Yesaya 17 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 17:1-14

Uthenga Wotsutsa Damasiko

1Uthenga wonena za Damasiko:

“Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda,

koma udzasanduka bwinja.

2Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu

ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi

popanda wina woziopseza.

3Ku Efereimu sikudzakhalanso linga,

ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu;

Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu

monga anthu a ku Israeli,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

4“Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira;

ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.

5Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu

umene anatsiriza kukolola.

Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu

anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.

6Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale

monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni

kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi

mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,”

akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.

7Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo

ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.

8Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe,

ntchito ya manja awo,

ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera,

ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.

9Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.

10Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu;

simunakumbukire Thanthwe, linga lanu.

Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino,

ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,

11nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo

ndi kuphukira maluwa mmawa mwake,

komabe zimenezi sizidzakupindulirani

pa tsiku la mavuto.

12Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri,

akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja!

Aa, phokoso la anthu a mitundu ina,

akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!

13Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri,

koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula.

Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri,

ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.

14Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika,

ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa.

Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu,

gawo la amene amatibera zinthu zathu.

New International Version – UK

Isaiah 17:1-14

A prophecy against Damascus

1A prophecy against Damascus:

‘See, Damascus will no longer be a city

but will become a heap of ruins.

2The cities of Aroer will be deserted

and left to flocks, which will lie down,

with no-one to make them afraid.

3The fortified city will disappear from Ephraim,

and royal power from Damascus;

the remnant of Aram will be

like the glory of the Israelites,’

declares the Lord Almighty.

4‘In that day the glory of Jacob will fade;

the fat of his body will waste away.

5It will be as when reapers harvest the standing corn,

gathering the corn in their arms –

as when someone gleans ears of corn

in the Valley of Rephaim.

6Yet some gleanings will remain,

as when an olive tree is beaten,

leaving two or three olives on the topmost branches,

four or five on the fruitful boughs,’

declares the Lord, the God of Israel.

7In that day people will look to their Maker

and turn their eyes to the Holy One of Israel.

8They will not look to the altars,

the work of their hands,

and they will have no regard for the Asherah poles17:8 That is, wooden symbols of the goddess Asherah

and the incense altars their fingers have made.

9In that day their strong cities, which they left because of the Israelites, will be like places abandoned to thickets and undergrowth. And all will be desolation.

10You have forgotten God your Saviour;

you have not remembered the Rock, your fortress.

Therefore, though you set out the finest plants

and plant imported vines,

11though on the day you set them out, you make them grow,

and on the morning when you plant them, you bring them to bud,

yet the harvest will be as nothing

in the day of disease and incurable pain.

12Woe to the many nations that rage –

they rage like the raging sea!

Woe to the peoples who roar –

they roar like the roaring of great waters!

13Although the peoples roar like the roar of surging waters,

when he rebukes them they flee far away,

driven before the wind like chaff on the hills,

like tumble-weed before a gale.

14In the evening, sudden terror!

Before the morning, they are gone!

This is the portion of those who loot us,

the lot of those who plunder us.