Yesaya 11 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 11:1-16

Za Ufumu Wamtendere wa Mesiya

1Padzatuluka mphukira pa tsinde la Yese

ndipo nthambi idzaphukira kuchokera ku mizu yake.

2Mzimu wa Yehova udzakhala pa iye

Mzimu wanzeru ndi wa kumvetsa zinthu,

Mzimu wauphungu ndi wamphamvu,

Mzimu wachidziwitso ndi wakuopa Yehova.

3Ndipo kuopa Yehova ndiye chidzakhale chinthu chomukondweretsa.

Iye sadzaweruza potsata zooneka pamaso,

kapena kugamula mlandu potsata zakumva;

4koma amphawi adzawaweruza mwachilungamo,

adzaweruza mwachilungamo mlandu wa anthu osauka a dziko lapansi.

Iye adzakantha dziko lapansi ndi mawu ake;

atalamula Iyeyu anthu oyipa adzaphedwa.

5Chilungamo chidzakhala ngati lamba wake

ndipo kukhulupirika kudzakhala ngati chomangira mʼchiwuno mwake.

6Mʼmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa,

kambuku adzagona pansi pamodzi ndi mwana wambuzi,

mwana wangʼombe ndi mwana wa mkango adzadyera limodzi

ndipo mwana wamngʼono adzaziweta.

7Ngʼombe yayikazi ndi chimbalangondo zidzadya pamodzi,

ana awo adzagona pamodzi,

ndipo mkango udzadya udzu ngati ngʼombe.

8Mwana wakhanda adzasewera pa dzenje la mamba,

ndipo mwana wamngʼono adzapisa dzanja lake ku phanga la mphiri osalumidwa.

9Sipadzakhala chilichonse chopweteka kapena chowononga

pa phiri lopatulika la Yehova,

pakuti anthu a dziko lapansi adzadzaza ndi nzeru yotha kudziwa Yehova

monga momwe nyanja imadzazira ndi madzi.

10Tsiku limenelo mfumu yatsopano yochokera pa Muzu wa Yese idzakhala ngati chizindikiro kwa anthu a mitundu yonse. Mitundu ya anthu idzasonkhana kwa Iye, ndipo malo awo okhalapo adzakhala aulemerero. 11Tsiku limenelo Ambuye adzatambasula dzanja lake kachiwiri kuti awombole anthu ake otsalira ku Asiriya, ku Igupto, ku Patirosi, Kusi, ku Elamu, ku Sinana, ku Hamati ndi pa zilumba za nyanja yamchere.

12Adzakwezera mitundu ya anthu mbendera,

ndipo adzasonkhanitsa otayika a ku Israeli;

Iye adzasonkhanitsa anthu obalalika a ku Yuda

kuchokera ku mbali zonse zinayi za dziko lapansi.

13Nsanje ya Efereimu idzatha,

ndipo adani a Yuda adzatha;

Efereimu sadzachitira nsanje Yuda,

ngakhale Yuda sadzamuda Efereimu.

14Yuda ndi Efereimu adzathira nkhondo pa Afilisti mbali ya kumadzulo;

ndipo onsewo pamodzi adzalanda zinthu za anthu a kummawa.

Adzalimbana ndi Edomu ndi Mowabu,

ndipo Aamoni adzawagonjera.

15Yehova adzaphwetsa

mwendo wa nyanja ya Igupto;

adzatambasula dzanja lake ndipo adzawombetsa mphepo yotentha

pa mtsinje wa Yufurate.

Iye adzawugawa mtsinjewo kukhala timitsinje tisanu ndi tiwiri

kuti anthu athe kuwoloka powuma atavala nsapato.

16Padzakhala msewu waukulu woti ayendepo anthu ake otsalira

amene anatsalira ku Asiriya,

monga mmene panali msewu waukulu woyendapo Israeli

pamene amachokera ku Igupto.

Luganda Contemporary Bible

Isaaya 11:1-16

Ettabi Eririva ku Yese

111:1 a nny 10; Is 9:7; Kub 5:5 b Is 4:2Ensibuka erimera ng’eva ku kikonge kya Yese,

ne ku mirandira kulivaako omuti, ne ku muti kulivaako Ettabi eriribala ekibala.

211:2 a Is 42:1; 48:16; 61:1; Mat 3:16; Yk 1:32-33 b Bef 1:17 c 2Ti 1:7Mwoyo wa Mukama alibeera ku ye,

Mwoyo ow’amagezi n’okutegeera

ne Mwoyo w’okusala ensonga, n’ow’amaanyi

ne Mwoyo w’okumanya era n’okutya Mukama Katonda.

311:3 a Yk 7:24 b Yk 2:25Era n’essanyu lye liribeera mu kutya Mukama Katonda.

Taasalenga misango ng’asinziira ku maaso ge gokka nga bwe galaba,

oba okusalawo ng’asinziira ku byawulira n’amatu ge byokka,

411:4 a Zab 72:2 b Is 9:7 c Is 3:14 d Mal 4:6 e Yob 4:9; 2Bs 2:8naye anaasaliranga abaavu emisango mu bwenkanya,

era asalire mu bwenkanya abo abawombeefu ab’omu nsi;

era alikuba ensi n’omuggo ogw’omu kamwa ke,

era alitta omukozi w’ebibi n’omukka ogw’omu kamwa ke.

511:5 a Is 25:1 b Bef 6:14Obutuukirivu, bwe buliba olukoba lwe yeesibya,

n’obwesigwa, bw’alyesiba mu kiwato kye.

611:6 Is 65:25Omusege gulisulanga wamu n’omwana gw’endiga,

n’engo egalamire wamu n’omwana gw’embuzi;

era ennyana n’empologoma n’ennyana eya ssava binaagalamiranga wamu;

era omwana omuto yalizirabirira.

7Ente n’eddubu biririira wamu,

abaana baazo banaagalamiranga wamu.

Empologoma erirya omuddo ng’ente.

8N’omwana ayonka alizannyira ku kinnya ky’enswera,

n’omwana omuto aliteeka omukono gwe mu kinnya ky’essalambwa.

911:9 a Yob 5:23 b Zab 98:2-3; Is 52:10 c Is 45:6, 14; Kbk 2:14Tewalibeera kukolaganako bulabe

wadde okuttiŋŋana ku lusozi lwange olutukuvu.

Kubanga ensi eribeera ejjudde okumanya Mukama Katonda,

ng’amazzi bwe gajjuza ennyanja.

1011:10 a Yk 12:32 b Is 49:23; Luk 2:32 c Bar 15:12* d Is 14:3; 28:12; 32:17-18Awo ku lunaku luli, muzzukulu wa Yese aliyimirira ng’ebendera eri amawanga. Oyo amawanga gwe ganaanoonyanga, n’ekifo kye eky’okuwummuliramu, kiribeera kya kitiibwa. 1111:11 a Is 10:20 b Is 19:24; Kos 11:11; Mi 7:12; Zek 10:10 c Lub 10:22 d Is 42:4, 10, 12; 66:19Era ku lunaku olwo Mukama aligolola omukono gwe omulundi ogwokubiri11:11 Abayisirayiri bwe baali bava e Misiri ogwo gwe mulundi ogwasooka. okununula abasigalawo ku bantu be, okubaggya mu Bwasuli ne mu Misiri ne mu Pasuloosi ne mu Kuusi ne mu Eramu ne mu Sinaali ne mu Kamasi ne mu bizinga eby’omu nnyanja.

1211:12 Zef 3:10Era aliwanikira amawanga bbendera, akuŋŋaanye abawaŋŋanguse ba Isirayiri;

aleete wamu abantu ba Yuda abaali basaasaanye mu nsonda ennya ez’ensi.

1311:13 Yer 3:18; Ez 37:16-17, 22; Kos 1:11Olwo obuggya bwa Efulayimu bulyoke buggweewo,

n’abo abateganya Yuda balizikirizibwa.

Efulayimu talikwatirwa Yuda buggya

wadde Yuda okubeera omulabe wa Efulayimu.

1411:14 a Dan 11:41; Yo 3:19 b Is 16:14; 25:10Bombi awamu balirumba ne bamalawo Abafirisuuti mu busozi bw’ebugwanjuba;

era bombiriri balinyaga abantu b’omu buvanjuba.

Baligolola omukono gwabwe ku Edomu ne Mowaabu;

n’abaana ba Amoni balibagondera.

1511:15 a Is 19:16 b Is 7:20Era Mukama Katonda alikaliza

omukutu gw’ennyanja y’Abamisiri;

era aliwujira omukono gwe ku mugga Fulaati

ne guleetawo omuyaga ogukaza,

agwawulemu ebitundu musanvu

abantu bye banaasomokanga ku bigere.

1611:16 a Is 19:23; 62:10 b Kuv 14:26-31Era abo abalisigalawo ku bantu be balibeera n’ekkubo ery’okuyitamu ery’eggwanga

eryasigala ku Bwasuli

nga bwe kyali eri Isirayiri ku lunaku

lwe baaviirako mu Misiri.