Yesaya 25 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 25:1-12

Nyimbo Yotamanda Yehova

1Yehova ndinu Mulungu wanga;

ine ndidzakukwezani ndi kutamanda dzina lanu,

pakuti mwachita zodabwitsa

zimene munakonzekeratu kalekale

mokhulupirika kwambiri.

2Inu mwasandutsa mzinda uja kukhala mulu wamiyala.

Ndipo mzinda wamalinga wasanduka bwinja,

linga la anthu achilendo lero si mzindanso

ndipo sidzamangidwanso.

3Nʼchifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani;

mizinda ya mitundu ya anthu ankhanza idzakuopani.

4Inu mwakhala ngati populumukira pa anthu osauka,

mwakhala ngati kobisalirako munthu wovutika pa nthawi ya masautso ake.

Mwakhala ngati pobisalirapo

pa nthawi ya mphepo yamkuntho ndi mthunzi pa nthawi ya dzuwa.

Pakuti anthu ankhanza

ali ngati mphepo yamkuntho yowomba pa khoma,

5ndiponso ngati kutentha mʼdziko lowuma.

Inu mumaletsa phokoso la anthu achilendo.

Monga momwe mthunzi wa mtambo umachepetsa kutentha,

inu munaletsa nyimbo za anthu ankhanza.

6Pa phiri ili Yehova Wamphamvuzonse adzakonzera

anthu a mitundu yonse madyerero a zakudya zokoma ndi vinyo wabwino.

Phwando la nyama yonona

ndi vinyo wabwino kwambiri.

7Iye adzachotsa kulira

kumene kwaphimba anthu ngati nsalu.

Adzachotsa chinsalu chimene chakuta mitundu yonse ya anthu.

8Yehova adzathetsa imfa mpaka muyaya,

Ambuye Yehova adzapukuta misozi mʼmaso

mwa munthu aliyense;

adzachotsa manyazi a anthu ake

pa dziko lonse lapansi,

Yehova wayankhula.

9Tsiku limenelo iwo adzati,

“Ndithudi, uyu ndiye Mulungu wathu;

ife tinamudalira ndipo anatipulumutsa.

Uyu ndiye Yehova, ife tinamudalira;

tiyeni tikondwe ndi kusangalala chifukwa watipulumutsa.”

10Yehova adzateteza phiri limeneli ndi dzanja lake;

ndipo Amowabu adzawapondereza pomwe alilipo,

ngati mmene amapondera manyowa mʼdzenje.

11Amowabuwo adzatambasula manja awo mʼmenemo,

ngati mmene amachitira munthu wosambira.

Koma Mulungu adzathetsa kunyada kwawo

ngakhale luso la manja awo.

12Iye adzagumula malinga awo ataliatali

ndipo adzawagwetsa

ndi kuwaponya pansi,

pa fumbi penipeni.

New International Version – UK

Isaiah 25:1-12

Praise to the Lord

1Lord, you are my God;

I will exalt you and praise your name,

for in perfect faithfulness

you have done wonderful things,

things planned long ago.

2You have made the city a heap of rubble,

the fortified town a ruin,

the foreigners’ stronghold a city no more;

it will never be rebuilt.

3Therefore strong peoples will honour you;

cities of ruthless nations will revere you.

4You have been a refuge for the poor,

a refuge for the needy in their distress,

a shelter from the storm

and a shade from the heat.

For the breath of the ruthless

is like a storm driving against a wall

5and like the heat of the desert.

You silence the uproar of foreigners;

as heat is reduced by the shadow of a cloud,

so the song of the ruthless is stilled.

6On this mountain the Lord Almighty will prepare

a feast of rich food for all peoples,

a banquet of aged wine –

the best of meats and the finest of wines.

7On this mountain he will destroy

the shroud that enfolds all peoples,

the sheet that covers all nations;

8he will swallow up death for ever.

The Sovereign Lord will wipe away the tears

from all faces;

he will remove his people’s disgrace

from all the earth.

The Lord has spoken.

9In that day they will say,

‘Surely this is our God;

we trusted in him, and he saved us.

This is the Lord, we trusted in him;

let us rejoice and be glad in his salvation.’

10The hand of the Lord will rest on this mountain;

but Moab will be trampled in their land

as straw is trampled down in the manure.

11They will stretch out their hands in it,

as swimmers stretch out their hands to swim.

God will bring down their pride

despite the cleverness25:11 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain. of their hands.

12He will bring down your high fortified walls

and lay them low;

he will bring them down to the ground,

to the very dust.