Yeremiya 20 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 20:1-18

Yeremiya ndi Pasuri

1Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi. 2Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova. 3Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse. 4Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo. 5Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni. 6Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’ ”

Madandawulo a Yeremiya

7Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi;

Inu ndi wamphamvu kuposa ine ndipo munandipambana.

Anthu akundinyoza tsiku lonse.

Aliyense akundiseka kosalekeza.

8Nthawi iliyonse ndikamayankhula,

ndimafuwula kunena kuti, ziwawa kuno! Tikuwonongeka!

Mawu anu Yehova andisandutsa chinthu chonyozeka

ndipo ndimachitidwa chipongwe tsiku lonse.

9Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye

kapena kuyankhulanso mʼdzina lake,”

mawu anu amayaka ngati moto mu mtima mwanga,

amakhaladi ngati moto wotsekeredwa mʼmafupa anga.

Ndapirira kusunga mawu anu mu mtima mwanga osawatulutsa,

koma sindingathe kupirirabe.

10Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti,

“Zoopsa ku mbali zonse!

Kamunenezeni! Tiyeni tikamuneneze!”

Onse amene anali abwenzi anga

akuyembekezera kuti ndigwa pansi, akumanena kuti,

“Mwina mwake adzanyengedwa;

tidzamugwira

ndi kulipsira pa iye.”

11Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu.

Nʼchifukwa chake ondizunza adzalephera ndipo sadzandipambana.

Adzachita manyazi kwambiri chifukwa sadzapambana.

Manyazi awo sadzayiwalika konse.

12Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama

ndipo mupenya za mu mtima mwa munthu.

Ndiloleni kuti ndione kuti mwalipsira adani anga

popeza ndapereka mlandu wanga kwa Inu.

13Imbirani Yehova!

Mutamandeni Yehova!

Iye amapulumutsa wosauka

mʼmanja mwa anthu oyipa.

14Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa!

Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!

15Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga

ndi uthenga woti:

“Kwabadwa mwana wamwamuna!”

16Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene

Yehova anayiwononga mopanda chisoni.

Amve mfuwu mmawa,

phokoso la nkhondo masana.

17Chifukwa sanandiphere mʼmimba,

kuti amayi anga asanduke manda anga,

mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.

18Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni

kuti moyo wanga

ukhale wamanyazi wokhawokha?

Hoffnung für Alle

Jeremia 20:1-18

Jeremia wird misshandelt

1Als der Priester Paschhur, der Sohn von Immer, ein Oberaufseher im Tempel, diese Weissagungen von Jeremia hörte, 2ließ er ihn schlagen und in einen Raum im oberen Benjamintor bringen, das zum Tempelbezirk führte. Dort schloss man Jeremias Hände und Füße in einen Holzblock ein.

3Am nächsten Morgen ließ Paschhur Jeremia wieder frei. Da sagte der Prophet zu ihm: »Der Herr nennt dich nicht mehr Paschhur, sondern Magor Missabib (›Schrecken überall‹). 4Denn so spricht der Herr: Ich mache dich zum Schrecken – für dich selbst und für all deine Freunde! Mit eigenen Augen wirst du sehen, wie sie durchs Schwert der Feinde umkommen. Ich liefere die Bewohner von ganz Juda dem König von Babylonien aus; er wird einen Teil von ihnen in sein Land verschleppen und die anderen umbringen lassen. 5Den ganzen Reichtum dieser Stadt übergebe ich ihren Feinden: die wertvollen Gegenstände, den mühsam erworbenen Besitz und die Schätze der Könige von Juda. Alles wird geplündert und nach Babylon gebracht. 6Dich, Paschhur, wird man samt deiner Familie nach Babylonien in die Gefangenschaft führen. Dort wirst du sterben, und dort wird man dich begraben, dich und all deine Freunde, denen du hier falsche Prophetien verkündet hast!«

Herr, du hast den Kampf gewonnen!

7Herr, du hast mich überredet, und ich habe mich überreden lassen! Du bist stärker als ich und hast den Kampf gewonnen. Und nun werde ich lächerlich gemacht – tagaus, tagein; alle verhöhnen mich! 8Denn sooft ich das Wort ergreife, muss ich schreien: »Gewalt und Zerstörung erwarten euch!« Deine Botschaft bringt mir nichts als Hohn und Spott. 9Wenn ich mir aber vornehme: »Ich will nicht mehr an Gott denken und nicht länger in seinem Namen reden«, dann brennt dein Wort in meinem Herzen wie ein Feuer, ja, es glüht tief in mir. Ich habe versucht, es zurückzuhalten, aber ich kann es nicht! 10Ich höre viele hinter meinem Rücken tuscheln: »Von ihm hört man nichts als Schreckensmeldungen! Zeigt ihn an, wir wollen ihn verklagen!« Alle, denen ich vertraut habe, lauern darauf, dass ich zu Fall gebracht werde. »Vielleicht lässt er sich hereinlegen, dann ist er uns ausgeliefert, und wir können uns an ihm rächen!«, sagen sie.

11Aber du, Herr, stehst mir bei wie ein mächtiger Held! Darum werden meine Feinde stürzen und nicht den Sieg davontragen. Nein, es wird ihnen niemals gelingen! Unvergesslich und groß wird ihre Schande sein! 12Herr, allmächtiger Gott, du prüfst die Menschen, die nach deinem Willen leben, du kennst sie ganz genau. Lass mich mit eigenen Augen sehen, wie du meine Feinde für ihre Bosheit bestrafst! Dir habe ich meinen Fall anvertraut. 13Singt für den Herrn und lobt ihn! Denn er rettet den Armen aus der Gewalt boshafter Menschen.

Warum nur bin ich geboren?

14Verflucht sei der Tag, an dem ich geboren wurde; der Tag, an dem meine Mutter mich zur Welt brachte, soll für immer vergessen werden! 15Verflucht sei der Mann, der meinem Vater die frohe Nachricht brachte: »Du hast einen Sohn bekommen!« 16Es möge ihm ergehen wie den Städten, die der Herr erbarmungslos vernichtet hat! Schon am Morgen soll er Schreckensschreie hören und am Mittag Kriegsalarm! 17Wäre ich doch im Mutterleib gestorben. Dann wäre meine Mutter mein Grab geworden und für immer schwanger geblieben! 18Warum nur bin ich geboren? Um ein Leben zu führen, das mir nichts als Leid und Elend bringt? Um jeden Tag nur Schimpf und Schande zu ernten?