Yesaya 52 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 52:1-15

1Dzambatuka, dzambatuka iwe Ziyoni,

vala zilimbe.

Vala zovala zako zokongola,

iwe Yerusalemu, mzinda wopatulika.

Pakuti kuyambira tsopano anthu osachita mdulidwe ndi odetsedwa

sadzalowanso pa zipata zako.

2Sasa fumbi lako;

imirira nukhale pa mpando waufumu, iwe Yerusalemu.

Inu omangidwa a ku Ziyoni,

masulani maunyolo amene ali mʼkhosi mwanumo.

3Pakuti Yehova akuti,

“Sindinalandirepo kanthu pamene ndinakugulitsani,

choncho mudzawomboledwa wopanda ndalama.”

4Pakuti Ambuye Yehova akuti,

“Poyamba paja anthu anga anapita kukakhala ku Igupto;

nawonso Asiriya awapondereza popanda chifukwa.”

5Tsopano Ine Yehova ndikuti,

“Kodi nditani pakuti anthu anga atengedwa ukapolo osaperekapo kanthu,

amene amawalamulira amawanyoza,”

akutero Yehova.

“Ndipo tsiku lonse, akungokhalira

kuchita chipongwe dzina langa.

6Tsono tsiku limenelo anthu anga adzadziwa dzina langa;

kotero adzadziwa

kuti ndi Ine amene ndikuyankhula,

Indedi, ndine.”

7Ngokongoladi mapazi a

amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri.

Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere,

chisangalalo ndi chipulumutso.

Iwo akubwera kudzawuza anthu

a ku Ziyoni kuti,

“Mulungu wako ndi mfumu!”

8Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo;

akuyimba pamodzi mwachimwemwe.

Popeza akuona chamaso

kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.

9Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe,

inu mabwinja a Yerusalemu,

pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake,

wapulumutsa Yerusalemu.

10Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika

pamaso pa anthu a mitundu yonse,

ndipo anthu onse a dziko lapansi

adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.

11Nyamukani, nyamukani, chokaniko ku Babuloniko!

Musakhudze kanthu kodetsedwa!

Inu amene mumanyamula ziwiya za Yehova

tulukanimo ndipo mudziyeretse.

12Koma simudzachoka mofulumira

kapena kuchita chothawa;

pakuti Yehova adzayenda patsogolo panu,

Mulungu wa Israeli adzakutetezani kumbuyo kwanu.

Kuzunzika ndi Ulemerero wa Mtumiki

13Taonani, mtumiki wanga adzapambana pa ntchito yake

adzakwezedwa ndi kulemekezedwa ndipo adzalandira ulemu waukulu kwambiri.

14Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka,

chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu.

Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.

15Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye,

ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye.

Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona,

ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.

La Bible du Semeur

Esaïe 52:1-15

Jérusalem rétablie

1Réveille-toi, ╵réveille-toi,

Sion, pare-toi de ta force !

Mets tes vêtements d’apparat,

Jérusalem, ô ville sainte !

Car désormais ╵ni l’incirconcis ni l’impur

n’entreront plus chez toi.

2Secoue donc ta poussière, ╵relève-toi, Jérusalem, ╵installe-toi,

délivre-toi des chaînes ╵qui enserrent ton cou,

toi qui es prisonnière, ╵Dame Sion !

3Car voici ce que l’Eternel déclare : Puisqu’on vous a vendus pour rien, ce sera sans argent qu’on vous libérera. 4Car voici ce que déclare le Seigneur, l’Eternel : Mon peuple est tout d’abord descendu en Egypte afin d’y séjourner, ensuite l’Assyrien l’a opprimé sans cause. 5Mais à présent ici, qu’est-ce que j’ai à faire ? demande l’Eternel. Puisque mon peuple a été pris pour rien, ses oppresseurs se vantent52.5 D’après le texte hébreu de Qumrân. Le texte hébreu traditionnel a : poussent des cris., déclare l’Eternel, et, à longueur de jour, mon nom est outragé52.5 Cité en Rm 2.24 d’après l’ancienne version grecque. ! 6C’est pourquoi mon peuple va savoir qui je suis. Oui, il saura en ce jour-là que c’est moi qui ai dit : Je viens !

Dieu délivre

7Comme il est beau de voir ╵sur les montagnes

les pas du messager ╵d’une bonne nouvelle,

qui annonce la paix52.7 Voir Na 2.1 ; Ep 6.15. Cité en Rm 10.15.,

qui parle de bonheur,

et qui annonce le salut,

qui dit à Sion : « Ton Dieu règne. »

8On entend tes guetteurs,

ils élèvent la voix,

ils crient de joie ensemble

car de leurs propres yeux ils voient

l’Eternel arriver ╵de nouveau à Sion52.8 Le texte hébreu de Qumrân ajoute ici : avec amour..

9Poussez des cris de joie, ╵ensemble faites éclater ╵votre allégresse,

vous, ruines de Jérusalem !

Car l’Eternel ╵a consolé son peuple

et délivré Jérusalem.

10L’Eternel a manifesté ╵sa puissance et sa sainteté

aux yeux de toutes les nations,

et tous les confins de la terre ╵verront

la délivrance ╵qu’apporte notre Dieu.

11Partez, partez, ╵sortez de là,

ne touchez rien d’impur52.11 Cité en 2 Co 6.17 d’après l’ancienne version grecque. !

Sortez de cette ville !

Purifiez-vous,

vous qui portez les ustensiles ╵de l’Eternel52.11 C’est-à-dire les ustensiles sacrés du culte que les Babyloniens avaient emportés lors de la destruction du temple de Jérusalem en 587 et que les exilés ramèneront. Les lévites ne devaient rien toucher d’impur, rien qui ait rapport aux pratiques idolâtres des païens (voir Nb 4.24-28). !

12Vous ne sortirez pas ╵en courant à la hâte52.12 Pas comme lors de la sortie d’Egypte.,

vous ne marcherez pas ╵comme des fugitifs,

car l’Eternel ╵marchera devant vous,

et le Dieu d’Israël ╵fermera votre marche.

Le quatrième chant du Serviteur

13Voici, mon serviteur

agira en toute sagesse52.13 Autre traduction : réussira.,

il sera haut placé,

très élevé, ╵grandement exalté.

14Beaucoup ont été horrifiés

tellement son visage ╵était défiguré

et tant son apparence ╵n’avait plus rien d’humain.

15Car il accomplira le rite ╵de l’aspersion ╵pour des peuples nombreux52.15 Traduction incertaine. Les versions ont compris : de même, de nombreux peuples s’émerveilleront à son sujet..

Les rois, à son sujet, ╵resteront bouche close,

car ils verront eux-mêmes ╵ce qui ne leur avait ╵pas été raconté,

ils comprendront ╵ce qui ne leur avait ╵pas été annoncé52.15 Cité en Rm 15.21, d’après l’ancienne version grecque..