Yesaya 26 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 26:1-21

Nyimbo ya Matamando

1Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi.

Tili ndi mzinda wolimba.

Mulungu amawuteteza ndi zipupa

ndi malinga.

2Tsekulani zipata za mzinda

kuti mtundu wolungama

ndi wokhulupirika ulowemo.

3Inu mudzamupatsa munthu

wa mtima wokhazikika

mtendere weniweni.

4Mudalireni Yehova mpaka muyaya,

chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.

5Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba,

iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula,

amagumula makoma ake

ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.

6Mapazi a anthu akuwupondereza,

mapazi a anthu oponderezedwa,

mapazi anthu osauka.

7Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza,

Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.

8Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama,

ife timayembekezera Inu;

mitima yathu imakhumba kukumbukira

ndi kulemekeza dzina lanu.

9Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse;

nthawi yammawa ndimafunafuna Inu.

Pamene muweruza dziko lapansi

anthu amaphunzira kuchita chilungamo.

10Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa,

saphunzira chilungamo.

Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo,

ndipo sazindikira ululu wa Yehova.

11Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange,

koma iwo sakuliona dzanjalo.

Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu;

ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.

12Yehova, mumatipatsa mtendere;

ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.

13Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu,

koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.

14Iwo tsopano sadzadzukanso;

mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa

pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga;

palibenso amene amawakumbukira.

15Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu;

mwauchulukitsa ndithu

ndipo mwalandirapo ulemu;

mwaukuza mbali zonse za dziko.

16Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso;

pamene munawalanga,

iwo anapemphera kwa Inu.

17Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira

amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu,

ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.

18Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana,

koma sitinapindulepo kanthu,

kapena kupulumutsa dziko lapansi;

sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.

19Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo;

matupi awo adzadzuka.

Iwo amene ali ku fumbi tsopano

adzadzuka ndi kuyimba mosangalala.

Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera,

momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.

20Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu

ndipo mukadzitsekere;

mukabisale kwa kanthawi kochepa

mpaka ukali wake utatha.

21Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala;

akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo.

Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo;

dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.