Tito 1 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tito 1:1-16

1Ndine Paulo, mtumiki wa Mulungu, ndi mtumwi wa Yesu Khristu. Ndinatumidwa kuti nditsogolere amene Mulungu anawasankha ku chikhulupiriro ndi ku chidziwitso cha choonadi chimene chimawafikitsa ku moyo wolemekeza Mulungu 2ndi kuwapatsa chiyembekezo cha moyo wosatha, umene Mulungu amene sanama, analonjeza nthawi isanayambe. 3Pa nthawi yake Mulungu, Mpulumutsi wathu anawulula poyera mawu ake ndipo analamula kuti ndipatsidwe udindo wolalikira uthengawu.

4Kwa Tito, mwana wanga weniweni mʼchikhulupiriro cha ife tonse:

Chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Mpulumutsi wathu.

Ntchito ya Tito ku Krete

5Ndinakusiya ku Krete kuti ulongosole zonse zimene ndinazisiya zisanathe ndiponso usankhe akulu ampingo mʼmizinda yonse, monga momwe ndinakulamulira. 6Mkulu wampingo akhale munthu wopanda cholakwa, akhale wa mkazi mmodzi yekha, munthu amene ana ake ndi okhulupirira, osati amakhalidwe oyipa ndi osamvera. 7Popeza mkulu wa mpingo amayendetsa ntchito za banja la Mulungu, ayenera kukhala wopanda cholakwa, asakhale womva zayekha, kapena wopsa mtima msanga, kapena womwa zoledzeretsa, kapena wandewu, kapena wopeza phindu mwachinyengo. 8Koma akhale wosamala bwino alendo, wokonda zabwino, wodziretsa, wolungama, woyera mtima ndi wosunga mwambo. 9Iye ayenera kugwiritsa mawu okhulupirika monga tinaphunzitsira, kuti athe kulimbikitsa ena ndi chiphunzitso choona ndiponso kugonjetsa amene atsutsana nacho.

Kudzudzula Olephera Kuchita Bwino

10Paja pali anthu ambiri osaweruzika, makamaka mʼgulu la anthu a mdulidwe, oyankhula nkhani zopanda pake ndi kusocheretsa anzawo. 11Ayenera kuletsedwa kuyankhula chifukwa akusokoneza mabanja athunthu pophunzitsa zinthu zomwe sayenera kuwaphunzitsa. Iwo amachita izi kuti apeze ndalama mwachinyengo. 12Mneneri wina, mmodzi wa iwo omwewo anati, “Akrete nthawi zonse ndi amabodza, akhalidwe loyipitsitsa ndiponso alesi adyera.” 13Mawu amenewa ndi woona. Nʼchifukwa chake, uwadzudzule mwamphamvu, kuti akhale ndi chikhulupiriro choona, 14kuti asasamalenso nthano za Chiyuda, ndi malamulo a anthu amene akukana choonadi. 15Kwa oyera mtima, zinthu zonse ndi zoyera, koma kwa amene ndi odetsedwa ndi osakhulupirira, palibe kanthu koyera. Kunena zoona, mitima yawo ndi chikumbumtima chawo, zonse nʼzodetsedwa. 16Iwo amati amadziwa Mulungu, pamene ndi zochita zawo amamukana. Ndi anthu onyansa ndi osamvera, ndi osayenera kuchita kalikonse kabwino.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

אגרת פולוס אל-טיטוס 1:1‏-16

1‏-2מאת פולוס, עבדו של אלוהים ושליחו של ישוע המשיח. נשלחתי לחזק ולבנות את אמונתם של המשיחיים וללמדם את אמת אלוהים, שבה הכוח לשנות חיי אדם, כדי שיוכלו לקבל את מתנת חיי הנצח שהבטיח להם ה׳ עוד לפני בריאת העולם, ואלוהים אינו משקר. 3אלוהים החליט כי עכשיו הזמן המתאים לגלות ברבים את הבשורה על אודות בנו, והוא עצמו הטיל עלי את המשימה הזאת וציווה עלי לבצעה למענו.

4אל טיטוס, בני האמיתי באמונה.

יברך אותך אלוהים וישכין בלבך שלום ושלווה.

5השארתיך באי־כרתים כדי שתעזור כמיטב יכולתך לתיקון ולחיזוק הקהילות שם, וכדי שבכל עיר תמנה זקנים אשר ימלאו את ההוראות שנתתי לך.

6‏-7אלה הן הדרישות מהזקנים – עליהם להיות: בעלי שם טוב וללא דופי (שהרי הם שליחי ה׳), בעלים לאישה אחת בלבד, שילדיהם אוהבים את אלוהים, בעלי תדמית טובה, מחונכים היטב וממושמעים, שלא אשמים בשום פשע, ענווים, לא רגזניים, שאינם מרבים בשתיית יין, לא אלימים, שונאי בצע, 8מכניסי אורחים, אוהבים כל דבר טוב, נבונים, ישרי, בעלי ריסון עצמי 9ובעלי אמונה חזקה ויציבה באמת (כדי שיוכלו לעמוד בוויכוח עם מתנגדיהם ולהוכיחם על טעותם).

10אנשים רבים מסרבים לשמוע בקול אלוהים, במיוחד בין אלה שטוענים שהמאמינים המשיחיים חייבים לעבור ברית מילה ולקיים את כל ההלכה כדי להיוושע. 11עלינו לשים קץ לדבר, כי אנשים אלה הרחיקו משפחות רבות מן האמת אך ורק למען בצע כסף. 12אחד מאנשיהם, נביא מכרתים, אמר עליהם: ”אנשי כרתים הם שקרנים, חיות אכזריות וגזלנים עצלנים!“ 13וזוהי האמת. משום כך דבר אל המאמינים בחומרה הנדרשת ועורר אותם להתחזק באמונתם. 14הזהר אותם שלא יקשיבו לסיפורים ולאגדות הרווחות בין היהודים, ושלא ישמעו לאנשים שדוחים את האמת.

15אדם טוב מוצא מעלות ויתרונות בכל דבר, ואילו אדם רשע, שאי־אפשר לסמוך עליו, מוצא פגמים וחסרונות בכל דבר, בגלל מחשבותיו הטמאות ותכונותיו הרעות.

16אנשים אלה טוענים שהם מאמינים באלוהים, אולם מעשיהם ואורח חייהם אינם מעידים על כך. הם כופרים, עושים מעשי תועבה ואינם מסוגלים לעשות כל מעשה טוב.