Tito 1 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tito 1:1-16

1Ndine Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndinatumidwa kuti nditsogolere amene Mulungu anawasankha ku chikhulupiriro ndi ku chidziwitso cha choonadi chimene chimawafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu 2ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. 3Pa nthawi yake Mulungu, Mpulumutsi wathu anawulula poyera mawu ake ndipo analamula kuti ndipatsidwe udindo wolalikira uthengawu.

4Kwa Tito, mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro cha ife tonse:

Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.

Ntchito ya Tito ku Krete

5Ndinakusiya ku Krete kuti ulongosole zonse zimene ndinazisiya zisanathe ndiponso usankhe akulu ampingo mʼmizinda yonse, monga momwe ndinakulamulira. 6Mkulu wampingo akhale munthu wopanda cholakwa, akhale wa mkazi mmodzi yekha, munthu amene ana ake ndi okhulupirira, osati amakhalidwe oyipa ndi osamvera. 7Popeza mkulu wa mpingo amayendetsa ntchito za banja la Mulungu, ayenera kukhala wopanda cholakwa, asakhale womva zayekha, kapena wopsa mtima msanga, kapena womwa zoledzeretsa, kapena wandewu, kapena wopeza phindu mwachinyengo. 8Koma akhale wosamala bwino alendo, wokonda zabwino, wodziretsa, wolungama, woyera mtima ndi wosunga mwambo. 9Iye ayenera kugwiritsa mawu okhulupirika monga tinaphunzitsira, kuti athe kulimbikitsa ena ndi chiphunzitso choona ndiponso kugonjetsa amene atsutsana nacho.

Kudzudzula Olephera Kuchita Bwino

10Paja pali anthu ambiri osaweruzika, makamaka mʼgulu la anthu a mdulidwe, oyankhula nkhani zopanda pake ndi kusocheretsa anzawo. 11Ayenera kuletsedwa kuyankhula chifukwa akusokoneza mabanja athunthu pophunzitsa zinthu zomwe sayenera kuwaphunzitsa. Iwo amachita izi kuti apeze ndalama mwachinyengo. 12Mneneri wina, mmodzi wa iwo omwewo anati, “Akrete nthawi zonse ndi amabodza, akhalidwe loyipitsitsa ndiponso alesi adyera.” 13Mawu amenewa ndi woona. Nʼchifukwa chake, uwadzudzule mwamphamvu, kuti akhale ndi chikhulupiriro choona, 14kuti asasamalenso nthano za Chiyuda, ndi malamulo a anthu amene akukana choonadi. 15Kwa oyera mtima, zinthu zonse ndi zoyera, koma kwa amene ndi odetsedwa ndi osakhulupirira, palibe kanthu koyera. Kunena zoona, mitima yawo ndi chikumbumtima chawo, zonse nʼzodetsedwa. 16Iwo amati amadziwa Mulungu, pamene ndi zochita zawo amamukana. Ndi anthu onyansa ndi osamvera, ndi osayenera kuchita kalikonse kabwino.

New Serbian Translation

Титу 1:1-16

Увод

1Од Павла, слуге Божијег и апостола Исуса Христа.

Бог ме је изабрао да подстакнем веру изабраника Божијих и њихово знање о истини која је у сагласности са побожношћу, 2која се темељи на нади у вечни живот. Бог који не лаже обећао је овај живот пре почетка времена, 3а у своје време објавио своју реч кроз службу проповедања која ми је поверена наредбом нашег Спаситеља, Бога.

4Титу, мом правом детету у заједничкој вери. Милост ти и мир од Бога Оца и Христа Исуса, нашег Спаситеља.

Титова служба на Криту

5Оставио сам те на Криту да уредиш што је недовршено, и да поставиш старешине по градовима, према упутствима која сам ти дао. 6Старешина треба да је беспрекоран, једне жене муж, да има верујућу децу, којој се не приговара да су раскалашна и непослушна. 7Јер будући да надгледник врши службу управљања коју му је поверио Бог, он треба да је беспрекоран, а не саможив, ни раздражљив, ни склон пићу, ни насилник, нити лаком на непоштен добитак. 8Напротив, он треба да је гостољубив, да воли добро, да је разуман, праведан, посвећен, уздржљив. 9Он треба да се чврсто држи поуздане поруке нашег учења, да буде у стању да опомиње са здравим учењем, и да уверава оне који се противе учењу.

10Има, наиме, много непослушних, који говоре бесмислице, те заводе друге, нарочито они од обрезаних. 11Овима треба запушити уста, јер уносе пометњу у целе породице учећи што не треба, све зарад непоштеног добитка. 12Један од њих, њихов сопствени пророк, рече: „Крићани су вазда лажљивци, зле звери, и лењи трбуси.“ 13Ова изјава је истинита. Због тога их строго опомињи да буду здрави у вери, 14да не обраћају пажњу на јудејске приче и заповести људи који одбацују истину. 15Чистима је све чисто, а опогањенима и невернима ништа није чисто, него су им ум и савест опогањени. 16Они исповедају да познају Бога, али га се својим делима одричу. Они су гнусни и непослушни људи, неспособни за било какво добро дело.