Yesaya 12 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 12:1-6

Nyimbo za Mayamiko

1Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:

“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;

chifukwa ngakhale munandipsera mtima,

mkwiyo wanu wachoka,

ndipo mwanditonthoza.

2Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;

ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.

Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;

Iye wakhala chipulumutso changa.”

3Mudzakondwera popeza Yehova

ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.

4Tsiku limenelo mudzati:

“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;

mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,

ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.

5Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;

zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.

6Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;

pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”

Ketab El Hayat

إشعياء 12:1-6

تسبيحة شكر

1وَتَقُولُ فِي ذَلِكَ الْيَوْمِ: «أَحْمَدُكَ يَا رَبُّ، لأَنَّكَ وَإِنْ غَضِبْتَ عَلَيَّ، فَإِنَّ غَضَبَكَ يَرْتَدُّ عَنِّي وَتُعَزِّينِي. 2هَا إِنَّ اللهَ خَلاصِي فَأَطْمَئِنُّ وَلا أَرْتَعِدُ، لأَنَّ الرَّبَّ اللهَ هُوَ قُوَّتِي وَتَرْنِيمَتِي وَقَدْ أَصْبَحَ لِي خَلاصاً». 3فَتَسْتَقُونَ بِبَهْجَةٍ مِنْ يَنَابِيعِ الْخَلاصِ. 4وَتَقُولُونَ فِي ذَلِكَ الْيَوْمِ: «احْمَدُوا الرَّبَّ، نَادُوا بِاسْمِهِ، عَرِّفُوا بِأَفْعَالِهِ بَيْنَ الشُّعُوبِ، وَأَعْلِنُوا أَنَّ اسْمَهُ قَدْ تَعَالَى. 5اشْدُوا لِلرَّبِّ لأَنَّهُ قَدْ صَنَعَ عَظَائِمَ. لِيُعْلَنْ ذَلِكَ فِي الأَرْضِ كُلِّهَا 6اهْتُفُوا وَتَغَنُّوا يَا أَهْلَ صِهْيَوْنَ، لأَنَّ قُدُّوسَ إِسْرَائِيلَ عَظِيمٌ بَيْنَكُمْ».