Yesaya 1 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 1:1-31

1Masomphenya wonena za Yuda ndi Yerusalemu, amene Yesaya mwana wa Amozi, anaona pa nthawi ya ulamuliro wa Uziya, Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a Yuda.

Anthu Owukira

2Tamverani, miyamba inu! Tchera khutu, iwe dziko lapansi!

Pakuti Yehova wanena kuti,

“Ndinabala ana ndi kuwalera,

koma anawo andiwukira Ine.

3Ngʼombe imadziwa mwini wake,

bulu amadziwa kumene kuli gome la mbuye wake,

koma Israeli sadziwa,

anthu anga samvetsa konse.”

4Haa, mtundu wochimwa,

anthu olemedwa ndi machimo,

obadwa kwa anthu ochita zoyipa,

ana odzipereka ku zoyipa!

Iwo asiya Yehova;

anyoza Woyerayo wa Israeli

ndipo afulatira Iyeyo.

5Chifukwa chiyani mukufuna kuti muzingolangidwabe?

Chifukwa chiyani mukupitirira kukhala mʼmoyo wowukira?

Mutu wanu wonse uli ndi mabala,

mtima wanu wonse wafowokeratu.

6Kuchokera ku phazi mpaka ku mutu

palibe pabwino,

paliponse pali mikwingwirima ndi zilonda,

mabala ali magazi chuchuchu,

mabala ake ngosatsuka, ngosamanga

ndiponso ngosapaka mafuta ofewetsa.

7Dziko lanu lasanduka bwinja,

mizinda yanu yatenthedwa ndi moto;

minda yanu ikukololedwa ndi alendo

inu muli pomwepo,

dziko lanu lasanduka bwinja monga ngati lagonjetsedwa ndi alendo.

8Mwana wamkazi wa Ziyoni watsala yekha

ngati nsanja mʼmunda wampesa,

ngati chisimba mʼmunda wa minkhaka,

ngati mzinda wozingidwa ndi nkhondo.

9Yehova Wamphamvuzonse akanapanda

kutisiyira opulumuka,

tikanawonongeka ngati Sodomu,

tikanakhala ngati anthu a ku Gomora.

10Imvani mawu a Yehova,

inu olamulira Sodomu;

mverani lamulo la Mulungu wathu,

inu anthu a ku Gomora!

11Yehova akuti, “Kodi ndili nazo chiyani

nsembe zanu zochuluka?”

“Zandikola nsembe zanu zopsereza

za nkhosa zazimuna ndiponso mafuta a nyama zonenepa;

sindikusangalatsidwanso

ndi magazi angʼombe zamphongo ndi a ana ankhosa ndi ambuzi zazimuna.

12Ndani anakulamulirani kuti

mubwere nazo pamaso panga?

Ndani anakuwuzani kuti muzipondaponda mʼmabwalo a nyumba yanga?

13Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo!

Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine.

Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa,

kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata.

14Zikondwerero zanu za Mwezi Watsopano ndi masiku anu opatulika

ndimadana nazo.

Zasanduka katundu wondilemera;

ndatopa kuzinyamula.

15Mukamatambasula manja anu popemphera,

Ine sindidzakuyangʼanani;

ngakhale muchulukitse mapemphero anu,

sindidzakumverani.

Manja anu ndi odzaza ndi magazi;

16sambani, dziyeretseni.

Chotsani pamaso panu

ntchito zanu zoyipa!

Lekani kuchita zoyipa,

17phunzirani kuchita zabwino!

Funafunani chilungamo,

thandizani oponderezedwa.

Tetezani ana amasiye,

muwayimirire akazi amasiye pa milandu yawo.”

18Yehova akuti,

“Tiyeni tsono tikambe mlandu wanu.

Ngakhale machimo anu ali ofiira,

adzayera ngati thonje.

Ngakhale ali ofiira ngati kapezi,

adzayera ngati ubweya wankhosa.

19Ngati muli okonzeka kundimvera

mudzadya zinthu zabwino za mʼdziko;

20koma mukakana ndi kuwukira

mudzaphedwa ndi lupanga.”

Pakuti Yehova wayankhula.

21Taonani momwe mzinda wokhulupirika

wasandukira wadama!

Mzinda umene kale unali wodzaza ndi chiweruzo cholungama;

mu mzindamo munali chilungamo,

koma tsopano muli anthu opha anzawo!

22Siliva wako wasanduka wachabechabe,

vinyo wako wabwino wasungunulidwa ndi madzi.

23Atsogoleri ako ndi owukira,

anthu ogwirizana ndi mbala;

onse amakonda ziphuphu

ndipo amathamangira mphatso.

Iwo sateteza ana amasiye;

ndipo samvera madandawulo a akazi amasiye.

24Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova Wamphamvu,

Wamphamvuyo wa Israeli, akunena kuti,

“Haa, odana nane ndidzawatha,

ndipo ndidzawabwezera ndekha adani anga.

25Ndidzatambasula dzanja langa kuti ndilimbane nawe;

ndidzasungunula machimo ako nʼkuwachotsa,

monga mmene amachotsera dzimbiri ndi mankhwala.

26Ndidzabwezeretsa oweruza ako ngati masiku amakedzana,

aphungu ako ndidzawabwezeretsa ngati poyamba paja.

Kenaka iweyo udzatchedwa

mzinda wolungama,

mzinda wokhulupirika.”

27Ziyoni adzawomboledwa mwa chiweruzo cholungama,

anthu ake olapadi adzapulumutsidwa mwachilungamo.

28Koma owukira ndi ochimwa adzawawonongera pamodzi,

ndipo amene asiya Yehova adzatheratu.

29“Mudzachita nayo manyazi mitengo ya thundu

imene inkakusangalatsani;

mudzagwetsa nkhope chifukwa cha minda

imene munayipatula.

30Mudzakhala ngati mtengo wa thundu umene masamba ake akufota,

mudzakhala ngati munda wopanda madzi.

31Munthu wamphamvu adzasanduka ngati udzu wowuma,

ndipo ntchito zake zidzakhala ngati mbaliwali;

motero zonse zidzayakira limodzi,

popanda woti azimitse motowo.”

New Serbian Translation

Књига пророка Исаије 1:1-31

1Виђење Исаије сина Амоцова, што је за Јуду и Јерусалим видео у време Јудиних царева: Озије, Јотама, Ахаза и Језекије.

Неразумни и грешни народ

2Чујте, небеса! Слушај, земљо,

јер говори Господ:

„Синове сам васпитао и подигао,

а они се одметнуше од мене.

3Во познаје власника својега

и магарац јасле господара својега.

Израиљ не зна;

народ мој не разуме!“

4Јао, грешнога ли пука,

народа огрезлог у кривици,

потомака злочиначких,

синова покварењачких!

Господа су оставили;

Светитеља Израиљевог презрели,

леђа му окренули.

5Где још да ударим,

одметници тврдокорни?

Сва је глава болна

и све срце изнемогло;

6од пете до главе здравог места нема,

него су убоји и модрице и ране отворене;

очишћене нису,

у завојима нису,

уљем заблажене нису.

7Опустошена вам је земља,

огањ вам је градове попалио,

ваше њиве пред вама харају туђинци.

Пустош је као кад опустоше туђинци.

8Остављена је ћерка сионска

као сеница у винограду,

као колиба у градини за краставце,

као град под опсадом.

9Да нам Господ над војскама

није оставио остатка,

као Содома били бисмо,

слични Гомори били бисмо.

10Реч Господњу чујте,

главари содомски!

Закон Бога нашег послушајте,

народе гоморски!

11„Шта ли ће мени мноштво жртава ваших?

– говори Господ.

Сит сам овнујских свеспалница

и наслага лојних са телади гојних.

И крв од бикова и јагањаца и јараца

не мили се мени.

12Кад долазите да ми се покажете,

ко то тражи од вас

да по мојим предворјима трупкате?

13Не умножавајте безвредне приносе,

кађење на које се гадим;

младине и суботе, сазивање сазива,

не подносим зле1,13 Или: идолске, грешне. свечаности.

14Младине ваше и празници ваши,

то мрзи душа моја,

то је терет за ме,

додија ми подносити.

15Кад за молитву ширите руке своје,

ја од вас одвраћам очи своје;

и кад продужујете молитву,

ја вас не слушам.

Ваше су руке огрезле у крви.

16Оперите себе, очистите себе.

Уклоните злоћу дела ваших испред очију мојих.

Престаните зло чинити,

17учите се добро чинити: тежите праву,

ублажите угњетавање,

дајте права сиротињи,

парничите се у корист удовице.

18Затим дођите да расправљамо

– говори Господ –

буду ли греси ваши као скерлет,

постаће бели као снег;

буду ли црвени као пурпур,

постаће као вуна.

19Ако будете вољни и послушате,

добра земаљска јешћете.

20А ако одбаците и буните се,

мач ће вас прогутати

– јер уста Господња рекоше.“

Тужбалица над Јерусалимом

21Како се претвори у блудницу

верна насеобина!

Била је пуна правичности,

у њој је боравила правда,

а сада су убице.

22Твоје је сребро као згура постало.

Твоје пиће се разводнило.

23Твоји главари су се одметнули,

с крадљивцима другови су постали.

Сваки се граби за мито

и хрли за поклонима.

Право сиротињи они ускраћују;

удовичина парница до њих не досеже.

24Зато говори Господар,

Господ над војскама, Силни Израиљев:

„Ах, кад се искалим на противницима

и кад се осветим непријатељима!

25Кад руку на тебе испружим,

да лужином згуру твоју очистим,

да из тебе онечишћења уклоним.

26Па ти судије опет поставим као некад,

саветнике као од давнина,

те да те прозову

’Град праведности’,

’Верна насеобина.’“

27Правда ће откупити Сион,

и праведност покајнике његове;

28а преступници и грешници заједно ће се скршити

и они који напуштају Господа погинуће.

Против обожавања светог дрвета

29„Због племенитог дрвећа ће се стидети,

зато што их славите;

и због лугова ћете се црвенети,

зато што сте их изабрали.

30Ви ћете бити слични храсту,

с лишћем што се на њему суши.

Налик лугу у ком воде нема.

31И скривено благо ће бити као кучина,

и онај ко га начини као варница –

обоје ће заједно изгорети,

а нико неће гасити.“