1Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake
Koresi amene anamugwira dzanja lamanja
kuti agonjetse mitundu ya anthu
ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo,
ndi kutsekula zitseko
kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
2Ine ndidzayenda patsogolo pako,
ndi kusalaza mapiri;
ndidzaphwanya zitseko za mkuwa
ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
3Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima,
katundu wa pamalo obisika,
kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova
Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
4Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo,
chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli,
Ine ndakuyitana pokutchula dzina
ndipo ndakupatsa dzina laulemu
ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
5Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina;
kupatula Ine palibenso Mulungu wina.
Ndidzakupatsa mphamvu,
ngakhale sukundidziwa Ine,
6kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo
anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha.
Ine ndine Yehova,
ndipo palibenso wina.
7Ndimalenga kuwala ndi mdima,
ndimabweretsa madalitso ndi tsoka;
ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
8“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba;
mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo.
Dziko lapansi litsekuke,
ndipo chipulumutso chiphuke kuti
chilungamo chimereponso;
Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
9“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake,
ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake.
Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti,
‘Kodi ukuwumba chiyani?’
Kodi ntchito yako inganene kuti,
‘Ulibe luso?’
10Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti,
‘Kodi munabereka chiyani?’
Kapena amayi ake kuti,
‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
11“Yehova
Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena,
zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi:
Kodi iwe ukundifunsa za ana anga,
kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12Ndine amene ndinapanga dziko lapansi
ndikulenga munthu kuti akhalemo.
Ine ndi manja anga ndinayalika thambo;
ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
13Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe:
ndipo ndidzawongolera njira zake zonse.
Iye adzamanganso mzinda wanga
ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo,
wopanda kupereka ndalama kapena mphotho,
akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
14Yehova akuti,
“Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu.
Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba
adzabwera kwa inu
ndipo adzakhala anthu anu;
iwo adzidzakutsatani pambuyo panu
ali mʼmaunyolo.
Adzakugwadirani
ndi kukupemphani, ponena kuti,
‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina;
palibenso mulungu wina.’ ”
15Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika
amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
16Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa.
Adzakhala osokonezeka maganizo.
17Koma Yehova adzapulumutsa Israeli
ndi chipulumutso chamuyaya;
simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka
mpaka kalekale.
18Yehova
analenga zinthu zakumwamba,
Iye ndiye Mulungu;
amene akulenga dziko lapansi,
ndi kulikhazikitsa,
sanalipange kuti likhale lopanda kanthu,
koma analipanga kuti anthu akhalemo.
Iyeyu akunena kuti:
Ine ndine Yehova,
ndipo palibenso wina.
19Ine sindinayankhule mwachinsinsi,
pamalo ena a mdima;
Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti,
“Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.”
Ine Yehova, ndimayankhula zoona;
ndikunena zolungama.
20Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere;
yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina.
Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo,
amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
21Fotokozani mlandu wanu,
mupatsane nzeru nonse pamodzi.
Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale?
Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana?
Kodi si Ineyo Yehova?
Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine,
Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa,
palibenso wina kupatula Ine.
22“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke,
inu anthu onse a pa dziko lapansi,
pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
23Ndalumbira ndekha,
pakamwa panga patulutsa mawu owona,
mawu amene sadzasinthika konse akuti,
bondo lililonse lidzagwada pamaso panga;
anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
24Iwo adzanene kwa Ine kuti,
‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’ ”
Onse amene anamuwukira Iye
adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli
zidzapambana ndi kupeza ulemerero.
Пророштво о Киру
1Говори Господ о помазанику свом,
Киру, ког прихватих за десницу
да пред њим оборим народе
и цареве лишим њиховог угледа:
„Пред њим двострука врата отварам,
и неће вратнице пред њим затворене бити.
2Ја ћу марширати пред тобом
да поравнам неравнине,
да разломим врата бронзана,
и покршим преворнице гвоздене.
3Дајем ти блага из мрачних одаја
и богатства из скровишта,
да схватиш да сам ја Господ,
који те зове по имену, Бог Израиљев.
4Ради слуге свога Јакова,
и изабраника Израиља,
и тебе позвах по имену,
наименовах те, иако ме ниси знао.
5Ја сам Господ и другога нема,
осим мене другог Бога нема.
Иако мене не познајеш,
ја сам те наоружао.
6Нека се зна од истока и од запада
да је ништавило све што је мимо мене.
Бог обећава спасење
Ја сам Господ и другога нема:
7ја творим светлост и стварам таму,
чиним мир и несрећу стварам;
ја, Господ, све то чиним.
8Росите, небеса, одозго,
и праведност, облаци, нека из вас пада.
Нека се отвори земља
и спасење нека буде плод,
те заједно проклија праведност;
ја, Господ, то сам створио.
Господ је свесилан
9Тешко оном ко расправља са Саздатељем својим,
а грне је међу грнчаријом!
Каже ли глина грнчару:
’Шта радиш?’
или дело његово:
’Он нема обе руке’?
10Тешко оном који оцу каже:
’Зашто си родио?’
или жени:
’Зашто си на свет донела?’“
11Говори Господ,
Израиљев Светитељ и његов Саздатељ:
„Зар је ваше да ме питате
о знацима над децом мојом,
и да ми заповедате над делом мојих руку?
12Ја сам земљу начинио
и човека на њој створио;
својим сам рукама небеса распростро
и свим војскама њиховим заповедам.
13Ја сам га подигао у праведности
и поравнао све путеве његове.
Он ће обновити мој град
и ослободити заробљене моје
без откупнине и без накнаде –
говори Господ над војскама.“
Обраћење туђинаца
14Говори Господ:
„Труд египатски и добитак кушки,
и Савајци, људи повисоки,
теби ће прећи и твоји ће бити,
за тобом ће ићи, у оковима претходити,
и теби ће се клањати,
и тебе молити:
’О, само код тебе је Божанство,
и осим Бога други не постоји.’“
15Заиста, ти си Божанство скривено,
Бог Израиљев, Спаситељ.
16Постидеће се и осрамотиће се сви,
заједно ће се повући покуњени они који праве кипове.
17Господ ће спасти Израиља
спасењем вечним,
нећете се постидети,
и до векова вечних нећете се осрамотити.
Господ указује на своја дела
18Та, говори Господ,
створитељ небеса
– он је Бог –
који је обликовао земљу
и изглед јој дао,
који је учврстио,
и није је створио да буде пустош,
него је уобличио да се на њој станује:
„Ја сам Господ и другог нема.
19Нисам говорио у тајности,
у закутку земље тамне.
Нисам рекао потомству Јаковљеву:
’Тражите ме у пустоши.’
Ја, Господ, говорим правду
и благовестим честитости.
Господ је Бог за све људе
20Саберите се и дођите,
заједно приступите, избеглице из других народа.
Незналице су који носе дрво идолско
и моле се божанству које не спасава.
21Објавите и предочите,
хајде, посаветујте се заједнички.
Ко је ово од давнина изјавио
и још тада предсказао?
Нисам ли ја, Господ?
Осим мене другог бога нема;
праведног Божанства и Спаситеља
осим мене нема.
22Обратите се мени и бићете спасени,
сви крајеви земљини,
јер ја сам Божанство и другог нема.
23Заклињем се самим собом:
из мојих уста излази реч праведна
и нећу је опозвати:
да ће се преда мном свако колено савити,
сваки језик мноме заклињати.
24’Само у Господу имам – вели –
праведност и снагу.’“
К њему ће доћи и стидеће се
сви који су беснели против њега.
25У Господу ће имати
праведност и прослављање
све потомство Израиљево.