Yeremiya 52 – CCL & NUB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 52:1-34

Kuwonongeka kwa Yerusalemu

1Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina. 2Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu. 3Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake.

Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.

4Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo. 5Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.

6Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya. 7Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba, 8koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.

9Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake. 10Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda. 11Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.

12Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu. 13Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse. 14Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu. 15Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni. 16Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.

17Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni. 18Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova. 19Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.

20Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka. 21Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi. 22Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija. 23Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.

24Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata. 25Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo. 26Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula. 27Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe.

Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo. 28Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi:

Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;

29mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara,

anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;

30mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara,

Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo.

Onse pamodzi analipo anthu 4,600.

Kumasulidwa kwa Yehoyakini

31Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo. 32Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni. 33Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse. 34Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.

Swedish Contemporary Bible

Jeremia 52:1-34

Sidkia regerar i Jerusalem

(2 Kung 24:18-20; 2 Krön 36:11-14)

1Sidkia var tjugoett år gammal när han blev kung, och han regerade i elva år i Jerusalem. Hans mor hette Hamutal och var dotter till Jeremia från Livna. 2Han gjorde det som var ont i Herrens ögon, precis som Jojakim hade gjort. 3Herren förkastade till sist i sin vrede både Jerusalem och Juda.

Jerusalems fall, förstörelse och folkets bortförande

(2 Kung 24:20—25:21; 2 Krön 36:15-20; Jer 39:1-10)

Men Sidkia gjorde uppror mot kungen i Babylonien. 4I Sidkias nionde regeringsår, på den tionde dagen i tionde månaden, kom Nebukadnessar, kungen av Babylonien, tågande med hela sin armé mot Jerusalem och belägrade det. De byggde en belägringsvall omkring staden. 5Belägringen varade ända till kung Sidkias elfte regeringsår. 6På nionde dagen i fjärde månaden var hungersnöden i staden så svår att folket inte längre hade någon mat i landet. 7Då stormades staden, och alla trupper flydde på natten genom en port som fanns mellan de båda murarna i närheten av den kungliga trädgården, medan de kaldeiska trupperna omringade staden. De flydde mot Jordandalen.

8Men den kaldeiska armén förföljde kungen och tog honom till fånga på Jerikoslätten. Alla hans män lämnade honom och skingrades. 9Kaldéerna grep honom och förde honom till den babyloniske kungen i Rivla i Hamat, där denne dömde honom. 10Den babyloniske kungen lät avrätta Sidkias söner inför hans ögon, och likaså lät han i Rivla avrätta alla de förnämsta männen i Juda. 11Sedan lät han sticka ut ögonen på Sidkia. Den babyloniske kungen band honom med kopparkedjor och förde honom till Babylon och satte honom i fängelse, och där fick han sitta ända tills han dog.

12På tionde dagen i femte månaden av den babyloniske kungen Nebukadnessars nittonde regeringsår kom Nebusaradan, befälhavaren för livgardet och en av den babyloniske kungens närmaste män, till Jerusalem. 13Han brände ner Herrens hus, kungapalatset, och även alla andra byggnader av värde i Jerusalem. 14De kaldeiska trupperna som han var befälhavare för rev ner alla Jerusalems murar. 15Nebusaradan, befälhavaren för livgardet, förde bort till exilen några av de fattigaste som var kvar i staden, tillsammans med de desertörer som hade gått över till den babyloniske kungen och de hantverkare som var kvar, 16men några av de fattigaste i landet lämnade befälhavaren Nebusaradan kvar för att sköta om vingårdar och åkrar.

17Kaldéerna högg ner kopparpelarna i Herrens hus, ställningen och kopparhavet som fanns där och tog med sig all koppar till Babylonien. 18De tog också kärlen, skovlarna, knivarna, skålarna, fyrfaten och alla kopparföremål som användes i gudstjänsten. 19Befälhavaren för livgardet tog också faten, fyrfaten, offerskålarna, grytorna, lampställen, skålarna och bägarna, allt som var av rent guld och rent silver.

20Pelarna, kopparhavet, de tolv koppartjurarna under det och ställningarna, som Salomo låtit göra till Herrens hus, bestod sammantaget av så mycket koppar att det inte gick att väga. 21Pelarna var 9 meter höga, 6 meter i omkrets och ihåliga med väggar tjocka som fyra fingrars bredd.52:21 Uppgifterna om pelarna, liksom en del andra detaljer i templet, varierar något, jfr 1 Kung 7 och 2 Krön 3-5 (spec. 3:15). Tjockleken på pelarna/pelarväggarna kan tolkas olika, men det troligaste är att pelarväggarna (även om ordet inte finns i grundtexten här) var fyra fingerbredder, dvs. ca 10 cm. 22På var och en av dem fanns ett pelarhuvud av koppar, som var 2,5 meter högt och hade ornament i form av granatäpplen som dekoration runt pelarhuvudet. Allt var gjort av koppar. 23Det fanns nittiosex granatäpplen på utsidan och sammanlagt etthundra granatäpplen i ett flätverk runtom.

24Befälhavaren för livgardet tog till fånga översteprästen Seraja och prästen närmast honom, Sefanja, samt tre av dörrvakterna. 25Från staden tog han en hovman som var befälhavare i armén, sju av kungens närmaste män i staden, och sekreteraren åt den överbefälhavare som skrev ut folket till krigstjänst, samt ytterligare sextio män i staden. 26Nebusaradan, befälhavaren för livgardet, tog dem och förde dem till den babyloniske kungen i Rivla. 27Den babyloniske kungen lät avrätta dem i Rivla i Hamat. Så fördes Juda bort från sitt land.

28Detta är de som Nebukadnessar förde bort:

under det sjunde året 3 023 judar,

29under Nebukadnessars artonde regeringsår 832 personer från Jerusalem,

30och under Nebukadnessars tjugotredje regeringsår 745 personer,

som Nebusaradan, befälhavaren för livgardet, förde bort,

sammanlagt 4 600 personer.

Jojakins benådning

(2 Kung 25:27-30)

31Under det trettiosjunde året som Judas kung Jojakin var i fångenskap, den tjugofemte dagen i tolfte månaden, samma år som Evil Merodak blev kung i Babylonien, benådade denne Jojakin, Juda kung, och släppte ut honom ur fängelset. 32Han talade vänligt till honom och gav honom den främsta platsen bland de kungar som var hos honom i Babylon. 33Jojakin fick lägga av sig fångdräkten och alltid äta vid kungens bord under resten av sitt liv. 34Så länge han levde gav den babyloniske kungen honom också ett dagligt underhåll.