Yesaya 34 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 34:1-17

Chiweruzo cha Anthu a Mitundu Yonse

1Inu anthu a mitundu yonse, bwerani pafupi kuti mumve:

tcherani khutu, inu anthu a mitundu ina yonse:

Limvetsere dziko lapansi pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo,

dziko lonse pamodzi ndi zonse zochokera mʼmenemo!

2Yehova wayipidwa ndi anthu a mitundu yonse;

wapsera mtima magulu awo onse ankhondo.

Iye adzawawononga kotheratu,

nawapereka kuti aphedwe.

3Anthu awo ophedwa adzatayidwa kunja,

mitembo yawo idzawola ndi kununkha;

mapiri adzafiira ndi magazi awo.

4Dzuwa, mwezi ndi nyenyezi zidzasungunuka

ndipo mlengalenga mudzakulungidwa ngati chipepala;

nyenyezi zonse zidzayoyoka

ngati masamba ofota a mphesa,

ngati masamba onyala a mtengo wa mkuyu.

5Yehova akuti, “Lupanga langa lakhutiratu magazi kumwamba;

taonani, likutsika kudzalanga anthu a ku Edomu,

anthu amene ndawawononga kotheratu.”

6Lupanga la Yehova lakhuta magazi,

lakutidwa ndi mafuta;

magazi a ana ankhosa onenepa ndi ambuzi,

mafuta a ku impsyo za nkhosa zazimuna.

Pakuti Yehova ali ndi nsembe mu Bozira

ndiko kuphedwa kwa anthu ambiri mʼdziko la Edomu.

7Pamodzi ndi anthuwo zidzaphedwanso njati,

ngʼombe zazimuna zazingʼono ndi zazikulu zomwe.

Dziko lawo lidzakhala magazi okhaokha,

ndipo nthaka idzakutidwa ndi mafuta.

8Iyi ndi nthawi imene Yehova adzalipsira

ndi kulanga adani a Ziyoni.

9Madzi a mʼmitsinje ya Edomu adzasanduka phula,

ndipo fumbi lake lidzasanduka sulufule;

dziko lake lidzasanduka phula lamoto!

10Motowo sudzazimitsidwa usiku ndi usana;

utsi wake udzafuka kosalekeza.

Dzikolo lidzakhala chipululu pa mibado ndi mibado;

palibe ndi mmodzi yemwe amene adzadutsemo.

11Mʼdzikomo mudzakhala akabawi ndi anungu;

amantchichi ndi akhwangwala adzapanga zisa zawo mʼmenemo.

Mulungu adzatambalitsa pa Edomu

chingwe choyezera cha chisokonezo

ndi chingwe chowongolera cha chiwonongeko.

12Anthu olemekezeka ake sadzatchedwanso mfumu kumeneko;

akalonga ake onse adzachotsedwa.

13Minga idzamera mʼnyumba zake zankhondo zotetezedwa,

khwisa ndi mitungwi zidzamera mʼmalinga ake.

Ankhandwe azidzadya mʼmenemo;

malo okhalamo akadzidzi.

14Avumbwe adzakumana ndi afisi,

ndipo zirombo za mʼchipululu zizidzayitanizana.

Kumeneko kudzafikanso mizimu yoyipa

ndi kupeza malo opumulirako.

15Kadzidzi adzamangako chisa chake nʼkuyikirako mazira,

adzaswa ana ake ndi kusamalira ana ake mu mthunzi wa mapiko ake;

akamtema adzasonkhananso kumeneko,

awiriawiri.

16Funafunani mʼbuku la Yehova ndi kuwerenga:

mwa zolengedwazi palibe chimene chidzasowa;

sipadzakhala nʼchimodzi chomwe chopanda chinzake.

Pakuti Yehova walamula kuti zitero,

ndipo Mzimu wake udzawasonkhanitsa pamodzi.

17Yehova wagawa dziko lawo;

wapatsa chilichonse chigawo chake.

Dziko lidzakhala lawo mpaka muyaya

ndipo zidzakhala mʼmenemo pa mibado yonse.

Het Boek

Jesaja 34:1-17

Gods oordeel over zijn vijanden

1Kom hier en luister, volken van de aarde, laat de hele wereld en alles wat erop leeft, mijn woorden horen. 2Want de Here is toornig tegen de volken. Hij keert zijn toorn tegen hun legers. Hij zal hen volledig vernietigen en blootstellen aan een slachting. 3Hun doden zullen niet worden begraven en de stank van rottende lichamen zal het land vullen en hun bloed zal langs de berghellingen naar beneden vloeien. 4In die tijd wordt de hemel als een boekrol opgerold. De sterren zullen als bladeren vallen, net als het verwelkte blad van de wijnstok en het dorre gebladerte van de vijgenboom.

5In de hemel wordt het zwaard van de Here scherp gemaakt. Kijk, nu daalt het op Edom neer, het volk dat ik heb vervloekt. 6Het zwaard van de Here is bevlekt met bloed en druipt van vet, alsof het gebruikt is voor het slachten van lammeren en geiten voor de offerdienst. Want de Here zal een grote slachting aanrichten in Edom. 7Hun leger zal het onderspit delven, alsof het ging om wilde stieren en buffels. Het land zal worden doordrenkt met het bloed en de aarde zal glimmen van vet. 8Want het is de dag van de wraak, het jaar van vergelding voor wat Edom Israël heeft aangedaan. 9De rivieren van Edom zullen gevuld zijn met brandende pek en de grond zal met vuur zijn bedekt. 10Deze berechting van Edom zal nooit eindigen. De rook zal blijven opstijgen. Het land zal van generatie op generatie verlaten blijven liggen, nooit zal zich daar meer iemand vestigen. 11De pelikanen en roerdompen, uilen en raven zullen er voortaan leven. Want God zal de verwoesting breed uitmeten en de leegheid van het land vaststellen. Hij zal zijn edelen op de proef stellen en vaststellen dat niemand van hen het koningschap waard is. 12Het zal ‘Niemandsland’ worden genoemd en de vorsten van dat land zullen verdwenen zijn. 13Dorens zullen de paleizen overwoekeren en in de burchten zullen netels en distels groeien. Alleen jakhalzen en struisvogels zullen zich daar nog op hun gemak voelen. 14Er zullen wolven en hyenaʼs zijn. Hun gehuil zal klinken in de stilte van de nacht. De nachtmonsters zullen daar elkaars schreeuw beantwoorden en de boze geesten zullen daar komen rusten. 15De pijlslang zal haar eieren leggen, ze uitbroeden en haar jongen koesteren. Gieren zullen er komen, in paren. 16Zoek het op in het Boek van de Here en ontdek alles wat Hij zal gaan doen, Hij zal geen enkel detail vergeten, want de Here heeft het gezegd en zijn Geest zal zorgen dat het allemaal zo gebeurt. 17Hij heeft het land verkend en verdeeld onder die wezens, zij zullen het voor altijd bezitten, van generatie op generatie.