟的消息傳到猶大王那裡,舉國上下都嚇得膽戰心驚,好像林中被風吹動的樹木。 3耶和華對以賽亞說:「你帶著兒子施亞雅述出去,到上池水溝的盡頭——通往漂布場的路上迎見亞哈斯4告訴他要謹慎鎮定,不要害怕,不要因亞蘭利迅利瑪利的兒子的怒氣而膽怯,他們不過是兩個冒煙的火把頭。 5亞蘭王和以法蓮利瑪利的兒子陰謀毀滅他, 6企圖攻打並瓜分猶大,改立他比勒的兒子為王。 7但主耶和華說,

『這陰謀必無法得逞。

8亞蘭的都城是大馬士革

大馬士革的首領是利迅

六十五年之內,

以色列必亡國。

9以色列的都城是撒瑪利亞

撒瑪利亞的首領是利瑪利的兒子。

你們信心若不堅定,

必無法堅立。』」

10耶和華又對亞哈斯說: 11「向你的上帝耶和華求個徵兆吧,或顯在天上,或顯在陰間。」 12亞哈斯說:「我不求,我不要試探耶和華。」 13以賽亞說:「大衛的子孫啊,你們聽著!你們使人厭煩還不夠嗎?還要使我的上帝厭煩嗎? 14所以,主會親自給你們一個徵兆,必有童貞女7·14 童貞女」或譯「女子」。懷孕生子並給祂取名叫以馬內利7·14 以馬內利」意思是「上帝與我們同在」。15他將吃乳酪和蜂蜜,一直到他能明辨是非。 16然而,在他能明辨是非之前,你所懼怕的這二王的國土必荒廢。

17「之後,耶和華必讓亞述王來攻擊你們。這是你全家及你的人民自以色列猶大分裂以來從未有的日子。 18那時,耶和華的哨聲一響,埃及的大軍必像蒼蠅一樣從遙遠的尼羅河飛撲而來,亞述的人馬必如黃蜂一樣蜂擁而至, 19遍佈險峻的山谷、岩穴、一切荊棘叢和草場。 20那時,主必使用幼發拉底河對岸的亞述王來毀滅你們,就像用租來的剃刀剃光你們的頭髮、鬍鬚和身上的汗毛。

21「那時,一個人將養活一頭母牛和兩隻羊。 22因出產的奶豐富,他就有乳酪吃,境內剩下的人都將吃乳酪和蜂蜜。 23那時,本來有千株葡萄、價值千金的園子必長滿荊棘和蒺藜, 24人們必帶著弓箭去打獵,因為遍地長滿了荊棘和蒺藜。 25你因懼怕荊棘和蒺藜,將不再去從前用鋤頭開墾的山地,那裡將成為牧放牛羊的地方。」