Yesaya 45 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 45:1-25

1Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake

Koresi amene anamugwira dzanja lamanja

kuti agonjetse mitundu ya anthu

ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo,

ndi kutsekula zitseko

kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:

2Ine ndidzayenda patsogolo pako,

ndi kusalaza mapiri;

ndidzaphwanya zitseko za mkuwa

ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.

3Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima,

katundu wa pamalo obisika,

kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova

Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.

4Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo,

chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli,

Ine ndakuyitana pokutchula dzina

ndipo ndakupatsa dzina laulemu

ngakhale iwe sukundidziwa Ine.

5Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina;

kupatula Ine palibenso Mulungu wina.

Ndidzakupatsa mphamvu,

ngakhale sukundidziwa Ine,

6kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo

anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha.

Ine ndine Yehova,

ndipo palibenso wina.

7Ndimalenga kuwala ndi mdima,

ndimabweretsa madalitso ndi tsoka;

ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.

8“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba;

mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo.

Dziko lapansi litsekuke,

ndipo chipulumutso chiphuke kuti

chilungamo chimereponso;

Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.

9“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake,

ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake.

Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti,

‘Kodi ukuwumba chiyani?’

Kodi ntchito yako inganene kuti,

‘Ulibe luso?’

10Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti,

‘Kodi munabereka chiyani?’

Kapena amayi ake kuti,

‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’

11“Yehova

Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena,

zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi:

Kodi iwe ukundifunsa za ana anga,

kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?

12Ndine amene ndinapanga dziko lapansi

ndikulenga munthu kuti akhalemo.

Ine ndi manja anga ndinayalika thambo;

ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.

13Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe:

ndipo ndidzawongolera njira zake zonse.

Iye adzamanganso mzinda wanga

ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo,

wopanda kupereka ndalama kapena mphotho,

akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

14Yehova akuti,

“Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu.

Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba

adzabwera kwa inu

ndipo adzakhala anthu anu;

iwo adzidzakutsatani pambuyo panu

ali mʼmaunyolo.

Adzakugwadirani

ndi kukupemphani, ponena kuti,

‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina;

palibenso mulungu wina.’ ”

15Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika

amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.

16Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa.

Adzakhala osokonezeka maganizo.

17Koma Yehova adzapulumutsa Israeli

ndi chipulumutso chamuyaya;

simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka

mpaka kalekale.

18Yehova

analenga zinthu zakumwamba,

Iye ndiye Mulungu;

amene akulenga dziko lapansi,

ndi kulikhazikitsa,

sanalipange kuti likhale lopanda kanthu,

koma analipanga kuti anthu akhalemo.

Iyeyu akunena kuti:

Ine ndine Yehova,

ndipo palibenso wina.

19Ine sindinayankhule mwachinsinsi,

pamalo ena a mdima;

Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti,

“Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.”

Ine Yehova, ndimayankhula zoona;

ndikunena zolungama.

20Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere;

yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina.

Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo,

amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.

21Fotokozani mlandu wanu,

mupatsane nzeru nonse pamodzi.

Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale?

Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana?

Kodi si Ineyo Yehova?

Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine,

Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa,

palibenso wina kupatula Ine.

22“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke,

inu anthu onse a pa dziko lapansi,

pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.

23Ndalumbira ndekha,

pakamwa panga patulutsa mawu owona,

mawu amene sadzasinthika konse akuti,

bondo lililonse lidzagwada pamaso panga;

anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.

24Iwo adzanene kwa Ine kuti,

‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’ ”

Onse amene anamuwukira Iye

adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.

25Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli

zidzapambana ndi kupeza ulemerero.

Hoffnung für Alle

Jesaja 45:1-25

Der Herr ruft Kyrus in seinen Dienst

1Gott hat Kyrus für eine besondere Aufgabe erwählt: Er wird ihn an seiner rechten Hand nehmen und ihm zum Sieg über viele Völker verhelfen; er wird die feindlichen Könige entwaffnen und ihm überall Tür und Tor öffnen.

So spricht der Herr zu Kyrus: 2»Ich gehe vor dir her und räume dir alle Hindernisse aus dem Weg. Ich zertrümmere die bronzenen Stadttore und zerbreche ihre eisernen Riegel. 3Die verborgenen Schätze und die versteckten Reichtümer gebe ich dir. Daran sollst du erkennen, dass ich der Herr bin, der Gott Israels, der dich, Kyrus, in seinen Dienst ruft. 4Warum berufe ich dich und verleihe dir einen Ehrentitel, obwohl du mich gar nicht kennst? Ich tue es für Israel, mein Volk, das ich erwählt habe, damit es mir dient. 5Ich bin der Herr, ich allein. Außer mir gibt es keinen Gott. Ich rüste dich aus für deinen Eroberungszug, auch wenn du mich nicht kennst.

6Der Westen und der Osten, ja, die ganze Welt soll daran erkennen, dass es außer mir keinen Gott gibt. Ich bin der Herr, ich allein. 7Ich bilde das Licht und schaffe die Finsternis; ich wirke den Frieden, und auch das Unglück lasse ich kommen. Ich bin der Herr, dies alles vollbringe ich. 8Ihr Wolken am Himmel, lasst Gerechtigkeit herabströmen; und du, Erde, sauge sie auf und lass Heil und Gerechtigkeit hervorsprießen! Ich, der Herr, bewirke dies alles.«

Wehe dem, der seinen Schöpfer anklagt!

9Wehe dem, der seinen Schöpfer anklagt! Er ist doch in Gottes Augen nicht mehr als ein Tonkrug unter vielen anderen. Fragt denn ein Tonklumpen den Töpfer: »Was tust du da mit mir?« Oder macht er sich lustig und sagt: »Mein Meister hat zwei linke Hände«? 10Wehe dem, der seinem Vater vorwirft: »Warum hast du mich gezeugt?«, und der Mutter: »Weshalb hast du mich in die Welt gesetzt?«!

11So spricht der Herr, der heilige Gott und Schöpfer Israels: »Wie könnt ihr nur in Frage stellen, was ich mit meinen Kindern vorhabe? Wollt ihr mir etwa vorschreiben, wie ich mit meinen eigenen Geschöpfen umgehen muss?45,11 Oder: Wenn ihr wissen wollt, was ich mit meinen Kindern vorhabe, dann kommt zu mir! Ich weiß, wie ich mit meinen eigenen Geschöpfen umgehen muss, darum vertraut euch mir an! 12Ich habe die Erde gemacht; und die Menschen, die darauf leben, habe ich geschaffen. Eigenhändig habe ich den Himmel ausgespannt wie ein Zelt und jedem einzelnen Stern seinen Platz zugewiesen. 13Ich bin es auch, der Kyrus berufen hat, meine gerechten Pläne in die Tat umzusetzen. Ich will ihm alle Hindernisse aus dem Weg räumen. Er wird meine Stadt Jerusalem wieder aufbauen und mein verschlepptes Volk freilassen, ohne Lösegeld oder Bestechungsgeschenke. Das verspreche ich, der Herr, der allmächtige Gott!«

Es gibt keinen Gott außer dem Herrn

14So spricht der Herr zu seinem Volk: »Die Ägypter und Äthiopier werden zu euch kommen und ihren ganzen Reichtum bringen, allen Gewinn aus ihren Handelsgeschäften. Auch die hochgewachsenen Leute aus Seba unterwerfen sich euch und werden eure Sklaven. In Ketten ziehen sie hinter euch her. Sie werden vor euch auf die Knie fallen und bekennen: ›Wirklich, nur bei euch ist Gott! Außer ihm gibt es keinen anderen.‹« 15Ja, Herr, du bist ein Gott, der sich verborgen hält, du Gott und Retter Israels. 16Schämen müssen sich alle, die Götterstatuen anfertigen! Sie enden mit Schimpf und Schande. 17Israel aber wird für alle Zeiten vom Herrn gerettet. Nie mehr müsst ihr euch schämen, in alle Ewigkeit werdet ihr bestehen.

18Der Herr ist der einzige Gott. Er ist es, der den Himmel geschaffen hat. Er gab der Erde ihre Form und legte ihre Fundamente. Nicht als einsame Wüste hat er sie gebildet, sondern als Wohnraum für seine Geschöpfe. Dieser Gott spricht: »Ich bin der Herr, außer mir gibt es keinen Gott. 19Ich habe nicht im Verborgenen geredet, nicht irgendwo im Dunkeln. Nie habe ich zu den Nachkommen von Jakob gesagt: ›Sucht mich vergeblich!‹ Ich bin der Herr, und was ich sage, das ist gerecht; was ich ankündige, das trifft ein!

20Kommt alle her, die ihr den Untergang eurer Völker überlebt habt! Tretet noch einmal zu einer Gerichtsverhandlung an! Wer hölzerne Götterfiguren herumträgt, hat keinen Verstand. Er fleht einen Gott an, der ihm nicht helfen kann. 21Berichtet von den Taten eurer Götter! Ja, beratet euch und bringt Beweise für ihre Gottheit vor! Wer hat vor langer Zeit angekündigt, was nun geschehen ist? Wer hat es längst vorausgesagt? War ich es nicht, der Herr? Es gibt keinen Gott außer mir, keinen, der gerecht ist und der rettet. Ich bin der einzige Gott.

22Kommt zu mir und lasst euch retten, ihr Menschen aus allen Winkeln der Erde! Denn ich bin der einzige Gott. 23Ich habe bei meinem Namen geschworen, ich sage die Wahrheit und nehme mein Wort nicht zurück: Vor mir werden alle niederknien, und alle werden bekennen: 24›Nur beim Herrn gibt es Rettung und Hilfe!‹«

Auch die, die den Herrn einmal gehasst haben, werden beschämt zu ihm kommen. 25Dann wird der Herr das Recht der Nachkommen Israels wiederherstellen, und sie werden ihn dafür preisen.