Yeremiya 13 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 13:1-27

Lamba Womanga Mʼchiwuno

1Yehova anandiwuza kuti, “Pita kagule lamba wansalu yosalala ndipo ukavale mʼchiwuno mwako, koma usakamuviyike mʼmadzi.” 2Choncho ndinakagula lambayo, monga momwe anandiwuzira Yehova, ndipo ndinamanga mʼchiwuno mwanga.

3Kenaka Yehova anandiyankhulanso kachiwiri kuti, 4“Tenga lamba amene unagula ndi kuvala mʼchiwuno mwako uja. Tsono pita ku mtsinje wa Yufurate ndipo ukamubise lambayo mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.” 5Ndipo ndinapitadi ndi kukabisa lambayo ku Yufurate, monga anenera Yehova.

6Patapita masiku ambiri Yehova anandiwuzanso kuti, “Pitanso ku Yufurate ndipo ukatenge lamba amene ndinakuwuza kuti ukamubise kumeneko.” 7Choncho ndinapita ku Yufurate kukafukula lambayo ndi kumuchotsa pamalo pamene ndinamubisa, koma nthawi imeneyi nʼkuti lambayo atawonongeka kotheratu ndipo analibenso ntchito.

8Pamenepo Yehova anandiwuza kuti, 9“Izi ndi zimene ine ndikunena: ‘Umu ndi mmene ndidzawonongere zimene akunyadira kwambiri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. 10Anthuwa ndi oyipa. Iwo akana kumvera mawu anga. Mʼmalo mwake amawumirira kutsata milungu ina, kuyitumikira ndi kuyipembedza. Anthu amenewa adzakhala ngati lamba wopanda ntchitoyu. 11Monga momwe lamba amakanirira mʼchiwuno cha munthu, momwemonso ndinakonza kuti nyumba yonse ya Israeli ndi nyumba yonse ya Yuda indikangamire Ine kuti akhale anthu anga, kuti azitamanda dzina langa ndi kulemekeza Ine. Koma iwo sanamvere,’ akutero Yehova.

Zikopa Zothiramo Vinyo

12“Awuze anthuwo kuti, ‘Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Mtsuko uliwonse adzawudzaza ndi vinyo.’ Ndipo ngati iwo anena kwa iwe kuti, ‘Kodi ngati ife sitikudziwa kuti mtsuko uliwonse udzadzazidwa ndi vinyo?’ 13Tsono iwe uwawuze kuti, Yehova akuti ‘Ine ndidzaledzeretsa anthu onse okhala mʼdziko muno, kuyambira mafumu amene amakhala pa mpando waufumu wa Davide, ansembe, aneneri, pamodzi ndi anthu onse amene akukhala mu Yerusalemu. 14Ndidzawagundanitsa mitu kuti aphwanyane okhaokha ngati mitsuko, makolo ndi ana awo, akutero Yehova. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwachitira chifundo kapena kukhudzidwa nawo kuti ndileke kuwawononga.’ ”

Yuda Adzapita ku Ukapolo

15Imvani inu Aisraeli ndipo tcherani khutu,

musadzitukumule,

pakuti ndi Yehova amene akuyankhula.

16Lemekezani Yehova Mulungu wanu

asanagwetse mdima,

mapazi anu asanayambe kupunthwa

mʼchisisira chamʼmapiri.

Asanasandutse kuwala

mukuyembekezerako kukhala

mdima wandiweyani.

17Koma ngati simumvera,

ndidzalira kwambiri

chifukwa cha kunyada kwanu.

Mʼmaso mwanga

mwadzaza ndi misozi yowawa

chifukwa nkhosa za Yehova zatengedwa ukapolo.

18Uza mfumu pamodzi ndi amayi ake kuti,

“Tsikani pa mipando yaufumuyo,

pakuti zipewa zanu zaufumu zokongolazo

zagwa pansi.”

19Mizinda ya ku Negevi yatsekedwa

ndipo palibe wina woti nʼkuyitsekula.

Yuda yense watengedwa kupita ku ukapolo,

watengedwa yense ukapolo.

20Tukula maso ako kuti uwone

amene akubwera kuchokera kumpoto.

Kodi nkhosa zimene anakusungitsa zili kuti,

nkhosa zanu zokongola zija?

21Kodi udzanena chiyani pamene [Yehova] adzakuyikira

anthu amene unkanena kuti ndi abale ako akukugonjetsa ndi kukulamulira?

Kodi sudzamva zowawa

ngati za mayi pa nthawi yake yochira?

22Ndipo ngati udzadzifunsa kuti,

“Kodi zimenezi zandichitikira chifukwa chiyani?”

Ndi chifukwa cha machimo anu ambiri

kuti zovala zanu zingʼambike

ndiponso kuti akuchitireni nkhanza.

23Kodi wa dziko la Kusi nʼkusintha khungu lake,

kapena kambuku kusintha mawanga ake?

Inunso amene munazolowera kuchita

zoyipa simungathe kusintha.

24“Ine ndidzakumwazani ngati mankhusu

amene amawuluka ndi mphepo ya ku chipululu.

25Limeneli ndiye gawo lanu,

chilango chimene ndakukonzerani

chifukwa chondiyiwala Ine

ndi kutumikira milungu yabodza,

akutero Yehova.

26Ine ndidzakwinya zovala zanu mpaka ku maso

kuti umaliseche wanu uwonekere.

27Ndaona zonyansa zanu: zigololo zanu, kutchetcherera kwanu

ndi ziwerewere zanu,

zochitika pa mapiri ndi mʼminda.

Tsoka iwe Yerusalemu!

Udzakhala wosayeretsedwa

pa zachipembedzo mpaka liti?”

Het Boek

Jeremia 13:1-27

Het lot van het volk

1De Here zei tegen mij: ‘Koop een linnen riem en doe die om, maar zorg dat hij niet nat wordt.’ 2Ik kocht een riem en deed hem om mijn middel. 3Toen sprak de Here opnieuw tegen mij en zei: 4‘Neem de riem mee naar de Eufraat en verberg hem daar in een grot tussen de rotsen.’ 5Dat deed ik, ik verborg de riem, zoals de Here mij had opgedragen. 6Een hele tijd later zei de Here tegen mij: ‘Ga weer naar de rivier en haal de riem op.’ 7Ik deed dat en groef de riem op uit de grot waarin ik hem had verborgen. Maar hij was helemaal verrot en viel uit elkaar. Hij was onbruikbaar geworden! 8-9 Toen zei de Here: ‘Dit laat zien hoe Ik de trots van Juda en Jeruzalem zal breken. 10Dit slechte volk weigert naar Mij te luisteren, volgt zijn eigen zondige verlangens en vereert afgoden. Daarom zal het net als deze riem totaal onbruikbaar worden. 11Zoals een riem rond de heupen van een man vastzit, zo zaten Juda en Israël aan Mij vast,’ zegt de Here. ‘Zij waren mijn volk en deden mijn naam eer aan. Maar toen keerden zij Mij de rug toe.

12Zeg hun dit: de Here, de God van Israël zegt: al uw kruiken moeten vol zitten met wijn. En zij zullen antwoorden: natuurlijk, we weten zelf ook wel dat kruiken gevuld moeten zijn. 13Zeg dan tegen hen: dit is wat de Here u te zeggen heeft: Ik zal ieder die in dit land woont dronken maken, de koning die op de troon van David zit, de priesters, de profeten en heel Jeruzalem. 14Ik zal vaders en zonen tegen elkaar aan stukken slaan,’ zegt de Here. ‘Ik zal niet toelaten dat medelijden of genade hen van de totale verwoesting redden.

15Och, was u maar niet zo trots en koppig! Dan zou u wel luisteren naar de woorden van de Here. 16Geef alle eer aan de Here, uw God, voordat het te laat is. Voordat Hij een diepe, ondoordringbare duisternis op u laat neerdalen, zodat u struikelt op de donkere bergen. Als u dan zoekt naar licht, zult u alleen een vreselijke duisternis vinden. 17Weigert u nog steeds te luisteren? Dan zal Ik in eenzaamheid huilen om uw trots. Mijn ogen zullen zich met tranen vullen, omdat het volk van de Here in slavernij zal worden weggevoerd. 18Zeg tegen de koning en de koningin-moeder: kom van uw tronen af, want uw prachtige kronen worden u afgenomen. Zij zijn niet langer van u. 19De steden van de Negev tot aan de zuidkant van Jeruzalem hebben hun poorten voor de vijand gesloten. Zij moeten zichzelf verdedigen, want Jeruzalem kan niet helpen. Er woont helemaal niemand meer in Juda. 20Kijk eens hoe de legers uit het noorden oprukken! Waar is uw kudde, Jeruzalem, de prachtige kudde waarover Ik u de verantwoordelijkheid heb gegeven en waarop u zo trots was? 21Hoe zult u zich voelen als Ik uw bondgenoten als heersers over u aanstel? U zult kronkelen van pijn als een vrouw die een kind baart. 22Als u zich afvraagt: “Waarom overkomt mij dit?” dan is dat om uw vele zonden, daarom zijn uw kleren afgerukt en wordt uw eer geschonden. 23Kan de Ethiopiër zijn huidskleur veranderen? Kan een luipaard zijn vlekken laten verdwijnen? Net zo min kunt u, die zo gewend bent kwaad te doen, beginnen goed te doen. 24-25 Omdat u Mij uit uw gedachten hebt verbannen en hebt vertrouwd op valse goden, zal Ik u verspreiden als kaf, dat wordt weggeblazen door de woestijnwind. Dit is het lot dat u zichzelf op de hals hebt gehaald en dat Ik u heb toegewezen. 26Ik zal zorgen dat uw naaktheid en schande door iedereen gezien worden. 27Ik heb het allemaal gezien: uw overspel en uw begeren, uw ontrouw tegenover Mij en uw afschuwelijke afgoderij in de velden en op de heuvels. Pas op Jeruzalem! Hoelang duurt het nog voordat u weer rein wordt?’