Yesaya 65 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 65:1-25

Chiweruzo ndi Chipulumutso

1“Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu;

ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze.

Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine,

ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’

2Tsiku lonse ndatambasulira manja anga

anthu owukira aja,

amene amachita zoyipa,

natsatira zokhumba zawo.

3Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa

mopanda manyazi.

Iwo amapereka nsembe mʼminda

ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.

4Amakatandala ku manda

ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika.

Amadya nyama ya nkhumba,

ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.

5Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire,

chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’

Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga,

ngati moto umene umayaka tsiku lonse.

6“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo;

sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu

chifukwa cha machimo awo

7ndi a makolo awo,”

akutero Yehova.

“Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri

ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo,

Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata

zimene anachita kale.”

8Yehova akuti,

“Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa

ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo,

popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’

Inenso chifukwa cha mtumiki wanga;

sindidzawononga onse.

9Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo,

ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo.

Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi,

ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.

10Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa,

ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe

kwa anthu anga ondifunafuna Ine.

11“Koma inu amene mumasiya Yehova

ndi kuyiwala phiri langa lopatulika,

amene munamukonzera Gadi chakudya

ndi kuthirira Meni chakumwa,

12ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe,

ndipo nonse mudzaphedwa;

chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani,

ndinayankhula koma simunamvere.

Munachita zoyipa pamaso panga

ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”

13Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti,

“Atumiki anga adzadya,

koma inu mudzakhala ndi njala;

atumiki anga adzamwa,

koma inu mudzakhala ndi ludzu;

atumiki anga adzakondwa,

koma inu mudzakhala ndi manyazi.

14Atumiki anga adzayimba

mosangalala,

koma inu mudzalira kwambiri

chifukwa chovutika mu mtima

ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.

15Anthu anga osankhidwa

adzatchula dzina lanu potemberera.

Ambuye Yehova adzakuphani,

koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.

16Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo

adzachita zimenezo kwa Mulungu woona;

ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo

adzalumbira mwa Mulungu woona.

Pakuti mavuto akale adzayiwalika

ndipo adzachotsedwa pamaso panga.

Chilengedwe Chatsopano

17“Taonani, ndikulenga

mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano.

Zinthu zakale sizidzakumbukika,

zidzayiwalika kotheratu.

18Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya

chifukwa cha zimene ndikulenga,

pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa

ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.

19Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu

ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga.

Kumeneko sikudzamvekanso kulira

ndi mfuwu wodandaula.

20“Ana sadzafa ali akhanda

ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse.

Wamngʼono mwa iwo

adzafa ali ndi zaka 100.

Amene adzalephere kufika zaka 100

adzatengedwa kukhala

wotembereredwa.

21Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo,

adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.

22Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo,

kapena kudzala ndi ena nʼkudya.

Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo

wautali ngati mitengo.

Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito

ya manja awo nthawi yayitali.

23Sadzagwira ntchito pachabe

kapena kubereka ana kuti aone tsoka;

chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova,

iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.

24Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe.

Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.

25Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi.

Mkango udzadya udzu monga ngʼombe,

koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka.

Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala

chinthu chopweteka kapena chowononga,”

akutero Yehova.

New Serbian Translation

Књига пророка Исаије 65:1-25

Против идола, а за Јерусалим

1„Потражили су ме који нису питали,

нашли су ме који нису искали.

Рекао сам: ’Ево ме! Ево ме!’

пуку који моје име призивао није.

2Руке своје пружао сам ваздан

према народу одметничком,

који путем неваљаним хода

по својим замислима;

3народу који ме у лице

изазива стално,

жртве приносе по вртовима

и каде на опекама,

4бораве по гробовима,

ноћ проводе по скривеним местима,

једу месо свињско

и дробе гадости у зделе своје;

5који говоре: ’Себе се држи!

Не приступај мени, јер сам од тебе светији.’

Ови су дим у носу мом,

ватра што поваздан гори.

6Ево, записано је преда мном,

нећу ућутати док не намирим,

а намирићу у недра њихова.

7Кривице ваше и кривице отаца ваших,

заједно су – говори Господ –

јер они каде по горама

и руже ме по узвишицама.

И некадашње дело њихово

одмерићу у недра њихова.“

8Говори Господ:

„Као кад се стиче сок у грозду,

па се каже: ’Не затири га.

У њему је благослов’,

тако ћу учинити ради својих слугу:

нећу све то затрти.

9И извешћу из Јакова потомство,

и из Јуде мојих гора поседника,

и то ће изабраници моји баштинити,

и слуге моје тамо ће се настанити.

10И Сарон ће постати за овце пландиште,

и долина Ахор65,10 Долина Ахор Долина пропасти, позната из догађаја око Јерихона и Аја. за говеда почивалиште –

народу мојем који мене тражи.

11А ви, који сте Господа оставили,

који сте свету гору моју заборавили,

који Гаду65,11 Божанство среће. трпезу постављате,

и који наливе изливате на олтар Менију65,11 Божанство судбине.

12за вас одредио сам мач

и да се сви савијете ради клања.

Зато што сам звао и одговорили нисте,

што сам говорио и слушали нисте.

Него сте чинили оно што ја сматрам да је зло,

изабрали сте оно што ми није угодно.“

13Зато говори Господар Господ:

„Ево, слуге моје ће јести,

а ви ћете гладовати.

Ево, слуге моје ће пити,

а ви ћете жедни бити.

Ево, слуге моје ће се радовати,

а ви ћете се стидети.

14Ево, слуге моје ће се веселити

због добра у срцу,

а ви ћете викати

због бола у срцу,

и туговаћете због сломљеног духа.

15И оставићете име своје

да њим куну моји изабраници:

и нека те усмрти Господар Господ!

А слуге ћу своје другим именом назвати.

16Широм земље ко се буде благосиљао,

нека се благосиља Богом верним.

И ко се буде заклињао широм земље,

нека се заклиње Богом верним.

Наиме, пређашње невоље ће бити заборављене,

и зато ће бити од очију мојих сакривене.

Нова небеса и нова земља

17Јер, гле, ја стварам

небеса нова и земљу нову,

и пређашње се помињати неће,

и на ум вам то падати неће.

18Стога веселите се и кличите

од колена до колена за оно што стварам.

А ево, ја стварам од Јерусалима клицање

и од народа његова весеље.

19И клицаће у Јерусалиму,

и веселиће се у мом народу;

и више у њему чути се неће

глас који оплакује и глас који вапи.

20Тамо више неће бити

одојчета краткога живота,

ни старца који не би навршио дане своје,

јер ће младић као стогодишњак умирати,

и стогодишњи грешник

проклетим ће се сматрати.

21И куће ће градити и настањивати,

и винограде садити и род њихов јести.

22Неће једни градити, а други настањивати;

неће једни садити, а други јести.

Него ће као трајање дрвета

бити трајање народа мојега,

а дела својих руку

користиће изабраници моји.

23Неће се мучити напразно,

нити ће рађати за ужас,

јер они ће бити потомство благословених од Господа

и изданци њихови с њима.

24И биће пре него што ће призвати,

а ја ћу им одговорити;

још док буду говорили,

ја ћу их услишити.

25Вук и јагње заједно ће се напасати,

и лав ће слично волу сламу јести,

а змији ће прашина бити за храну.

Они зло чинити неће, и потирати неће

нигде на светој гори мојој

– говори Господ.“