Yeremiya 3 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 3:1-25

1“Ngati munthu asudzula mkazi wake

ndipo mkaziyo nʼkuchoka nakakwatiwa ndi mwamuna wina,

kodi mwamuna woyambayo angathe kumutenganso mkaziyo?

Kodi atatero sindiye kuti dzikolo layipitsidwa kwambiri?

Koma iwe Israeli wachita zadama ndi zibwenzi zambiri.

Komabe bwerera kwa ine,”

akutero Yehova.

2“Tayangʼana ku zitunda zowuma.

Kodi aliponso malo ena amene iwe sunachitepo zadama?

Iwe unkakhala mʼmbali mwa njira kumadikira zibwenzi zako,

ngati Mluya wobisalira anthu mʼchipululu.

Inu mwayipitsa dziko ndi zadama zanu

ndi ntchito zanu zoyipa.

3Nʼchifukwa chake Yehova wayimitsa mvula,

ndipo mvula ya nthawi ya masika sinagwe.

Komabe uli ndi maonekedwe a mkazi wachiwerewere;

ndipo sukuchita manyazi ndi pangʼono pomwe.

4Kodi iwe siposachedwa pomwepa pamene wanena

kuti, ‘Abambo anga, Inu bwenzi langa la unyamata wanga,

5kodi mudzandikwiyira nthawi zonse?

Kodi ukali wanu udzakhalabe mpaka muyaya?’

Umu ndimo mmene umayankhulira,

koma umapitirizabe kuchita zoyipa monga momwe umathera.”

Kusakhulupirika kwa Israeli

6Pa nthawi ya Mfumu Yosiya Yehova anandiwuza kuti, “Kodi waona zomwe Israeli wosakhulupirika uja wachita? Anakwera pa phiri lililonse lalitali ndi kupita pa tsinde pa mtengo uliwonse wogudira kukapembedza. Choncho anachita za chiwerewere kumeneko. 7Ndinaganiza kuti atachita zonsezi, adzabwerera kwa Ine, koma sanabwerere, ndipo mlongo wake wosakhulupirika uja, Yuda, anaziona zimenezi. 8Anaona kuti ndinasudzula Israeli wosakhulupirikayo ndi kumupirikitsa chifukwa cha zigololo zake. Komabe Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanaope, nayenso anapita kukachita chigololo. 9Chiwerewere cha Israeli chinali chochititsa manyazi kotero kuti chinayipitsa dziko lonse. Anachita chigololo popembedza mafano a miyala ndi mitengo. 10Israeli atachita zonsezi, Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanabwerere kwa Ine ndi mtima wake wonse, koma mwachiphamaso chabe,” akutero Yehova.

11Yehova anandiwuza kuti, “Kusakhulupirika kwa Israeli nʼkochepa kuyerekeza ndi kusakhulupirika kwa Yuda. 12Pita ukalalikire kumpoto uthenga wakuti,

“ ‘Israeli wosakhulupirikawe, bwerera,’ akutero Yehova.

‘Sindidzakukalipira mpaka kalekale,

pakuti ndine wachifundo,’ akutero Yehova.

‘Sindidzakukwiyira mpaka kalekale.

13Ungovomera kulakwa kwako

kuti unawukira Yehova Mulungu wako.

Vomera kuti unayendayenda kukapembedza milungu yachilendo

pansi pa mtengo uliwonse wogudira,

ndiponso kuti sunandimvere,’ ”

akutero Yehova.

14“Bwererani, ana osakhulupirika, pakuti ndine mbuye wanu,” akutero Yehova. “Ndinakusankhani, mmodzimmodzi kuchokera ku mudzi uliwonse ndiponso awiriawiri kuchokera ku banja lililonse. 15Ndipo ndidzakupatsani abusa a pamtima panga amene adzakutsogolerani mwanzeru ndi mwaluntha. 16Masiku amenewo mukadzachulukana kwambiri mʼdzikomo, anthu sadzanenanso za ‘Bokosi la Chipangano la Yehova’ kapena kuliganizira. Sadzalikumbukiranso kapena kulifuna, ndipo sadzapanganso lina,”

akutero Yehova.

17Nthawi imeneyo adzatcha Yerusalemu Mpando Waufumu wa Yehova, ndipo mitundu yonse ya anthu idzasonkhana mu Yerusalemu pamaso pa Yehova. Sadzawumiriranso kutsata mitima yawo yoyipa. 18Masiku amenewo fuko la Yuda lidzaphatikizana ndi fuko la Israeli, onse pamodzi adzachokera ku dziko la kumpoto kupita ku dziko limene ndinapatsa makolo awo, kuti likhale cholowa.

19“Ine mwini ndinati,

“ ‘Ndikanakonda bwanji kukukhazikani pakati pa ana anga

ndikukupatsani dziko labwino kwambiri,

cholowa chokongola kwambiri kuposa cha mitundu ina ya anthu.’

Ndinaganiza kuti mudzanditcha Ine ‘Atate’

ndi kuti simudzaleka kunditsata.

20Koma monga mkazi wosakhulupirika amasiya mwamuna wake,

momwemonso inu mwakhala osakhulupirika kwa Ine, inu fuko la Israeli,”

akutero Yehova.

21Mawu akumveka pa magomo,

Aisraeli akulira ndi kupempha chifundo

chifukwa anatsata njira zoyipa

ndi kuyiwala Yehova Mulungu wawo.

22Inu mukuti, “Bwererani, anthu osakhulupirika;

ndidzachiritsa kubwerera mʼmbuyo kwanu.”

“Inde, tidzabwerera kwa Inu

pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.

23Ndithu kupembedza pa magomo

komanso kuchita maphwando pa mapiri zilibe phindu.

Zoonadi chipulumutso cha Israeli

chili mwa Yehova Mulungu wathu basi.

24Kuyambira pa ubwana wathu milungu yochititsa manyazi ija yakhala ikutiwonongetsa phindu

la ntchito za makolo athu,

nkhosa ndi ngʼombe zawo,

ana awo aamuna ndi aakazi.

25Tilekeni tigone pansi mwa manyazi,

ndipo kunyozeka kwathu kutiphimbe.

Paja tachimwira Yehova Mulungu wathu,

ife pamodzi ndi makolo athu

kuyambira nthawi ya ubwana wathu mpaka lero lino

sitinamvere Yehova Mulungu wathu.”

Het Boek

Jeremia 3:1-25

De ontrouw van Israël

1De Here zei tegen mij: ‘Als een man zijn vrouw verstoot en zij gaat bij hem weg en trouwt met een andere man, kan hij dan nog wel bij haar terugkeren? Als zoiets veel zou voorkomen, zou het hele land ontheiligd worden. Maar u leeft als een prostituee en houdt er talloze minnaars op na. Denkt u dan echt dat u ooit weer naar Mij kunt terugkeren?’ zegt de Here. 2‘Is er één plaats in dit land waar u zich niet hebt laten misbruiken door overspel? U zit als een prostituee langs de kant van de weg, als een rover in de woestijn. U hebt het land verontreinigd met uw prostitutie en andere goddeloze daden. 3Daarom bleven de lenteregens uit. Want u bent een prostituee en net zo brutaal. 4-5 En toch zegt u tegen Mij: “Och vader, U bent altijd mijn vriend geweest. U kunt toch niet boos blijven om zoiets onbelangrijks! Dat zult U toch wel vergeten?” Zo praat u, maar ondertussen gaat u gewoon door met zoveel mogelijk kwaad te doen.’

6De volgende boodschap van de Here kreeg ik tijdens de regering van koning Josia: ‘Hebt u gezien hoe ontrouw Israël is? Als een prostituee die zich bij elke gelegenheid aan mannen geeft, aanbad Israël haar afgoden op elke heuvel en in de schaduw van elke boom. 7Ik dacht dat zij op een goede dag naar Mij zou terugkeren en weer van Mij zou zijn, maar zij kwam niet terug. En haar trouweloze zuster Juda zag de voortdurende opstandigheid van Israël. 8Toch schonk zij daar geen aandacht aan, ook al zag zij dat Ik het ontrouwe Israël verstootte. Maar nu heeft ook Juda Mij verlaten en zich aan anderen verkocht. 9Lichtzinnig, zonder er verder bij na te denken, begon zij stenen en houten afgoden te vereren. Zo werd het land verontreinigd en ontheiligd. 10Deze trouweloze zuster Juda keerde niet echt naar Mij terug, want haar berouw was maar schijn,’ zegt de Here God.

11‘Als het erop aankomt, is het ontrouwe Israël minder schuldig dan het bedrieglijke Juda! 12Daarom moet u naar het noorden gaan en tegen Israël zeggen: Israël, mijn zondige volk, kom weer terug bij Mij, want Ik ben genadig, Ik zal niet altijd toornig op u blijven. 13Erken dat u schuldig bent, geef toe dat u opstandig bent geweest tegen de Here, uw God, en overspel pleegde door onder elke boom afgoden te aanbidden, beken dat u weigerde Mij te volgen. 14O zondige kinderen, kom tot inkeer, want Ik ben uw meester en zal u terugbrengen naar het land Israël, één uit elke stad en twee uit elk geslacht, waar u ook bent. 15Ik zal u leiders naar mijn hart geven, die u zullen leiden met kennis en verstand. 16Dan, als uw land opnieuw bevolkt is,’ zegt de Here, ‘zult u niet langer verlangen naar die goede oude tijd, toen u de ark van Gods verbond in uw midden had. Niemand zal die tijd missen of eraan terugdenken en er zal ook geen nieuwe ark worden gemaakt, 17want de Here zal Zelf bij u zijn en de hele stad Jeruzalem zal bekendstaan als de Troon van de Here en alle volken zullen daar samenkomen om de naam van de Here te loven. Zij zullen niet langer hun eigen zondige verlangens volgen. 18In die tijd zullen de volken Israël en Juda gezamenlijk terugkeren uit de ballingschap naar het land dat Ik hun voorouders als een eeuwige erfenis heb gegeven. 19En Ik bedacht hoe heerlijk het zou zijn als Ik u als mijn eigen kinderen kon verzorgen. Ik was van plan u dit prachtige land, het mooiste ter wereld, te geven. Ik verlangde ernaar dat u Mij vader zou noemen en Ik dacht dat u zich nooit meer van Mij zou afkeren. 20Maar u hebt Mij bedrogen, Israël, u hebt zich gedragen als een ontrouwe vrouw die haar man in de steek heeft gelaten.

21Vanaf de kale heuvels hoor Ik stemmen die huilend smeken. Het is het volk Israël dat de Here de rug heeft toegekeerd en ver van Hem is afgedwaald. 22O mijn opstandige kinderen, kom weer bij Mij terug, dan zal Ik u genezen van uw zonden. En zij zullen antwoorden: “Ja, wij komen terug, want U bent de Here, onze God. 23Wij zijn het aanbidden van afgoden op de heuvels en het houden van feesten in de bergen zat. Het is allemaal erg tegengevallen. Alleen in de Here, onze God, kan Israël haar hulp en heil vinden. 24Sinds onze jeugd hebben wij gezien dat het bezit van onze voorouders is verspild aan afgoden: runderen, schapen, zonen en dochters. 25Wij knielen neer in schaamte en schande, want wij en onze voorouders hebben sinds onze jeugd tegen de Here, onze God, gezondigd, wij hebben Hem niet gehoorzaamd.” ’