Yesaya 28 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 28:1-29

Tsoka kwa Efereimu

1Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu.

Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa

limene lili pa mutu pa anthu

oledzera a mʼchigwa chachonde.

2Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga.

Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga,

ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho;

ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.

3Ulamuliro wa atsogoleri oledzera

a ku Efereimu adzawuthetsa.

4Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa

lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja,

udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa

imene munthu akangoyiona amayithyola

nthawi yokolola isanakwane.

5Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse

adzakhala ngati nkhata yaufumu,

chipewa chokongola

kwa anthu ake otsala.

6Iye adzapereka mtima

wachilungamo kwa oweruza,

adzakhala chilimbikitso kwa

amene amabweza adani pa zipata za mzinda.

7Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo

ndipo akusochera chifukwa cha mowa:

ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa

ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo;

akusochera chifukwa cha mowa,

akudzandira pamene akuona masomphenya,

kupunthwa pamene akupereka chigamulo.

8Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha

ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.

9Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani?

Uthengawu akufuna kufotokozera yani?

Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa,

kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?

10Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono

lemba ndi lemba, mzere ndi mzere,

phunziro ndi phunziro.

Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”

11Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino.

Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene

12anakuwuzani kuti,

“Malo opumulira ndi ano,

otopa apumule, malo owusira ndi ano.”

Koma inu simunamvere.

13Choncho Yehova adzakuphunzitsani

pangʼonopangʼono lemba ndi lemba,

mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro.

Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo,

adzapweteka ndi kukodwa mu msampha

ndipo adzakutengani ku ukapolo.

14Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova,

inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.

15Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa,

ife tachita mgwirizano ndi manda.

Pamene mliri woopsa ukadzafika

sudzatikhudza ife,

chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu

ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.”

16Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi:

“Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri

ngati maziko mu Ziyoni,

mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu;

munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.

17Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake,

ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere;

matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza,

ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.

18Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa;

mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa.

Pakuti mliri woopsa udzafika,

ndipo udzakugonjetsani.

19Ndipo ukadzangofika udzakutengani.

Udzafika mmawa uliwonse,

usiku ndi usana.”

Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu

adzaopsedwa kwambiri.

20Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo;

ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.

21Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu

adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni;

adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo,

ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.

22Tsopano lekani kunyoza,

mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri;

Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti,

“Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”

23Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga;

mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.

24Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha?

Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?

25Pamene iye wasalaza mundawo,

kodi samafesa mawere ndi chitowe?

Kodi suja samadzala tirigu

ndi barele mʼmizere yake,

nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?

26Mulungu wake amamulangiza

ndi kumuphunzitsa njira yabwino.

27Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero,

kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta;

mawere amapuntha ndi ndodo

ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.

28Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi,

komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke.

Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta,

koma akavalo ake satekedza tiriguyo.

29Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse,

wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.

Het Boek

Jesaja 28:1-29

Gods profetie over Samaria

1Wee de stad Samaria, omringd door haar vruchtbare vallei. Samaria, de trots en vreugde van de dronkaards van Israël! Wee haar schoonheid, de gekroonde glorie van dronkaards, het is een bloem die verwelkt! 2De Here is sterk en machtig, Hij is als een hagelstorm, een vernietigende orkaan, als een alles wegspoelende vloedgolf, Hij zet de hele aarde naar zijn hand. 3Eens zal de oogstrelende schoonheid van Samaria, omringd door een vruchtbare vallei, plotseling verdwenen zijn. 4Zij zal gretig worden weggeplukt, zoals een vroege vijg wordt weggeplukt en gretig opgegeten!

5Uiteindelijk zal dan de Here van de hemelse legers Zelf hun gekroonde glorie zijn, de prachtige diadeem voor wie er van zijn volk zijn overgebleven. 6Hij zal de rechters een verlangen naar rechtvaardigheid geven en grote moed aan de soldaten die bij de poort weten stand te houden.

7Maar ook Jeruzalem wordt door dronkaards geleid! Haar priesters en profeten wankelen en waggelen. Zij maken domme fouten en begaan grote vergissingen. 8Hun tafels liggen vol met braaksel, overal ligt vuil. 9‘Wie denkt Jesaja wel dat hij is,’ zeggen de mensen, ‘om op zoʼn toon tegen ons te spreken! Zijn wij soms kleine kinderen, net oud genoeg om te praten? 10Hij vertelt ons steeds weer hetzelfde, gebod op gebod, regel op regel, dan weer dit en dan weer dat!’

11Werkelijk, om tot dit volk te spreken zal God buitenlanders sturen, mensen die in onverstaanbare talen spreken! 12Zij zouden rustig kunnen leven in hun eigen land, maar zij wilden niet naar Hem luisteren. 13De Here zal het daarom steeds opnieuw voor hen uitspellen. Het keer op keer in simpele bewoordingen vertellen, elke keer als Hij de kans heeft. Maar toch zullen zij over deze simpele en oprechte boodschap struikelen en vallen. Zij zullen worden gebroken en vertrapt en gevangengenomen.

14Luister daarom goed naar de woorden van de Here, spottende heersers in Jeruzalem. 15U zegt: ‘Wij hebben een afspraak gemaakt met de dood en een verdrag met het dodenrijk, om gedekt te zijn tegen de stormvloed die over ons komt. Wij hebben de leugen als een schuilplaats en verstoppen ons achter bedrog.’

16Maar de Here God zegt: ‘Kijk, Ik plaats een steen als fundament in Sion, een kostbare hoeksteen die Ik heb uitgekozen, en wie zijn vertrouwen daarin stelt, hoeft nooit meer een andere toevlucht te zoeken. 17Ik zal met het meetsnoer en het paslood van de rechtvaardigheid het fundament dat u maakte, controleren. Het ziet er wel goed uit, maar de hagelstorm van Assur zal die onbetrouwbare schuilplaats vernietigen, als een watervloed zal hij het wegvagen. 18Ik zal uw verbond met de dood en het dodenrijk tenietdoen, zodat u in de grond wordt gestampt als de vijand uw land binnenstormt.

19Steeds weer zal die stormvloed komen opzetten en u meevoeren, totdat uiteindelijk de vreselijke waarheid van mijn waarschuwingen tot u zal doordringen.’

20Het bed dat u hebt gemaakt, is veel te kort om op te liggen, de dekens zijn te smal om u te bedekken. 21De Here zal plotseling in toorn verschijnen, net als op de berg Perazim en in het dal bij Gibeon, om iets vreemds en ongewoons te doen. 22Spot daarom niet meer, anders wordt uw straf alleen maar zwaarder. Want God, de Here van de hemelse legers, heeft mij duidelijk gezegd dat Hij vastbesloten is het land te vernietigen.

23-24 Luister naar mij, luister eens heel goed: ploegt een boer voortdurend zijn land zonder te zaaien? Blijft hij de aarde eggen, zonder gewas in te planten? 25Plant hij uiteindelijk niet verschillende soorten kruiden en koren, elk op een apart stuk grond? 26Hij weet precies wat hij moet doen, want God heeft het hem laten zien en begrijpen. 27Hij dorst niet alles op dezelfde manier. Voor dille wordt geen dorsslede gebruikt, maar een stok. Komijn wordt niet gedorst met een wagenrad, maar met een roede, heel voorzichtig. 28Koren voor brood wordt niet helemaal geplet, maar alleen kort gedorst. 29Zo zal ook Here van de hemelse legers in zijn wijsheid niet eindeloos, zonder maat, straffen.