Yeremiya 52 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 52:1-34

Kuwonongeka kwa Yerusalemu

1Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina. 2Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu. 3Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake.

Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.

4Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo. 5Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.

6Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya. 7Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba, 8koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.

9Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake. 10Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda. 11Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.

12Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu. 13Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse. 14Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu. 15Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni. 16Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.

17Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni. 18Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova. 19Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.

20Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka. 21Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi. 22Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija. 23Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.

24Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata. 25Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo. 26Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula. 27Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe.

Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo. 28Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi:

Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;

29mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara,

anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;

30mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara,

Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo.

Onse pamodzi analipo anthu 4,600.

Kumasulidwa kwa Yehoyakini

31Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo. 32Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni. 33Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse. 34Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.

La Bible du Semeur

Jérémie 52:1-34

Appendice historique

La prise de Jérusalem

1Sédécias avait vingt et un ans à son avènement. Il régna onze ans à Jérusalem. Sa mère s’appelait Hamoutal, elle était fille de Jérémie, de Libna52.1 Ce chapitre reproduit presque intégralement 2 R 24.18-20 ; 25.1-21, 25-30. Pour les notes, voir ces chapitres de 2 Rois.. 2Il fit ce que l’Eternel considère comme mal, tout comme Yehoyaqim. 3Tout cela arriva parce que l’Eternel était en colère contre Jérusalem et Juda, au point de les chasser loin de lui.

Or, Sédécias se révolta contre le roi de Babylone. 4La neuvième année de son règne, le dixième jour du dixième mois, Nabuchodonosor, roi de Babylone, vint avec toute son armée attaquer Jérusalem. Ils établirent leur camp devant la ville et construisirent des terrassements tout autour.

5La ville resta assiégée jusqu’à la onzième année du règne de Sédécias.

6Le neuvième jour du quatrième mois, alors que la famine sévissait durement dans la ville et que la population du pays n’avait plus rien à manger, 7une brèche fut ouverte dans le rempart de la ville et tous les soldats52.7 Le texte parallèle de Jr 39.4 mentionne le roi Sédécias avec les soldats. Il figurera aussi dans le présent texte au verset 8. Il est donc possible que l’omission du roi au v. 7 soit due à une erreur de copiste. de Juda s’enfuirent : ils s’échappèrent de la ville, de nuit, par la porte qui se trouvait entre les deux remparts et qui donnait sur le jardin du roi, tandis que la ville était encerclée par les Chaldéens, et ils prirent le chemin de la vallée du Jourdain. 8Mais l’armée des Chaldéens se lança à la poursuite du roi, et rattrapa Sédécias dans la plaine de Jéricho. Alors tous ses soldats se dispersèrent loin de lui. 9Les Chaldéens se saisirent du roi et l’amenèrent au roi de Babylone à Ribla, dans le pays de Hamath, et celui-ci prononça son jugement contre lui. 10Le roi de Babylone fit égorger les fils de Sédécias sous ses yeux. Il fit aussi égorger à Ribla tous les ministres de Juda. 11Puis il fit crever les yeux à Sédécias et le fit lier avec une double chaîne de bronze. Après cela, le roi de Babylone le déporta à Babylone où il l’enferma en prison. Sédécias y resta jusqu’à sa mort.

12Le dixième jour du cinquième mois – c’était la dix-neuvième année du règne de Nabuchodonosor, roi de Babylone – Nebouzaradân, chef de la garde impériale qui était attaché au service personnel du roi de Babylone, fit son entrée à Jérusalem. 13Il mit le feu au temple de l’Eternel, au palais royal, à toutes les maisons et à tous les édifices importants de la ville. 14Les troupes chaldéennes, sous le commandement du chef de la garde, démantelèrent les remparts qui entouraient la ville.

15Nebouzaradân, chef de la garde impériale, déporta une partie des gens les plus pauvres et le reste de la population qui était demeurée dans la ville, ceux qui s’étaient déjà rendus au roi de Babylone et ce qui restait des artisans. 16Mais il laissa une partie des gens pauvres du pays pour cultiver les vignes et les champs.

17Les Chaldéens mirent en pièces les colonnes de bronze du temple de l’Eternel, les chariots et la grande cuve de bronze qui étaient dans le parvis du Temple, et ils emportèrent tout le bronze à Babylone. 18Ils prirent aussi les chaudrons, les pelles, les couteaux, les coupes à aspersion, les autres coupes et tous les autres objets de bronze employés pour le culte. 19Le chef de la garde s’empara de tous les objets d’or et d’argent massif : les bassins, les brasiers, les coupes à aspersion, les chaudrons, les chandeliers, les autres coupes et les bols.

20On ne saurait évaluer le poids du bronze des deux colonnes, de la grande cuve et des douze bœufs de bronze qui soutenaient les chariots, que le roi Salomon avait fait faire pour le temple de l’Eternel. 21Chaque colonne avait neuf mètres de haut, sa circonférence était de six mètres, le bronze avait près de huit centimètres d’épaisseur, la colonne étant creuse à l’intérieur. 22Elle était surmontée d’un chapiteau de bronze de deux mètres cinquante de haut, entouré d’un treillis décoré de grenades. Le tout était en bronze. 23Il y avait quatre-vingt-seize grenades en relief, et en tout, cent grenades autour du treillis.

24Le chef de la garde fit prisonnier le grand-prêtre Seraya, Sophonie, le prêtre en second, et les trois prêtres chargés de surveiller l’entrée du Temple. 25Il arrêta aussi, dans la ville, un haut responsable militaire, sept conseillers du roi, qui étaient restés dans la ville, le secrétaire du chef de l’armée chargé de recruter les soldats dans le pays, ainsi que soixante Judéens qui se trouvaient à l’intérieur de la ville. 26Nebouzaradân, chef de la garde, emmena tous ces prisonniers au roi de Babylone, à Ribla. 27Celui-ci les fit exécuter à Ribla, dans le pays de Hamath. Ainsi, la population de Juda fut déportée loin de sa patrie.

28Voici le nombre des captifs que Nabuchodonosor emmena en exil : 3 023 Judéens, la septième année de son règne52.28 En 597 av. J.-C. : 29832 habitants de Jérusalem la dix-huitième année52.29 En 587 av. J.-C.. 30Puis, la vingt-troisième année du règne de Nabuchodonosor52.30 En 582 av. J.-C., Nebouzaradân, le chef de la garde, déporta encore 745 Judéens ; ce qui donne un total de 4 600 déportés.

Un signe d’espoir : Yehoyakîn gracié

31La trente-septième année52.31 En 561 av. J.-C. de la déportation de Yehoyakîn52.31 Voir 2 R 24.10-17 ; Jr 22.24-27., roi de Juda, le vingt-cinquième jour du douzième mois, Evil-Merodak, roi de Babylone, gracia Yehoyakîn, roi de Juda, l’année de son accession au trône de Babylone, et le fit sortir de prison.

32Il le traita avec bonté et lui accorda une situation supérieure à celle des autres rois exilés avec lui à Babylone. 33Il lui fit quitter ses vêtements de prisonnier et l’admit à prendre ses repas à sa table jusqu’à la fin de sa vie. 34Le roi de Babylone pourvut à son entretien régulier, jour après jour, aussi longtemps qu’il vécut.