Yesaya 12 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 12:1-6

Nyimbo za Mayamiko

1Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:

“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;

chifukwa ngakhale munandipsera mtima,

mkwiyo wanu wachoka,

ndipo mwanditonthoza.

2Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;

ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.

Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;

Iye wakhala chipulumutso changa.”

3Mudzakondwera popeza Yehova

ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.

4Tsiku limenelo mudzati:

“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;

mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,

ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.

5Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;

zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.

6Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;

pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”

Nova Versão Internacional

Isaías 12:1-6

Ação de Graças

1Naquele dia, você dirá:

“Eu te louvarei, Senhor!

Pois estavas irado contra mim,

mas a tua ira desviou-se,

e tu me consolaste.

2Deus é a minha salvação;

terei confiança e não temerei.

O Senhor, sim, o Senhor

é a minha força e o meu cântico;

ele é a minha salvação!”

3Com alegria vocês tirarão água

das fontes da salvação.

4Naquele dia, vocês dirão:

“Louvem o Senhor, invoquem o seu nome;

anunciem entre as nações os seus feitos,

e façam-nas saber que o seu nome é exaltado.

5Cantem louvores ao Senhor, pois ele tem feito coisas gloriosas,

sejam elas conhecidas em todo o mundo.

6Gritem bem alto e cantem de alegria, habitantes de Sião,

pois grande é o Santo de Israel no meio de vocês”.