Yeremiya 12 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 12:1-17

Madandawulo a Yeremiya

1Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse

ndikati nditsutsane nanu.

Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga.

Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino?

Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?

2Inu munawadzala ndipo anamera mizu;

amakula ndi kubereka zipatso.

Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse,

koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.

3Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa;

mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga.

Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa!

Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!

4Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti

ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti?

Nyama ndi mbalame kulibiretu

chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa.

Iwo amati:

“Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”

Yankho la Mulungu

5Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu

nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo?

Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino,

udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango

za ku Yorodani?

6Ngakhale abale ako

ndi anansi akuwukira,

onsewo amvana zokuyimba mlandu.

Usawakhulupirire,

ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.

7“Ine ndawasiya anthu anga;

anthu amene ndinawasankha ndawataya.

Ndapereka okondedwa anga

mʼmanja mwa adani awo.

8Anthu amene ndinawasankha

asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango.

Akundibangulira mwaukali;

nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.

9Anthu anga amene ndinawasankha

asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga

imene akabawi ayizinga.

Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo.

Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.

10Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa,

anapondereza munda wanga;

munda wanga wabwino uja

anawusandutsa chipululu.

11Unawusandutsadi chipululu.

Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine.

Dziko lonse lasanduka chipululu

chifukwa palibe wolisamalira.

12Anthu onse owononga abalalikira

ku zitunda zonse za mʼchipululu.

Yehova watuma ankhondo ake

kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko,

ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.

13Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga;

anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse.

Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu

chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”

14“Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo. 15Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake. 16Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga. 17Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

耶利米书 12:1-17

耶利米的抱怨

1耶和华啊,每次我与你争论,

都显明你是对的。

然而,我还是对你的公正有所不解:

为什么恶人总是得势?

为什么诡诈之人反而生活安逸?

2你栽培他们,让他们生根长大,

结出果实。

他们嘴上尊崇你,

心却远离你。

3但耶和华啊,你认识我,了解我,

察验我的内心。

求你拖走他们,

就像拖走待宰的羊,

留到宰杀之日。

4大地哀恸、

田野的植物枯槁要到何时呢?

由于这地方居民的罪恶,

野兽和飞鸟都灭绝了。

他们说:“上帝看不见我们的行为12:4 上帝看不见我们的行为”参照《七十士译本》,希伯来文也可译作“他(指耶利米)看不见我们的结局”。。”

5耶和华说:“如果你与步行的人竞走,

尚且感到疲乏,

又怎能与马赛跑呢?

如果你在宽阔之地尚且跌倒,

约旦河边的丛林中又会怎样呢?

6你的弟兄和家人都背叛了你,

与你作对。

任他们甜言蜜语,你不要相信。

7“我已离开我的殿,

撇弃我的产业,

把我爱的子民交给他们的敌人。

8我的子民像林中的狮子一样向我吼叫,

因此我憎恶他们;

9我的子民就像一只带斑点的鸷鸟,

被其他鸷鸟围攻。

招聚野兽来吞吃它吧!

10列国的首领毁坏我的葡萄园,

践踏我美好的土地,

使它荒凉;

11他们使这片土地荒凉,

以致它在我面前哀哭。

遍地如此荒凉,却无人在意。

12杀戮者已来到旷野中光秃的山岭,

耶和华使刀剑横扫全境,

无人幸免。

13我的子民播种麦子,

却收割荆棘;

辛勤耕耘,却一无所获。

他们必因耶和华的烈怒而收获羞辱。”

14耶和华说:“邪恶的邻国侵占了我赐给我以色列子民的土地,我要把这些恶邻逐出他们的本土,正如我要逐出犹大一样。 15我逐出他们以后,还要再怜悯他们,把他们带回各自的家园和故土。 16如果他们真心接受我子民的信仰,凭永活的耶和华之名起誓,正如他们教导我子民向巴力起誓一样,他们便能成为我的子民。 17如果哪一国不听我的话,我必把它连根拔起,彻底毁灭。这是耶和华说的。”