Yesaya 51 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 51:1-23

Chipulumutso Chamuyaya cha Ziyoni

1“Mverani Ine, inu amene mukufuna chipulumutso

ndiponso amene mumafunafuna Yehova:

Taganizani za thanthwe kumene munasemedwa

ndipo ku ngwenya kumene anakukumbani;

2taganizani za Abrahamu, kholo lanu,

ndi Sara, amene anakubalani.

Pamene ndinkamuyitana nʼkuti alibe mwana,

koma ndinamudalitsa ndi kumupatsa ana ambiri.

3Yehova adzatonthozadi Ziyoni,

ndipo adzachitira chifundo mabwinja ake onse;

Dziko lake la chipululu adzalisandutsa ngati Edeni,

malo ake owuma ngati munda wa Yehova.

Anthu adzayimba nyimbo zonditamanda

ndi kundiyamika.

4“Mverani Ine, anthu anga:

tcherani khutu, inu mtundu wanga:

malangizo adzachokera kwa Ine;

cholungama changa chidzawunikira anthu a mitundu yonse.

5Ndili pafupi kubwera kudzawombola anthu anga.

Ndidzabwera mofulumira ngati kuwunika kudzapulumutsa anthu anga;

ndipo ndidzalamulira anthu a mitundu yonse.

Mayiko akutali akundiyembekezera.

Iwo akudikira kuti ndidzawapulumutse.

6Kwezani maso anu mlengalenga,

yangʼanani pansi pa dziko;

mlengalenga udzazimirira ngati utsi,

dziko lapansi lidzatha ngati chovala

ndipo anthu ake adzafa ngati nsabwe.

Koma chipulumutso changa chidzakhala mpaka muyaya,

chilungamo changa chidzakhala cha nthawi zonse.

7“Mverani Ine, inu amene mukudziwa choonadi,

anthu inu amene mukusunga malangizo anga mʼmitima yanu;

musaope kudzudzulidwa ndi anthu

kapena kuopsezedwa akamakulalatirani.

8Pakuti njenjete idzawadya ngati chovala;

mbozi idzawadya ngati thonje.

Koma chilungamo changa chidzakhala mpaka muyaya,

chipulumutso changa chidzakhala mpaka mibadomibado.”

9Dzambatukani, dzambatukani! Valani zilimbe,

Inu Yehova;

dzambatukani, monga munkachitira masiku amakedzana,

monga nthawi ya mibado yakale.

Si ndinu kodi amene munaduladula Rahabe,

amene munabaya chinjoka cha mʼnyanja chija?

10Kodi sindinu amene munawumitsa nyanja yayikulu,

madzi ozama kwambiri aja?

Kodi sindinu amene munapanga njira pa madzi ozama,

kuti anthu amene munawapulumutsa awoloke powuma?

11Anthu amene Yehova anawawombola adzabwerera

nakafika ku Ziyoni nyimbo ili pakamwa;

chimwemwe chamuyaya chizidzaonekera pa nkhope zawo.

Adzakhala ndi chikondwerero ndi chimwemwe,

chisoni ndi kubuwula zidzathawa.

12Yehova akuti, “Ndinetu amene ndimakutonthozani mtima.

Chifukwa chiyani mukuopa munthu woti adzafa?

Mukuopa munthu woti monga udzu sadzakhalitsa.

13Koma inu mumayiwala Yehova Mlengi wanu,

amene anayala za mlengalenga

ndi kuyika maziko a dziko lapansi.

Inu nthawi zonse mumaopsezedwa

chifukwa cha ukali wa anthu okuponderezani

amene angofuna kukuwonongani.

Kodi uli kuti tsopano ukali wa anthu okuponderezaniwo?

14Amʼndende adzamasulidwa posachedwa;

sadzalowa mʼmanda awo,

kapena kusowa chakudya.

15Pakuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

amene ndimavundula nyanja kotero mafunde ake amakokoma.

Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

16Ndayika mawu anga mʼkamwa mwanu

ndipo ndakuphimbani ndi mthunzi wa dzanja langa.

Ine ndimayika pa malo pake zinthu za mlengalenga,

ndipo ndinayika maziko a dziko lapansi,

ndimawuza anthu a ku Ziyoni kuti, ‘Ndinu anthu anga.’ ”

Kutha kwa Mavuto A Yerusalemu

17Dzambatuka, dzambatuka!

Imirira iwe Yerusalemu.

Iwe amene wamwa chikho cha mkwiyo

chimene Yehova anakupatsa.

Iwe amene unagugudiza

chikho chochititsa chizwezwe.

18Mwa ana onse amene anabereka,

panalibe ndi mmodzi yemwe anamutsogolera;

mwa ana onse amene analera,

panalibe ndi mmodzi yemwe anamugwira dzanja.

19Mavuto awiriwa akugwera iwe.

Dziko lako lasakazika ndi kuwonongeka. Anthu afa ndi njala ndi lupanga.

Ndani angakumvere chisoni?

Ndani angakutonthoze?

20Ana ako akomoka;

ali lambalamba pa msewu,

ngati mphoyo yogwidwa mu ukonde.

Ukali wa Yehova

ndi chidzudzulo chake zidzawagwera.

21Nʼchifukwa chake imva izi iwe amene ukuvutika,

iwe amene waledzera, koma osati ndi vinyo.

22Ambuye Yehova wanu,

Mulungu amene amateteza anthu ake akuti,

“Taona, ndachotsa mʼdzanja lako

chikho chimene chimakuchititsa kudzandira;

sudzamwanso chikho

cha ukali wanga.

23Ndidzapereka chikhocho kwa anthu amene amakuzunza,

amene ankakuwuza kuti,

‘gona pansi tikuyende pa msana.’

Ndipo msana wako anawuyesa pansi popondapo,

ngati msewu woti ayendepo.”

Nova Versão Internacional

Isaías 51:1-23

A Salvação Eterna para Sião

1“Escutem-me, vocês que buscam a retidão

e procuram o Senhor:

Olhem para a rocha da qual foram cortados

e para a pedreira de onde foram cavados;

2olhem para Abraão, seu pai,

e para Sara, que os deu à luz.

Quando eu o chamei, ele era apenas um,

e eu o abençoei e o tornei muitos.”

3Com certeza o Senhor consolará Sião

e olhará com compaixão para todas as ruínas dela;

ele tornará seus desertos como o Éden,

seus ermos, como o jardim do Senhor.

Alegria e contentamento serão achados nela,

ações de graças e som de canções.

4“Escute-me, povo meu;

ouça-me, nação minha:

A lei sairá de mim;

minha justiça se tornará uma luz para as nações.

5Minha retidão logo virá,

minha salvação está a caminho,

e meu braço trará justiça às nações.

As ilhas esperarão em mim

e aguardarão esperançosamente pelo meu braço.

6Ergam os olhos para os céus,

olhem para baixo, para a terra;

os céus desaparecerão como fumaça,

a terra se gastará como uma roupa,

e seus habitantes morrerão como moscas.

Mas a minha salvação durará para sempre,

a minha retidão jamais falhará.

7“Ouçam-me, vocês que sabem o que é direito,

vocês, povo que tem a minha lei no coração:

Não temam a censura de homens

nem fiquem aterrorizados com seus insultos.

8Pois a traça os comerá como a uma roupa;

o verme os devorará como à lã.

Mas a minha retidão durará para sempre,

a minha salvação de geração em geração.”

9Desperta! Desperta! Veste de força,

o teu braço, ó Senhor;

acorda, como em dias passados,

como em gerações de outrora.

Não foste tu que despedaçaste o Monstro dos Mares51.9 Hebraico: Raabe.,

que traspassaste aquela serpente aquática?

10Não foste tu que secaste o mar,

as águas do grande abismo,

que fizeste uma estrada nas profundezas do mar

para que os redimidos pudessem atravessar?

11Os resgatados do Senhor voltarão.

Entrarão em Sião com cântico;

alegria eterna coroará sua cabeça.

Júbilo e alegria se apossarão deles,

tristeza e suspiro deles fugirão.

12“Eu, eu mesmo, sou quem a consola.

Quem é você para que tema homens mortais,

os filhos de homens, que não passam de relva,

13e para que esqueça o Senhor, aquele que fez você,

que estendeu os céus e lançou os alicerces da terra,

para que você viva diariamente, constantemente apavorada

por causa da ira do opressor,

que está inclinado a destruir?

Pois onde está a ira do opressor?

14Os prisioneiros encolhidos logo serão postos em liberdade;

não morrerão em sua masmorra,

nem terão falta de pão.

15Pois eu sou o Senhor, o seu Deus,

que agito o mar para que suas ondas rujam;

Senhor dos Exércitos é o meu nome.

16Pus minhas palavras em sua boca

e o cobri com a sombra da minha mão,

eu, que pus os céus no lugar,

que lancei os alicerces da terra

e que digo a Sião:

Você é o meu povo.”

O Cálice da Ira do Senhor

17Desperte, desperte!

Levante-se, ó Jerusalém,

você que bebeu da mão do Senhor

o cálice da ira dele,

você que engoliu, até a última gota,

da taça que faz os homens cambalearem.

18De todos os filhos que ela teve

não houve nenhum para guiá-la;

de todos os filhos que criou

não houve nenhum para tomá-la pela mão.

19Quem poderá consolá-la

dessas duas desgraças que a atingiram?

Ruína e destruição, fome e espada,

quem poderá51.19 Conforme os manuscritos do mar Morto, a Septuaginta, a Vulgata e a Versão Siríaca. O Texto Massorético diz como poderei. consolá-la?

20Seus filhos desmaiaram;

eles jazem no início de cada rua,

como antílope pego numa rede.

Estão cheios da ira do Senhor

e da repreensão do seu Deus.

21Portanto, ouça isto, você, aflita,

embriagada, mas não com vinho.

22Assim diz o seu Soberano, o Senhor,

o seu Deus, que defende o seu povo:

“Veja que eu tirei da sua mão

o cálice que faz cambalear;

dele, do cálice da minha ira,

você nunca mais beberá.

23Eu o porei nas mãos dos seus atormentadores,

que disseram a você:

‘Caia prostrada para que andemos sobre você’.

E você fez as suas costas como chão,

como uma rua para nela a gente andar”.