Yesaya 33 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 33:1-24

Msautso ndi Thandizo

1Tsoka kwa iwe, iwe wowonongawe,

amene sunawonongedwepo!

Tsoka kwa iwe, iwe mthirakuwiri,

iwe amene sunanyengedwepo!

Iwe ukadzaleka kuwononga,

udzawonongedwa,

ukadzasiya umʼthirakuwiri, adzakuwononga,

ndipo ukadzaleka kuchita zachinyengo adzakunyenga.

2Inu Yehova, mutikomere mtima ife;

tikulakalaka Inu.

Tsiku ndi tsiku mutitchinjirize ndi mkono wanu,

ndipo mutipulumutse pa nthawi ya masautso.

3Mukatulutsa liwu lanu longa bingu mitundu ya anthu imathawa;

pamene Inu mwadzambatuka mitundu ya anthu imabalalika.

4Zofunkha za ku nkhondo za mitundu ina Aisraeli adzazisonkhanitsa ngati mmene limachitira dzombe.

Iwo adzalumphira zofunkhazo monga mmene limachitira dzombe.

5Yehova wakwezeka kwambiri pakuti amakhala pamwamba pa zonse

adzadzaza Ziyoni ndi chilungamo ndi chipulumutso.

6Iye adzakupatsani mtendere pa nthawi yanu,

adzakupatsani chipulumutso chochuluka, nzeru zambiri ndi chidziwitso chochuluka;

kuopa Yehova ngati madalitso.

7Taonani, anthu awo amphamvu akulira mofuwula mʼmisewu;

akazembe okhazikitsa mtendere akulira kwambiri.

8Mʼmisewu yayikulu mulibe anthu,

mʼmisewu mulibe anthu a paulendo.

Mdaniyo ndi wosasunga pangano.

Iye amanyoza mboni.

Palibe kulemekezana.

9Dziko likulira ndipo likunka likutha.

Nkhalango ya Lebanoni ikuchita manyazi, yafota.

Chigwa cha chonde cha Saroni chasanduka chachidalala.

Masamba a mitengo ya ku Basani ndi Karimeli akuyoyoka.

10Yehova akunena kuti, “Tsopano ndidzadzambatuka

ndipo ndidzaonetsa mphamvu zanga,

ndipo ndidzakwezedwa.

11Zolingalira zanu nʼzachabechabe

ngati udzu wamanyowa.

Mpweya wamoto udzakupserezani.

12Anthu a mitundu ina adzatenthedwa ngati miyala ya njereza;

ndi ngati minga yodulidwa.”

13Inu amene muli kutali, imvani zimene ndachita;

inu amene muli pafupi, dziwani mphamvu zanga

14Mu mzinda wa Ziyoni anthu ochimwa agwidwa ndi mantha;

anthu osapembedza Mulungu akunjenjemera:

Iwo akunena kuti, “Ndani wa ife angathe kukhala mʼmoto wonyeketsa?

Ndani wa ife angathe kukhala moto wosatha?”

15Angathe kuti ndi amene amachita zolungama

ndi kuyankhula zoona,

amene amakana phindu lolipeza monyenga

ndipo salola manja ake kulandira ziphuphu,

amene amatseka makutu ake kuti angamve mawu opangana kupha anzawo

ndipo amatsinzina kuti angaone zoyipa.

16Munthu wotere ndiye adzakhale pa nsanja,

kothawira kwake kudzakhala mʼmalinga a mʼmapiri.

Azidzalandira chakudya chake

ndipo madzi sadzamusowa.

17Nthawi imeneyo maso a ana adzaona mfumu ya maonekedwe wokongola

ndi kuona dziko lotambasukira kutali.

18Mu mtima mwanu muzidzalingalira zoopsa zinachitika kale zija:

“Ali kuti mkulu wa Asilikali uja?

Ali kuti wokhometsa misonkho uja?

Ali kuti mkulu woyangʼanira nsanja?”

19Simudzawaonanso anthu odzikuza aja,

anthu aja achiyankhulo chosadziwika,

chachilendo ndi chosamveka.

20Taonani Ziyoni, mzinda wa zikondwerero zachipembedzo chathu;

maso anu adzaona Yerusalemu,

mzinda wamtendere, tenti imene sidzachotsedwa,

zikhomo zake sizidzazulidwa,

kapena zingwe zake kuduka.

21Kumeneko Yehova adzaonetsa ulemerero wake

ndipo mzindawo udzakhala kasupe wa mitsinje yayikulu.

Ngalawa za zopalasa sizidzapitamo,

sitima zapamadzi zikuluzikulu sizidzayendamo.

22Pakuti Yehova ndi woweruza wathu,

Yehova ndiye wotilamulira,

Yehova ndiye mfumu yathu;

ndipo ndiye amene adzatipulumutse.

23Zingwe za sitima zapamadzi za adani athu zamasuka,

sizikutha kulimbitsa mlongoti wake,

matanga ake sakutheka kutambasuka.

Ngakhale tidzagawana zofunkha zochuluka kwambiri

ndipo ngakhale olumala adzatenga zofunkhazo.

24Palibe ndi mmodzi yemwe wokhala mʼZiyoni adzanene kuti, “Ndikudwala”

ndipo anthu onse okhala mʼmenemo machimo awo adzakhululukidwa.

Luganda Contemporary Bible

Isaaya 33:1-24

133:1 a Kbk 2:8; Mat 7:2 b Is 21:2Zikusanze ggwe omuzikiriza

ggwe atazikirizibwanga.

Zikusanze ggwe alya olukwe mu balala,

ggwe, gwe batalyangamu lukwe,

bw’olirekaraawo okuzikiriza,

olizikirizibwa.

Bw’olirekeraawo okulya mu balala olukwe,

balikulyamu olukwe.

233:2 a Is 40:10; 51:9; 59:16 b Is 25:9Ayi Mukama tusaasire,

tukuyaayaanira.

Obeere amaanyi gaffe buli makya,

obulokozi bwaffe mu biro eby’okulabiramu ennaku.

333:3 Is 59:16-18Olw’eddoboozi ery’okubwatuka, abantu balidduka,

bw’ogolokoka, amawanga gasaasaana.

4Omunyago gwo, gukungulwa enzige ento,

era abantu bagugwako ng’ekibinja ky’enzige.

533:5 a Zab 97:9 b Is 28:6 c Is 1:26Mukama agulumizibwe, kubanga atuula waggulu,

alijjuza Sayuuni n’obwenkanya n’obutuukirivu.

633:6 a Is 51:6 b Is 11:2-3; Mat 6:33Y’aliba omusingi omugumu mu biro byo,

nga lye tterekero eggagga ery’obulokozi, n’amagezi n’okumanya.

Okutya Mukama kye kisumuluzo kye tterekero ly’obugagga obwo.

733:7 2Bk 18:37Laba abasajja abazira ab’amaanyi bakaabira mu nguudo mu ddoboozi ery’omwanguka,

n’ababaka ab’emirembe bakaaba nnyo.

833:8 Bal 5:6; Is 35:8Enguudo ennene tezitambulirwako,

tewali azitambulirako.

Endagaano yamenyebwa,

n’abajulizi baayo banyoomebwa,

tewali assibwamu kitiibwa.

933:9 a Is 3:26 b Is 2:13; 35:2 c Is 24:4Ensi ekungubaga era eyongobera,

Lebanooni aswadde era awotose;

Saloni ali ng’eddungu,

ng’asuula Basani ne Kalumeeri.

1033:10 Zab 12:5; Is 2:21Mukama agamba nti, “Kaakano nnaagolokoka,

kaakano nnaagulumizibwa,

kaakano nnaayimusibwa waggulu.

1133:11 a Zab 7:14; Is 59:4; Yak 1:15 b Is 26:18 c Is 1:31Ofuna olubuto olw’ebisusunku,

ozaala ssubi,

omukka gwo, muliro ogukusaanyaawo.

1233:12 Is 10:17Abantu balyokebwa nga layimu bw’ayokebwa,

balyokebwa omuliro ng’ebisaka by’amaggwa amasale.”

1333:13 a Zab 48:10; 49:1 b Is 49:1Mmwe abali ewala, mutegeere kye nkoze.

Mmwe abali okumpi, mukkirize amaanyi gange.

1433:14 a Is 32:11 b Is 30:30; Beb 12:29Abakozi b’ebibi ab’omu Sayuuni batidde,

okutya kujjidde abatalina Katonda.

“Ani ku ffe ayinza okubeera awamu n’omuliro ogusaanyaawo?

Ani ku ffe ayinza okubeera awamu n’omuliro ogutaliggwaawo?”

1533:15 a Is 58:8 b Zab 15:2; 24:4 c Zab 119:37Atambulira mu butuukirivu,

n’ayogera ebituufu,

oyo atatwala magoba agava mu bubbi,

n’akuuma emikono gye obutakkiriza nguzi,

aziba amatu ge n’atawulira ntegeka za kutta,

n’aziba amaaso ge obutalaba nteekateeka ezitali za butuukirivu,

1633:16 a Is 25:4 b Is 26:1 c Is 49:10ye muntu alituula waggulu mu bifo ebya waggulu,

n’obuddukiro bwe buliba ebigo eby’omu nsozi.

Aliweebwa emmere,

n’amazzi tegalimuggwaako.

1733:17 a Is 6:5 b Is 26:15Amaaso go galiraba kabaka mu bulungi bwe,

ne galaba ensi eyeewala.

1833:18 Is 17:14Omutima gwo gulifumiitiriza ku ntiisa ng’ogamba nti,

“Omukungu omukulu ali ludda wa?

Ali ludda wa eyasoloozanga omusolo?

Omukungu avunaanyizibwa eminaala ali ludda wa?”

1933:19 Is 28:11; Yer 5:15Toliddayo kulaba bantu abo ab’amalala,

abantu ab’olulimi olutamanyiddwa,

olulimi olutategeerekeka.

2033:20 a Is 32:18 b Zab 46:5; 125:1-2Tunuulira Sayuuni ekibuga eky’embaga zaffe,

amaaso go galiraba Yerusaalemi,

ekifo eky’emirembe, eweema etalisimbulwa

enkondo zaayo tezirisimbulwa,

newaakubadde emiguwa gyayo okukutulwa.

2133:21 Is 41:18; 48:18; 66:12Weewaawo Mukama aliba Amaanyi gaffe

era aliba ekifo eky’emigga emigazi n’ensulo engazi.

Temuliyitamu lyato

newaakubadde ekyombo ekinene tekiriseeyeeyeramu.

2233:22 a Is 11:4 b Is 2:3; Yak 4:12 c Zab 89:18 d Is 25:9Kubanga Mukama ye mulamuzi waffe,

Mukama y’atuwa amateeka,

Mukama ye Kabaka waffe,

y’alitulokola.

2333:23 a 2Bk 7:8 b 2Bk 7:16Emiguwa gyo gisumulukuse

n’omulongooti si munywevu,

n’ettanga si lyanjuluze.

Awo omugabo omungi guligabanyizibwamu,

n’abalala balitwala eby’omunyago.

2433:24 a Is 30:26 b Yer 50:20; 1Yk 1:7-9Tewali abeera mu Sayuuni alyogera nti, “Ndi mulwadde,”

n’abo ababeeramu balisonyiyibwa ekibi kyabwe.