Yeremiya 49 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 49:1-39

Uthenga Wonena za Aamoni

1Yehova ananena izi:

Amoni,

“Kodi Israeli alibe ana aamuna?

Kapena alibe mlowamʼmalo?

Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi?

Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?

2Koma nthawi ikubwera,”

akutero Yehova,

“pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo

ku Raba, likulu la Amoni;

ndipo malo awo opembedzera milungu yawo

adzatenthedwa ndi moto.

Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo

kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,”

akutero Yehova.

3“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika!

Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba!

Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu;

thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga,

chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo,

pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.

4Chifukwa chiyani mukunyadira

chigwa chanu,

inu anthu osakhulupirika

amene munadalira chuma chanu nʼkumati:

‘Ndani angandithire nkhondo?’

5Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe

zochokera kwa onse amene akuzungulira,”

akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse.

“Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake.

Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.

6“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,”

akutero Yehova.

Uthenga Wonena za Edomu

7Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu:

“Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani?

Kodi anzeru analeka kupereka uphungu?

Kodi nzeru zawo zinatheratu?

8Inu anthu a ku Dedani, thawani,

bwererani ndi kukabisala ku makwalala

chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau

popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.

9Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu

akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?

Anthu akuba akanafika usiku

akanangotengako zimene akuzifuna zokha?

10Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau.

Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo,

kotero kuti sadzathanso kubisala.

Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka.

Palibe wonena kuti,

11‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza.

Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’ ”

12Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho. 13Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”

14Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova:

Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti,

“Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu!

Konzekerani nkhondo!”

15“Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina.

Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.

16Kuopseza kwako kwakunyenga;

kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,

iwe amene umakhala mʼmapanga

a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri.

Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga,

ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”

akutero Yehova.

17“Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha.

Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo

chifukwa cha kuwonongeka kwake.

18Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora,

pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,”

akutero Yehova,

“motero palibe munthu

amene adzakhala mu Edomu.

19“Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani

kupita ku malo a msipu wobiriwira,

Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo.

Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine.

Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani?

Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”

20Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova

ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani.

Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo

ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.

21Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera;

kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.

22Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka

nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.

Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu

idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.

Uthenga Wonena za Damasiko

23Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa:

“Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha

chifukwa amva nkhani yoyipa.

Mitima yawo yagwidwa ndi mantha

ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.

24Anthu a ku Damasiko alefuka.

Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa

chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu.

Ali ndi nkhawa komanso mantha

ngati za mayi pa nthawi yake yochira.

25Mzinda wotchuka

ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!

26Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa;

ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,”

akutero Yehova Wamphamvuzonse.

27“Ndidzatentha malinga a Damasiko;

moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”

Uthenga Wonena za Kedara ndi Hazori

28Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa:

“Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara.

Kawonongeni anthu a kummawako.

29Landani matenti awo ndi nkhosa zawo,

ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo.

Mutengenso ngamira zawo.

Anthu adzafuwula kwa iwo kuti,

‘Kuli zoopsa mbali zonse!’

30“Thawani mofulumira!

Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,”

akutero Yehova.

“Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu;

wakonzekera zoti alimbane nanu.

31“Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere,

umene ukukhala mosatekeseka,”

akutero Yehova,

“mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo;

anthu ake amakhala pa okha.

32Ngamira zawo zidzafunkhidwa,

ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa.

Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali.

Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,”

akutero Yehova.

33“Hazori adzasanduka bwinja,

malo okhalamo nkhandwe

mpaka muyaya.

Palibe munthu amene adzayendemo.”

Uthenga Wonena za Elamu

34Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:

35Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu,

umene uli chida chawo champhamvu.

36Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu

kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga;

ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi,

ndipo sipadzakhala dziko

limene anthu a ku Elamu sadzafikako.

37A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo

komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo.

Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga

ndipo adzakhala pa mavuto,”

akutero Yehova.

“Ndidzawapirikitsa ndi lupanga

mpaka nditawatheratu.

38Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu

ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,”

akutero Yehova.

39“Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera

anthu a ku Elamu dziko lawo,”

akutero Yehova.

Het Boek

Jeremia 49:1-39

1De Ammonieten

‘Wat bent u aan het doen? Waarom woont u in de steden van Israël? Heeft zij die steden niet van Mij geërfd? Waarom hebt u die Milkom vereert, Gad en al zijn steden in bezit genomen? 2Ik zal u hiervoor straffen,’ verklaart de Here, ‘door uw stad Rabba te verwoesten. Het zal een verlaten ruïne worden en de omliggende dorpen zullen worden platgebrand. Dan zal Israël terugkeren en haar land weer van u terugnemen. Zij zal onteigenen wie haar onteigenden,’ zegt de Here. 3‘Schreeuw het uit, Chesbon, want Ai is verwoest! Huil, inwoners van Rabba! Trek rouwkleding aan, huil en treur, ga naar buiten, want uw god Milkom zal, samen met zijn dienaren en priesters, worden verbannen. 4U bent trots op uw vruchtbare valleien, maar zij zullen spoedig worden verwoest. Ontrouwe dochter, u vertrouwde op uw rijkdom en dacht dat niemand u ooit iets zou kunnen aandoen. 5Maar kijk, Ik zal u angst aanjagen,’ zegt de Here, de God van de hemelse legers. ‘Want al uw buren zullen u uit uw land verdrijven en niemand zal uw vluchtelingen helpen. 6Maar later zal Ik de Ammonieten weer welvaart geven,’ zegt de Here.

7De Edomieten

De Here van de hemelse legers zegt: ‘Waar zijn al die wijze mannen die u vroeger had? Is er niet één overgebleven in heel Teman? 8Vlucht diep de grotten in, volk van Dedan, want de tijd is aangebroken dat Ik met u, nakomelingen van Esau, ga afrekenen! 9-10 Zij die de druiven oogsten, laten er altijd enkele achter voor de armen en zelfs dieven nemen nooit alles mee, maar Ik zal het land van Esau volledig afstropen en er zullen geen schuilplaatsen meer zijn. Al Esaus nakomelingen en verwanten zullen omkomen. Van de buren zegt niemand: 11“Ik zal uw wezen die u achterlaat, wel beschermen en ook uw weduwen kunnen op mij vertrouwen.” ’ 12De Here zegt tegen Edom: ‘Als zelfs de onschuldigen moeten lijden, waarom zou u dan ongestraft blijven? U zult net als zij deze beker leegdrinken en uw straf ondergaan! 13Want Ik heb bij mijn eigen naam gezworen,’ zegt de Here, ‘dat Bosra in een ruïne zal veranderen die iedereen zal bespotten en vervloeken. Haar steden zullen altijd puinhopen blijven.’

14Ik heb deze boodschap van de Here gehoord: Hij heeft een boodschapper gestuurd die er bij de volken op aandringt zich aaneen te sluiten om Edom te vernietigen. ‘Maak u klaar voor de strijd,’ roept hij. 15‘Ik zal u zwak maken te midden van de volken en zij zullen u allemaal haten,’ zegt de Here. 16‘U die daar in de rotskloven en op de bergen woont, bent misleid door uw roem en trots. Maar ook al woont u tussen de bergtoppen bij de adelaars, Ik zal u naar beneden halen,’ zegt de Here. 17‘Het lot van Edom zal vreselijk zijn, allen die voorbijlopen, zullen schrikken en spottend het hoofd schudden. 18Uw steden zullen net zo stil worden als Sodom en Gomorra en de steden daar in de buurt,’ zegt de Here. ‘Niemand zal er nog kunnen leven.

19Ik zal de vijand op hen af sturen als een leeuw die uit de wildernis van de Jordaan komt om de schapen te overvallen. In een oogwenk zal Ik Edom wegjagen en Ik zal iemand uitkiezen om dit te doen. Want wie is aan Mij gelijk en wie kan Mij ter verantwoording roepen? 20Welke herder blijft tegenover Mij op de been? Neem er daarom nota van: de Here zal dit vast en zeker doen met Edom en het volk van Teman, zelfs kleine kinderen zullen als slaven worden weggesleept! Het zal vreselijk zijn om te zien. 21De aarde beeft door het lawaai van Edoms val, het geschreeuw van haar inwoners is tot bij de Rode Zee te horen. 22Degene die zal komen, vliegt zo snel als een arend en zal zijn vleugels over Bosra uitspreiden. Dan zal de moed van de beste strijders verdwijnen als die van vrouwen die moeten bevallen.’

23Damascus

‘De steden Hamath en Arpad zijn verstijfd van angst, want zij hebben het slechte nieuws over hun toekomst gehoord. Het stormt in hun harten. 24Damascus heeft alle moed verloren en haar inwoners slaan op de vlucht. Ze zijn overmand door angst, vertwijfeling en pijn, zoals een vrouw tijdens de bevalling. 25Beroemde stad, die eens vol leven was, wat ligt u er nu verlaten bij! 26Uw jonge mannen zullen dood in de straten liggen, uw hele leger zal worden vernietigd,’ zegt de Here van de hemelse legers. 27‘Bij de muren van Damascus zal Ik een vuur aansteken dat de paleizen van Benhadad in de as zal leggen.’

28Kedar en Hazor

Deze profetie spreekt over Kedar en de koninkrijken van Hazor, die zullen worden verwoest door koning Nebukadnezar van Babel. ‘Maak u klaar en val Kedar aan,’ zegt de Here. ‘Vernietig de stammen in het oosten. 29Hun kuddes en tenten zullen worden buitgemaakt, samen met al hun huisraad. Hun kamelen zullen worden geroofd en overal zal in paniek worden geschreeuwd: “Wij zijn aan alle kanten omsingeld!” 30Vlucht voor uw leven,’ zegt de Here. ‘Ga diep de woestijn in, volk van Hazor, want koning Nebukadnezar van Babel heeft een aanslag op u beraamd en maakt zich klaar om u te vernietigen. 31Ga,’ zegt de Here tegen koning Nebukadnezar. ‘Val die rijke bedoeïenenstammen aan die daar eenzaam in de woestijn wonen, zonder zich ergens zorgen over te maken. Zij scheppen voortdurend op dat zij wel voor zichzelf kunnen zorgen en geen muren of poorten nodig hebben. 32Hun kamelen en kudden vee zijn voor u. Ik zal deze heidenen als door de wind uiteenjagen. Van alle kanten zal Ik rampen over hen laten komen. 33Hazor zal veranderen in een plaats voor jakhalzen, een woestenij. Niemand zal zich daar nog vestigen. Het zal voor altijd uitgestorven zijn.’

34Elam

Gods boodschap over Elam kreeg Jeremia aan het begin van de regering van koning Zedekia van Juda: 35de Here van de hemelse legers zegt: ‘Ik zal het leger van Elam vernietigen 36en Ik zal het volk van Elam in alle windrichtingen verspreiden, het zal verbannen worden naar alle landen van de wereld. 37Mijn vreselijke toorn zal een grote ramp over Elam brengen,’ zegt de Here, ‘en Ik zal ervoor zorgen dat haar vijanden haar wegvagen. Met het zwaard zal Ik haar achterna zitten en haar voorgoed uit de weg ruimen. 38Ik zal mijn troon in Elam neerzetten,’ zegt de Here. ‘Ik zal haar koning en bewindslieden vernietigen. 39Maar in de laatste dagen zal Ik het volk zijn welvaart teruggeven,’ zegt de Here.