Yesaya 17 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 17:1-14

Uthenga Wotsutsa Damasiko

1Uthenga wonena za Damasiko:

“Taonani, mzinda wa Damasiko sudzakhalanso mzinda,

koma udzasanduka bwinja.

2Mizinda ya Aroeri idzakhala yopanda anthu

ndipo idzakhala ya ziweto, zimene zidzagona pansi

popanda wina woziopseza.

3Ku Efereimu sikudzakhalanso linga,

ndipo ku Damasiko sikudzakhalanso ufumu;

Otsalira a ku Siriya adzachotsedwa ulemu

monga anthu a ku Israeli,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

4“Tsiku limenelo ulemerero wa Yakobo udzazimirira;

ndipo chuma chake chidzasanduka umphawi.

5Israeli adzakhala ngati munda wa tirigu

umene anatsiriza kukolola.

Adzakhalanso ngati munda wa mʼchigwa cha Refaimu

anthu atatha kukunkha ngala za tirigu.

6Komabe Aisraeli ochepa okha ndiwo ati adzatsale

monga mʼmene zimatsalira zipatso ziwiri kapena zitatu pa nthambi ya pamwamba penipeni

kapena zipatso zisanu pa nthambi za mʼmunsi

mwa mtengo wa olivi akawugwedeza,”

akutero Yehova, Mulungu wa Israeli.

7Tsiku limenelo anthu adzayangʼana Mlengi wawo

ndipo adzatembenukira kwa Woyerayo wa Israeli.

8Iwo sadzakhulupiriranso maguwa ansembe,

ntchito ya manja awo,

ndipo sadzadaliranso mitengo ya mafano a Asera,

ndiponso maguwa ofukizirapo lubani amene manja awo anapanga.

9Tsiku limenelo mizinda yawo yamphamvu, imene anasiya chifukwa cha Aisraeli, idzakhala ngati malo osiyidwa kuti awirire ndi kumera ziyangoyango. Ndipo yonse idzakhala mabwinja.

10Inu mwayiwalatu Mulungu Mpulumutsi wanu;

simunakumbukire Thanthwe, linga lanu.

Choncho, ngakhale munadzala mbewu zabwino,

ndi kuyitanitsa kunja mitengo ya mpesa,

11nimuyembekeza kuti zikule tsiku lomwelo

ndi kuphukira maluwa mmawa mwake,

komabe zimenezi sizidzakupindulirani

pa tsiku la mavuto.

12Aa, mkokomo wa anthu a mitundu yambiri,

akusokosa ngati kukokoma kwa nyanja!

Aa, phokoso la anthu a mitundu ina,

akusokosa ngati mkokomo wa madzi amphamvu!

13Ngakhale ankhondo a mitundu ina akubwera ndi mkokomo ngati wa madzi ambiri,

koma adzathawira kutali Mulungu akadzawadzudzula.

Yehova adzawapirikitsa ngati mankhusu owuluka ndi mphepo pa phiri,

ndi ngati fumbi la kamvuluvulu asanayambe.

14Pofika nthawi yamadzulo zoopsa zidzayamba kuchitika,

ndipo zidzakhala zitatha pofika mmawa.

Izi ndizo zidzachitikire anthu otilanda zinthu,

gawo la amene amatibera zinthu zathu.

New International Reader’s Version

Isaiah 17:1-14

Prophecies Against Damascus and Israel

1Here is a prophecy against Damascus that the Lord gave me. He said,

“Damascus will not be a city anymore.

Instead, all its buildings will be knocked down.

2The cities of Aroer will be deserted.

They will be left to the flocks that lie down there.

No one will make them afraid.

3Ephraim’s people will no longer have cities with high walls around them.

Royal power will disappear from Damascus.

Those who are left alive in Aram

will be like the glory of the people of Israel,”

announces the Lord who rules over all.

4“In days to come, the glory of Jacob’s people will fade.

Their strength will get weaker and weaker.

5It will be as when workers cut and gather grain

in the Valley of Rephaim.

They gather up stalks in their arms.

Only a few heads of grain are left.

6In the same way, only a few people will be left alive.

It will be as when workers knock olives off the trees.

Only two or three olives are left on the highest branches.

Four or five at most are left on the limbs that produce fruit,”

announces the Lord, the God of Israel.

7In days to come, people will look to their Maker for help.

They will turn their eyes to the Holy One of Israel.

8They won’t trust in the altars

they made with their own hands.

They won’t pay any attention to the poles they used

to worship the female god named Asherah.

And they won’t depend on the incense altars

they made with their own fingers.

9At that time the strong cities in Israel will be deserted. They will be as they were when the Israelites drove the Canaanites away. They will be like places that are taken over by bushes and weeds. The whole land will become dry and empty.

10Israel, you have forgotten God, who saves you.

You have not remembered the Rock, who keeps you safe.

You might set out the finest plants.

You might plant vines from other lands.

11The plants might start to grow on the day you set them out.

The vines might begin to bud on the morning you plant them.

But even if they do, there won’t be any harvest.

Instead, there will be sickness and pain that won’t go away.

12How terrible it will be for the nations that attack us!

The noise of their armies is like the sound of the ocean.

How terrible it will be for the nations who fight against us!

They are as loud as huge waves crashing on the shore.

13They sound like the roar of rushing waters.

But when the Lord speaks out against them, they run far away.

The wind blows them away like straw on the hills.

A strong wind drives them along like tumbleweeds.

14In the evening, the nations terrify us.

But before morning comes, they are gone.

That’s what happens to those who steal our goods.

That’s what happens to those who take what belongs to us.