Yesaya 60 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 60:1-22

Ulemerero wa Ziyoni

1“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika,

ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.

2Taona, mdima waphimba dziko lapansi

ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina,

koma Yehova adzakuwalira iwe,

ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.

3Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako

ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.

4“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika.

Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe;

ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali

ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.

5Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri,

mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe;

chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe

chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.

6Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako,

ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai.

Ndipo onse a ku Seba adzabwera

atanyamula golide ndi lubani

uku akutamanda Yehova.

7Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu,

nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani;

zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe,

ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.

8“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo,

ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?

9Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali;

patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi,

zikubweretsa ana ako ochokera kutali,

pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo,

kudzalemekeza Yehova Mulungu wako,

Woyerayo wa Israeli,

pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.

10“Alendo adzamanganso malinga ako,

ndipo mafumu awo adzakutumikira.

Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya,

koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.

11Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse,

sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku,

kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo,

akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.

12Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe;

adzawonongeka kotheratu.

13“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini,

mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni

kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika;

ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.

14Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani;

onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu.

Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova;

Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.

15“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe,

koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya,

ndipo udzakhala malo a chimwemwe

cha anthu amibado yonse.

16Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu

ndi kuleredwa pa maere aufumu,

motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako,

Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.

17Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa,

ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo.

Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa

ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala.

Olamulira ako adzakhala a mtendere.

Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.

18Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako,

bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako,

ndidzakhala malinga ako okuteteza

ndipo udzanditamanda.

19Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire,

kapena mwezi kuti uwunikire usiku,

pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya,

ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.

20Dzuwa lako silidzalowanso,

ndipo mwezi wako sudzazimiriranso;

Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya,

ndipo masiku a mavuto ako adzatha.

21Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama

ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya.

Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala,

ntchito ya manja anga,

kuti aonetse ulemerero wanga.

22Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko,

kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu.

Ine ndine Yehova,

nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”

New International Reader’s Version

Isaiah 60:1-22

Zion Will Be Glorious

1“People of Jerusalem, get up.

Shine, because your light has come.

The glory of the Lord will shine on you.

2Darkness covers the earth.

Thick darkness spreads over the nations.

But I will rise and shine on you.

My glory will appear over you.

3Nations will come to your light.

Kings will come to the brightness of your new day.

4“Look up. Look all around you.

All your people are getting together to come back to you.

Your sons will come from far away.

Your daughters will be carried on the hip like little children.

5Then your face will glow with joy.

Your heart will beat fast because you are so happy.

Wealth from across the ocean will be brought to you.

The riches of the nations will come to you.

6Herds of young camels will cover your land.

They will come from Midian and Ephah.

They will also come from Sheba.

They’ll carry gold and incense.

And people will shout praises to me.

7All of Kedar’s flocks will be gathered to you.

The rams of Nebaioth will serve as your sacrifices.

I will accept them as offerings on my altar.

That is how I will bring honor to my glorious temple.

8“Whose ships are these that sail along like clouds?

They fly like doves to their nests.

9People from the islands are coming to me.

The ships of Tarshish are out in front.

They are bringing your children back from far away.

Your children are bringing their silver and gold with them.

They are coming to honor me.

I am the Lord your God.

I am the Holy One of Israel.

I have honored you.

10“People from other lands will rebuild your walls.

Their kings will serve you.

When I was angry with you, I struck you.

But now I will show you my tender love.

11Your gates will always stand open.

They will never be shut, day or night.

Then people can bring you the wealth of the nations.

Their kings will come along with them.

12The nation or kingdom that will not serve you will be destroyed.

It will be completely wiped out.

13“Lebanon’s glorious trees will be brought to you.

Its junipers, firs and cypress trees will be brought.

They will be used to make my temple beautiful.

And I will bring glory to the place where my throne is.

14The children of those who crush you will come and bow down to you.

All those who hate you will kneel down at your feet.

Jerusalem, they will call you the City of the Lord.

They will name you Zion, the City of the Holy One of Israel.

15“You have been deserted and hated.

No one even travels through you.

But I will make you into something to be proud of forever.

You will be a place of joy for all time to come.

16You will get everything you need from kings and nations.

You will be like children who are nursing

at their mother’s breasts.

Then you will know that I am the one who saves you.

I am the Lord. I set you free.

I am the Mighty One of Jacob.

17Instead of bronze I will bring you gold.

In place of iron I will give you silver.

Instead of wood I will bring you bronze.

In place of stones I will give you iron.

I will make peace govern you.

I will make godliness rule over you.

18People will no longer harm one another in your land.

They will not wipe out or destroy anything inside your borders.

You will call your walls Salvation.

And you will name your gates Praise.

19You will not need the light of the sun by day anymore.

The bright light of the moon will no longer have to shine on you.

I will be your light forever.

My glory will shine on you.

I am the Lord your God.

20Your sun will never set again.

Your moon will never lose its light.

I will be your light forever.

Your days of sorrow will come to an end.

21Then all your people will do what is right.

The land will belong to them forever.

They will be like a young tree I have planted.

My hands have created them.

They will show how glorious I am.

22The smallest family among you will become a tribe.

The smallest tribe will become a mighty nation.

I am the Lord.

When it is the right time, I will act quickly.”