Yeremiya 26 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 26:1-24

Yeremiya Amangidwa

1Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti, 2“Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe. 3Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa. 4Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani, 5ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere, 6ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’ ”

7Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova. 8Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa! 9Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.

10Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova. 11Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”

12Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno. 13Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni. 14Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera. 15Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”

16Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”

17Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti, 18“Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“ ‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda,

Yerusalemu adzasanduka bwinja,

ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’

19Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”

20(Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya. 21Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto. 22Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto. 23Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).

24Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.

La Bible du Semeur

Jérémie 26:1-24

Salut pour Israël et Juda

Conflit de Jérémie avec les responsables religieux

Prédication au Temple

1Au commencement du règne de Yehoyaqim, fils de Josias, roi de Juda, l’Eternel m’adressa la parole :

2Voici ce que déclare l’Eternel : Tiens-toi dans le parvis du temple de l’Eternel, et proclame aux habitants de toutes les villes de Juda qui viennent se prosterner dans le Temple, tout ce que je t’ordonne de leur dire ; tu n’en retrancheras pas un mot. 3Peut-être écouteront-ils et renonceront-ils à leur mauvaise conduite ; alors je renoncerai, de mon côté, au malheur que j’ai décidé de leur infliger à cause de leurs mauvaises actions. 4Tu leur diras : Voici ce que déclare l’Eternel : Si vous ne m’écoutez pas, si vous ne vivez pas selon la Loi que je vous ai donnée, 5si vous n’écoutez pas les paroles de mes serviteurs les prophètes que je vous envoie sans me lasser, depuis longtemps, sans que vous les écoutiez, 6alors je traiterai ce temple comme j’ai traité le sanctuaire de Silo26.6 Voir 7.12 et note., et tous les peuples de la terre utiliseront le nom de cette ville dans leurs imprécations.

7Les prêtres, les prophètes et tout le peuple entendirent Jérémie prononcer ces paroles dans la cour du Temple. 8A peine eut-il achevé de dire tout ce que l’Eternel lui avait ordonné de dire à tout le peuple, que les prêtres, les prophètes et tout le peuple se saisirent de lui en criant : A mort ! A mort ! 9Comment oses-tu prophétiser au nom de l’Eternel en disant que ce temple va subir le même sort que le sanctuaire de Silo, et que cette ville sera détruite au point qu’il n’y restera plus d’habitants ?

Et toute la foule s’attroupa autour de Jérémie dans le Temple. 10Lorsque les ministres de Juda apprirent ce qui se passait, ils montèrent du palais royal au Temple et siégèrent à l’entrée de la « porte Neuve » du Temple26.10 Sans doute pour juger le cas de Jérémie. La porte Neuve est celle qu’avait fait construire le roi Yotam (2 R 15.35) ; elle est mentionnée aussi en 36.10. Elle menait au parvis intérieur.. 11Alors les prêtres et les prophètes dirent aux ministres et à toute la foule : Cet homme mérite d’être condamné à mort, car il a prophétisé contre cette ville, comme vous l’avez entendu de vos propres oreilles.

12Jérémie dit à tous les ministres et à toute la foule : L’Eternel m’a chargé de prophétiser au sujet de ce temple et de cette ville tout ce que vous m’avez entendu dire. 13Maintenant, adoptez une conduite bonne et agissez selon ce qui est bien et obéissez à l’Eternel, votre Dieu, alors l’Eternel renoncera au malheur dont il vous a menacés. 14Quant à moi, je suis en votre pouvoir, faites de moi ce que vous jugerez bon et juste. 15Mais, sachez bien que si vous me faites mourir, vous vous rendrez responsables, vous, cette ville et ses habitants, du meurtre d’un innocent, car l’Eternel m’a vraiment envoyé vers vous pour vous dire toutes ces choses.

16Alors les ministres et tout le peuple dirent aux prêtres et aux prophètes : Cet homme ne mérite pas la mort, car c’est au nom de l’Eternel, notre Dieu, qu’il nous a parlé.

17Quelques responsables du pays se levèrent et dirent à toute la foule qui était rassemblée : 18Au temps d’Ezéchias, roi de Juda, Michée de Morésheth prophétisait et il a dit ceci à tout le peuple de Juda : Voici ce que déclare le Seigneur des armées célestes :

Sion seralabourée comme un champ,

et Jérusalem deviendraun tas de ruines ;

le mont du Templesera une collinecouverte de broussailles26.18 Mi 3.12..

19A-t-il été mis à mort pour cela par Ezéchias, roi de Juda, ou par le peuple de Juda ? Le roi n’a-t-il pas plutôt craint l’Eternel ? Il l’a imploré, si bien que l’Eternel a renoncé au malheur dont il les avait menacés. Et nous, nous nous rendrions responsables d’un si grand crime26.19 Autre traduction : nous nous attirerions un terrible malheur. ?

20Il y avait encore un autre homme qui prophétisait au nom de l’Eternel : Urie, fils de Shemaya, de Qiryath-Yearim. Lui aussi prophétisa contre cette ville et contre ce pays, dans les mêmes termes que Jérémie. 21Le roi Yehoyaqim, tous les hommes de sa garde et tous ses ministres entendirent ses discours. Et le roi chercha à le faire mourir. Urie l’apprit, il eut peur et s’enfuit en Egypte. 22Mais le roi Yehoyaqim envoya des hommes en Egypte : Elnathan, fils d’Akbor26.22 Elnathan: l’un des ministres du roi Yehoyaqim (36.12). Il interviendra auprès du roi en faveur de Jérémie (36.14-26) et demanda au prophète de se cacher (36.19)., accompagné de quelques autres. 23Ils ramenèrent Urie d’Egypte et le conduisirent devant le roi Yehoyaqim26.23 Cet épisode se place sans doute au début du règne de Yehoyaqim au temps où il était encore vassal du pharaon Néko (2 Ch 36.4) et où il pouvait donc lui demander l’extradition du prophète. qui le fit tuer par l’épée et ordonna de jeter son cadavre dans la fosse commune.

24Quant à Jérémie, il avait l’appui d’Ahiqam, fils de Shaphân26.24 Il s’agit probablement du Shaphân qui fut le secrétaire royal (voir 2 R 22.12-14). Ahiqam aura comme fils Guedalia, gouverneur de Juda après la chute de Jérusalem (40.7). Guemaria, un défenseur de Jérémie (36.12, 25) est sans doute aussi son fils., qui empêchait qu’il soit livré au peuple pour être mis à mort.