Yesaya 3 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 3:1-26

Chiweruzo pa Yerusalemu ndi Yuda

1Taonani tsopano, Ambuye

Yehova Wamphamvuzonse,

ali pafupi kuchotsa mu Yerusalemu ndi mu Yuda

zinthu pamodzi ndi thandizo;

adzachotsa chakudya chonse ndi madzi onse,

2anthu amphamvu ndi asilikali ankhondo,

oweruza ndi aneneri,

anthu olosera ndi akuluakulu,

3atsogoleri a ankhondo makumi asanu ndi anthu olemekezeka,

aphungu ndi anthu amatsenga ndi akatswiri pa za kulosera.

4Ndidzawayikira anyamata kuti akhale mafumu awo;

ana akhanda ndiwo adzawalamulire.

5Anthu adzazunzana,

munthu ndi munthu mnzake, mnansi ndi mnansi wake.

Anthu wamba adzanyoza

akuluakulu.

6Munthu adzagwira mʼbale wake

mʼnyumba ya abambo awo, ndipo adzati,

“Iwe uli nawo mwinjiro, ndiye ukhale mtsogoleri wathu;

lamulira malo opasuka ano!”

7Koma tsiku limenelo mʼbale wakeyo adzafuwula kuti,

“Ayi, mavuto oterewa ndilibe mankhwala ake.

Ndilibe chakudya kapena chovala mʼnyumba mwanga;

musasankhe ine kukhala mtsogoleri wa anthu.”

8Yerusalemu akudzandira,

Yuda akugwa;

zokamba zawo ndi ntchito zawo nʼzotsutsana ndi Yehova,

sakulabadira ulemerero wa Mulungu.

9Maonekedwe a nkhope zawo amawatsutsa;

amaonetsera poyera tchimo lawo ngati Sodomu;

salibisa tchimo lawolo.

Tsoka kwa iwo

odziputira okha mavuto.

10Nena kwa olungama kuti zonse zidzawayendera bwino,

pakuti adzakondwera ndi phindu la ntchito zawo.

11Tsoka kwa anthu oyipa! Mavuto ali pa iwo!

Adzalandira malipiro a zimene manja awo anachita.

12Achinyamata akupondereza anthu anga,

ndipo amene akuwalamulira ndi akazi.

Aa, anthu anga, atsogoleri anu akukusocheretsani;

akukuchotsani pa njira yanu.

13Yehova wakhala pamalo pake mʼbwalo la milandu;

wakonzeka kuti aweruze anthu ake.

14Yehova akuwazenga milandu

akuluakulu ndi atsogoleri a anthu ake:

“Ndinu amene mwawononga munda wanga wa mpesa;

nyumba zanu zadzaza ndi zolanda kwa amphawi.

15Nʼchifukwa chiyani inu mukupsinja anthu anga,

nʼkudyera masuku pamutu amphawi?”

Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.

16Yehova akunena kuti,

“Akazi a ku Ziyoni ngodzikuza kwambiri,

akuyenda atakweza makosi awo,

akukopa amuna ndi maso awo

akuyenda monyangʼama

akuliza zigwinjiri za mʼmiyendo yawo

17Nʼchifukwa chake Ambuye, adzatulutsa zipere pa mitu ya akazi a ku Ziyoniwo;

Yehova adzachititsa dazi mitu yawo.”

18Tsiku limenelo Ambuye adzawachotsera zodzikongoletsera zawo: za mʼmiyendo, za ku mutu za mʼkhosi, 19ndolo ndi zibangiri, nsalu zophimba pa nkhope, 20maduku, zigwinjiri za mʼmiyendo ndi malamba, mabotolo a zonunkhira ndi zithumwa, 21mphete ndi zipini, 22zovala za pa mphwando, zipewa ndi mwinjiro, zikwama, 23magalasi oyangʼanira, zovala zosalala, nduwira ndiponso nsalu za mʼmapewa.

24Mʼmalo mwa kununkhira azidzanunkha,

mʼmalo mwa lamba, adzavala chingwe;

mʼmalo mwa tsitsi lopesa bwino, adzakhala ndi dazi;

mʼmalo mwa zovala zabwino, adzavala chiguduli;

mʼmalo mwa kunyadira kukongola adzachita manyazi.

25Iwe Yerusalemu anthu ako aamuna adzaphedwa ndi lupanga,

asilikali ako adzafera ku nkhondo.

26Pa zipata za Ziyoni padzakhala kubuma ndi kulira;

Iweyo udzasakazidwa nʼkukhala pansi, ukugubuduzika pa fumbi.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

以赛亚书 3:1-26

对耶路撒冷和犹大的审判

1主——万军之耶和华要从耶路撒冷犹大拿去众人倚靠的一切:粮食、水、

2英雄、战士、审判官、先知、

占卜者、长老、

3五十夫长、显贵、谋士、巧匠和巫师。

4主必使少儿做他们的首领,

让孩童治理他们。

5百姓将彼此欺凌,

邻居互相争斗,

少年目无尊长,

卑贱者欺尊犯上。

6那时,人会拉住一位同族的弟兄说:

“你至少还有件像样的衣服,

你就做我们的首领吧,

这废墟之地就交给你了!”

7但那人必高声说:

“我救不了你们。

我家中无衣无食,

不要让我做首领。”

8耶路撒冷必崩溃,

犹大必败落,

因为他们的言行冒犯耶和华,

蔑视荣耀的主。

9他们的表情显出他们心术不正,

他们跟所多玛人一样对自己的罪恶津津乐道,

毫不隐瞒。

他们必大祸临头,自招毁灭。

10要告诉义人:他们有福了,

必得善报。

11恶人有祸了!他们必大祸临头,

受到报应。

12耶和华说:“我的子民啊!

孩童欺压你们,

妇女管辖你们。

你们的首领领你们入迷途,

带你们走歧路。”

13耶和华准备就绪,

要审判祂的子民。

14祂必审问祂子民中的长老和首领,对他们说:

“你们毁坏了我的葡萄园——我的子民,

家里堆满了从穷人那里掠夺的东西。

15你们为何压榨我的子民,

虐待贫穷人?”

这是主——万军之耶和华说的。

16耶和华又说:

锡安的女子狂傲,

昂首走路,卖弄媚眼,

俏步徐行,脚镯叮当。

17所以,我要使她们头上长疮,

露出头皮。”

18到那日,主必拿去她们美丽的脚镯、发饰、项链、 19耳环、手镯、面纱、 20头饰、脚链、彩带、香盒、护身符、 21戒指、鼻环、 22礼服、外袍、披肩、钱包、 23镜子、内衣、头巾和围巾。

24她们的香气将变成臭味,

腰带将变成绳子,

美发将变成秃头,

华服将变成麻衣,

美丽的容颜将布满羞辱的烙印。

25城中的男子将丧身刀下,

勇士将战死沙场。

26锡安的城门必悲伤、哀哭,

锡安必空空地坐在地上。