Yeremiya 25 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 25:1-38

Zaka 70 za Ukapolo

1Yehova anayankhula ndi Yeremiya za anthu onse a ku Yuda mʼchaka chachinayi cha ufumu wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda, chimene chinali chaka choyamba cha ufumu wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni. 2Choncho mneneri Yeremiya anawuza anthu onse a ku Yuda pamodzi ndi onse amene amakhala mu Yerusalemu kuti: 3Kwa zaka 23, kuyambira chaka cha 13 cha ufumu wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya ku Yuda mpaka lero lino, Yehova wakhala akundipatsa mauthenga ake ndipo ine ndakhala ndikuyankhula ndi inu kawirikawiri, koma inu simunamvere.

4Ndipo ngakhale Yehova kawirikawiri wakhala akukutumizirani atumiki ake onse, aneneri, inuyo simunamvere kapena kutchera khutu. 5Aneneriwo ankanena kuti, “Ngati aliyense wa inu abwerere, kusiya njira zake zoyipa ndi machitidwe ake oyipa, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko limene Yehova anapereka kwa makolo anu kwamuyaya. 6Musatsatire milungu ina nʼkuyitumikira ndi kuyipembedza. Musapute mkwiyo wanga ndi mafano amene mwapanga ndi manja anu. Mukatero Ine sindidzakuwonongani.

7“Koma inu simunandimvere,” akutero Yehova, “ndipo munaputa mkwiyo wanga ndi mafano amene munapanga ndi manja anu. Choncho munadziwononga nokha.”

8Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Chifukwa simunamvere mawu anga, 9ndidzayitana mafuko onse akumpoto, pamodzi ndi mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni,” akutero Yehova, “ndipo adzathira nkhondo dziko lino ndi anthu ake pamodzi ndi mitundu yonse ya anthu ozungulira dzikoli. Ndidzawawononga kwathunthu ndi kuwasandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka, mpaka muyaya. 10Ndidzathetsa mfuwu wachimwemwe ndi wachisangalalo, mawu a mkwati ndi mkwatibwi, phokoso la mphero ndi kuwala kwa nyale. 11Dziko lonse lidzakhala bwinja ndi chipululu, ndipo mitundu ina idzatumikira mfumu ya ku Babuloni kwa 70.

12“Koma zaka 70 zikadzatha, ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi anthu ake, chifukwa cha zolakwa zawo,” akutero Yehova, “ndipo dziko lawo lidzakhala chipululu mpaka muyaya. 13Ndidzachita zinthu zonse zimene ndinayankhula zotsutsa dzikolo, zonse zimene zalembedwa mʼbuku lino, ndiponso zonse zimene Yeremiya analosera zotsutsa anthu amenewa. 14Iwo eni adzakhala akapolo a anthu a mitundu yochuluka ndi mafumu amphamvu. Ndidzawabwezera molingana ndi zochita zawo ndi ntchito za manja awo.”

Chikho cha Ukali wa Mulungu

15Yehova, Mulungu wa Israeli, anandiwuza kuti, “Tenga chikho ichi chodzaza ndi vinyo wa ukali wanga, ndipo ukamwetse anthu a mitundu yonse kumene ndikukutuma. 16Akadzamwa adzayamba kudzandira ndi kuchita misala chifukwa cha nkhondo imene ndikuyitumiza pakati pawo.”

17Choncho ine ndinatenga chikhocho mʼdzanja la Yehova ndipo ndinamwetsa mitundu yonse ya anthu kumene Iye ananditumako: 18Anandituma ku Yerusalemu ndi ku mizinda ya Yuda, kwa mafumu ake ndi nduna zake kuti ndikawasandutse ngati bwinja ndi chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka ndiponso chotembereredwa, monga mmene alili lero lino. 19Ananditumanso kwa Farao, mfumu ya ku Igupto, kwa atumiki ake, nduna zake ndi kwa anthu ake onse, 20ndi kwa anthu ena onse a mitundu yachilendo; mafumu onse a ku Uzi; mafumu onse a Afilisti, a ku Asikeloni, ku Gaza, ku Ekroni ndiponso kwa anthu a ku chigwa chotsala cha Asidodi; 21Edomu, Mowabu ndi Amoni. 22Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Turo ndi ku Sidoni; kwa mafumu a kutsidya la nyanja; 23ku Dedani, ku Tema, ku Buzi ndi kwa onse ometa chamʼmbali. 24Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Arabiya ndi mafumu onse a anthu achilendo amene amakhala mʼchipululu. 25Anandituma kwa mafumu onse a ku Zimuri, Elamu ndi Mediya; 26ndiponso kwa mafumu onse a kumpoto, akufupi ndi kutali omwe, mafumu onse a dziko lapansi. Ndipo potsiriza pake, idzamwenso ndi mfumu Sesaki.

27“Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Imwani, ledzerani ndipo musanze, mugwe osadzukanso chifukwa cha nkhondo imene ndikutumiza pakati panu.’ 28Koma ngati akana kutenga chikhocho mʼdzanja lako ndi kumwa, uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Muyenera kumwa ndithu!’ ” 29Taonani, tsopano ndiyamba kulanga mzinda uno umene umadziwika ndi dzina langa. Kodi inu muganiza kuti simudzalangidwa? Ayi, simudzapulumuka chifukwa ndikutumiza nkhondo pa onse okhala pa dziko lapansi, akutero Yehova Wamphamvuzonse.

30“Tsopano iwe nenera mawu owatsutsa ndipo uwawuze kuti,

“ ‘Yehova adzabangula kumwamba;

mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera ku malo ake opatulika.

Adzabangula mwamphamvu kukalipira dziko lake.

Iye adzafuwula ngati anthu oponda mphesa,

kukalipira onse amene akukhala pa dziko lapansi.

31Phokoso lalikulu lidzamveka mpaka kumalekezero a dziko lonse lapansi,

chifukwa Yehova adzazenga mlandu anthu a mitundu yonse;

adzaweruza mtundu wonse wa anthu

ndipo oyipa adzawapha ndi lupanga,’ ”

akutero Yehova.

32Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Taonani! Mavuto akuti akachoka

pa mtundu wina akukagwa pa mtundu wina;

mphepo ya mkuntho ikuyambira

ku malekezero a dziko.”

33Pa tsiku limenelo, onse ophedwa ndi Yehova adzangoti mbwee ponseponse, pa dziko lonse lapansi. Palibe amene adzawalire kapena kusonkhanitsa mitemboyo kuti ikayikidwe mʼmanda, koma idzakhala mbwee ngati ndowe.

34Khetsani misozi ndi kufuwula mwamphamvu, abusa inu;

gubudukani pa fumbi, inu atsogoleri a nkhosa.

Pakuti nthawi yanu yophedwa yafika;

mudzagwa ndi kuphwanyika ngati mbiya yabwino kwambiri.

35Abusa adzasowa kothawira,

atsogoleri a nkhosa adzasowa malo opulumukira.

36Imvani kulira kwa abusa,

atsogoleri a nkhosa akulira,

chifukwa Yehova akuwononga msipu wawo.

37Makola awo a nkhosa amene anali pamtendere adzasanduka bwinja

chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.

38Ngati mkango, Yehova wasiya phanga lake,

pakuti dziko lawo lasanduka chipululu

chifukwa cha nkhondo ya owazunza

ndiponso chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米书 25:1-38

预言被掳七十年

1犹大约西亚的儿子约雅敬执政第四年,即巴比伦尼布甲尼撒元年,耶和华告诉了耶利米有关犹大百姓的事。 2耶利米先知对犹大人和耶路撒冷的居民说: 3“从犹大亚们的儿子约西亚执政第十三年,到今天已有二十三年。在这期间,我不断把耶和华对我说的话传给你们,你们却充耳不闻。 4耶和华屡次差遣祂的仆人——众先知警告你们,你们却充耳不闻,毫不理会。 5他们对你们说,‘要改邪归正,停止作恶,以便可以永远住在耶和华赐给你们和你们祖先的土地上。 6不要随从、供奉、祭拜其他神明,不要制造神像惹耶和华发怒,免得祂惩罚你们。’” 7耶和华说:“然而,你们不听我的话,制造神像惹我发怒,自招惩罚。”

8因此,万军之耶和华说:“由于你们不遵行我的命令, 9我要召集北方各族和我的仆人巴比伦尼布甲尼撒,去攻击这片土地和其中的居民以及周围各国。我要彻底毁灭他们,使他们的下场很可怕、令人嗤笑、土地永远荒凉。这是耶和华说的。 10我要使他们的欢乐声、新郎新娘的欢笑声、推磨声和灯光都消失。 11整片土地要变得荒凉可怕,他们要臣服于巴比伦王七十年。 12七十年后,我要报应巴比伦王和他国民迦勒底人的罪,使他们的土地永远荒凉。这是耶和华说的。 13我借耶利米所说有关列国的预言都记在这书上了,我的话必应验在他们的土地上。 14他们必受许多国家和强大君王的奴役,我要按他们的所作所为报应他们。”

上帝审判列国

15以色列的上帝耶和华对我说:“你从我手中接过这盛满我烈怒的酒杯,到我差遣你去的国家给他们喝。 16他们喝了这杯烈怒后必东倒西歪、行为疯狂,因为我要使战祸临到他们。” 17于是,我从耶和华手中接过杯,奉祂的差遣到列国去给他们喝。 18我给耶路撒冷犹大的城邑,以及犹大的君王和官员喝这杯烈怒,使他们的城邑沦为废墟,令人惊惧,被嘲笑和咒诅,正如今日一样。 19喝这杯烈怒的还有埃及王法老及其王公大臣和全体百姓, 20他们当中所有的外族人,乌斯的众王和统治亚实基伦迦萨以革伦以及亚实突余民的非利士众王, 21以东摩押亚扪人, 22泰尔的众王、西顿的众王和海岛上的众王, 23底但提玛布斯和所有剃鬓发的人, 24阿拉伯的众王和荒野各族的诸王, 25心利的众王、以拦的众王和玛代的众王, 26北方诸王——无论远近、一个接一个,以及天下万国,最后是巴比伦王。 27耶和华对我说:“你要告诉他们,以色列的上帝——万军之耶和华说,‘你们要喝这杯烈怒,喝得大醉、呕吐、倒地不起,因为我要使战争临到你们。’ 28如果他们不肯从你手中接过杯来喝,你就告诉他们,万军之耶和华说,‘你们必须喝! 29看啊,我已在属我的城中降下灾祸,难道你们可以逃脱惩罚吗?你们必逃不过惩罚,因为我要使战争临到天下万民。’这是万军之耶和华说的。 30耶利米啊,你要告诉他们这些预言,

“‘耶和华要在高天怒吼,

从祂的圣所发出雷鸣;

祂要向祂的子民怒吼,

向地上的居民吶喊,

好像踩踏葡萄的人一样。

31耶和华的声音传到地极,

因为祂要指控列国,审判万民,

使恶人丧身刀下。

这是耶和华说的。’”

32万军之耶和华说:

“看啊,灾难正蔓延到列国,

有暴风从地极卷起。”

33到那日,遍地都是被耶和华杀戮的人,无人哀悼、收殓和埋葬,他们好像地上的粪便。

34你们这群牧人啊,要悲哀哭泣!

你们这群百姓的首领啊,

要在灰尘中伤心地打滚!

因为你们被宰杀、驱散的时候到了,

你们将像精美的器皿一样被摔得粉碎。

35牧人必无路可逃,

百姓的首领必无处藏身。

36听听牧人的哭喊,

百姓首领的哀号吧,

因为耶和华正在毁灭他们的家园。

37因为耶和华的烈怒,

宁静的草场变得一片荒凉。

38耶和华离开了祂的居所,

就像狮子离开了洞穴。

他们的土地因刀剑的蹂躏和耶和华的烈怒而一片荒凉。