Oweruza 7 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 7:1-25

Gideoni Agonjetsa Amidiyani

1Yeru-Baala (Gideoni) ndi anthu ake onse anadzuka mʼmamawa nakamanga misasa pambali pa kasupe ku Harodi. Misasa ya Amidiyani inali mʼchigwa kumpoto kwa phiri la More. 2Yehova anati kwa Gideoni, “Anthu uli nawowa andichulukira kwambiri kuti ndigonjetse Amidiyani chifukwa Aisraeli angamadzitukumule pamaso panga ndi kumanena kuti, ‘Tadzipulumutsa ndi mphamvu zathu.’ 3Tsono lengeza kwa anthu kuti, ‘Aliyense amene akuchita mantha ndi kunjenjemera abwerere kwawo, ndipo achoke kuno ku phiri la Giliyadi.’ ” Choncho anthu 22,000 anachoka, ndipo anatsalira anthu 10,000.

4Koma Yehova anawuza Gideoni kuti, “Anthuwa achulukabe. Uwatenge upite nawo ku mtsinje ndipo ndikawayesa kumeneko mʼmalo mwako. Ndikadzanena kuti, ‘Uyu apite nawe’ adzapita nawe; koma ndikanena kuti ‘Uyu asapite nawe,’ sadzapita nawe.”

5Choncho Gideoni anatenga anthuwo ndi kupita nawo ku madzi. Kumeneko Yehova anamuwuza kuti, “Amene amwe madzi mokhathira ndi manja ngati galu uwayike pawokha, ndipo amene amwe atagwada pansi uwayikenso pawokha.” 6Ndipo anthu 300 anamwa mokhathira, pamene ena onse anagwada pansi pakumwa.

7Yehova anati kwa Gideoni, “Ndi anthu 300 amene anamwa madzi mokhathira ndi manja awo ndidzakupulumutsani ndipo ndidzapereka Amidiyani mʼmanja mwanu. Koma anthu ena onse apite ku nyumba kwawo.” 8Choncho analola anthu ena onse kuti apite ku nyumba zawo kupatula anthu 300 osankhika aja. Iwowa anatenga zakudya ndi malipenga a anthuwo.

Ndipo misasa ya ankhondo Amidiyani inali kumunsi kwa chigwa. 9Usiku umenewo Yehova anati kwa Gideoni, “Dzuka, pita kachite nkhondo ku misasayo, chifukwa ndayipereka mʼmanja mwako. 10Ngati ukuopa, upite ku msasako ndi Pura wantchito wako, 11ndipo ukamvere zimene akunena ndipo pambuyo pake udzalimba mtima ndi kupita kukayithira nkhondo misasayo.” Choncho iye ndi wantchito wake Pura anapita kumbali ina ya msasawo kumene kunali ankhondo. 12Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena onse akummawa anadzaza chigwa chonse ngati dzombe. Ngamira zawo zinali zambiri zosawerengeka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.

13Gideoni atafika anangomva munthu wina akuwuza mnzake maloto ake kuti, “Ine ndinalota nditaona dengu la buledi wa barele likugubuduzika kupita ku misasa ya Amidiyani. Litafika linawomba tenti moti inagwa ndi kuphwasukaphwasuka.”

14Ndipo mnzakeyo anamuyankha kuti, “Iyi ndi nkhondo ya Gideoni mwana wa Yowasi, wa ku Israeli. Mulungu wapereka Amidiyani pamodzi ndi ankhondo ake onse mʼdzanja mwake.”

15Gideoni atamva za malotowo ndi kumasulira kwake, anapembedza Mulungu. Kenaka anabwerera ku msasa wa Israeli nawawuza kuti, “Dzukani popeza Yehova wapereka msasa wa Midiyani mʼmanja mwanu.” 16Anawagawa anthu 300 aja magulu atatu, nawapatsa malipenga mʼmanja mwawo ndi mbiya zimene mʼkati mwake munali nsakali zoyaka.

17Anawuza anthuwo kuti, “Muzikayangʼana ine ndi kuchita zimene ndizikachita. Ndikakafika kumalire a msasa, mukachite zomwe ndikachita ine. 18Ndikadzaliza lipenga ndi onse amene ali ndi ine, inunso mukalize malipenga kumbali zonse za misasa yonse ndi kufuwula kuti, ‘Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.’ ”

19Choncho Gideoni pamodzi ndi amuna 100 omwe anali nawo anafika ku malire a msasa pakati pa usiku, alonda atangosinthana kumene. Iwo analiza malipenga awo ndi kuphwanya mbiya zimene zinali mʼmanja mwawo. 20Magulu awiri ena aja anayimbanso malipenga ndi kuswa mbiya zawo. Aliyense ananyamula nsakali ya moto ku dzanja lamanzere ndi lipenga ku dzanja lamanja ndipo anafuwula kuti, “Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.” 21Aliyense anayima pa malo pake kuzungulira misasa. Ankhondo a mʼmisasa muja anadzuka nayamba kuthawa akufuwula.

22Anthu 300 aja ataliza malipenga, Yehova anawasokoneza ankhondo a Midiyani aja motero kuti ankamenyana okhaokha. Ankhondowo anathawira ku Beti-Sita cha ku Zerera mpaka ku malire a Abeli-Mehola pafupi ndi Tabati. 23Aisraeli a fuko la Nafutali, fuko la Aseri, ndi fuko lonse la Manase anayitanidwa, ndipo iwo anathamangitsa Amidiyaniwo. 24Gideoni anatumiza amithenga ku dziko lonse la ku mapiri la Efereimu kukanena kuti, “Tsikani mumenyane ndi Amidiyani ndipo mulande madooko awo owolokera mpaka ku Beti-Bara.”

Choncho anthu onse a fuko la Efereimu anasonkhana ndipo analanda madooko awo owolokera mpaka ku Betibaala. 25Iwo anagwiranso atsogoleri awiri a nkhondo a Amidiyani, Orebu ndi Zeebu. Anapha Orebu ku thanthwe la Orebu, koma Zeebu anamuphera ku malo ofinyira mphesa ku Zeebu pothamangitsa Amidiyani. Mitu ya Orebu ndi Zeebu anabwera nayo kwa Gideoni kutsidya kwa Yorodani.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Судьи 7:1-25

1Иеруб-Баал (он же Гедеон) и все его люди встали рано утром и расположились станом у источника Харод. Лагерь мадианитян находился к северу от них, в долине, рядом с холмом Море.

2Вечный сказал Гедеону:

– Воинов с тобой слишком много. Я не стану отдавать мадианитян в их руки. Чтобы Исроил не мог гордиться предо Мной, что его спасла его собственная сила, 3объяви воинам: «Всякий, кто боится и дрожит от страха, пусть уходит домой и оставит гору Галаад».

И двадцать две тысячи человек ушло, а десять тысяч осталось.

4Но Вечный сказал Гедеону:

– Воинов всё ещё слишком много. Отведи их к воде, и там Я испытаю их для тебя. О ком Я скажу тебе: «Этот пойдёт с тобой», тот пойдёт, а о ком скажу: «Этот с тобой не пойдёт», тот и не пойдёт.

5И Гедеон отвёл воинов к воде. Там Вечный сказал ему:

– Отдели тех, кто лакает воду языком, как собака, от тех, кто встал на колени, чтобы пить.

6Триста воинов лакали воду языком, а все остальные, чтобы напиться, встали на колени, поднося воду ко рту руками.

7Вечный сказал Гедеону:

– Тремя сотнями воинов, которые лакали, Я спасу вас и отдам мадианитян в ваши руки. Все остальные пусть идут домой. 8И Гедеон отпустил всех остальных исроильтян по шатрам, но оставил триста воинов, которым достались запасы пищи и боевые рога ушедших.

А лагерь мадианитян находился внизу, в долине. 9В ту же ночь Вечный сказал Гедеону:

– Встань, напади на лагерь, потому что Я отдам его в твои руки. 10Если ты боишься напасть, спустись к лагерю вместе со своим слугой Пурой 11и послушай, что они говорят. Это придаст тебе смелости напасть на лагерь.

Тогда Гедеон и его слуга Пура спустились к сторожевым заставам лагеря. 12Мадианитяне, амаликитяне и другие восточные народы наводнили долину, словно саранча. Их верблюдов было так много, как песчинок на морском берегу.

13Когда Гедеон пришёл, один человек рассказывал другу свой сон:

– Мне снился, – говорил он, – круглый ячменный хлеб, который катился в мадианский лагерь. Прикатившись к шатру, он ударил в него так, что шатёр опрокинулся и рухнул.

14Его друг ответил:

– Это не что иное, как меч исроильтянина Гедеона, сына Иоаша. Всевышний отдал мадианитян и весь лагерь в его руки.

15Когда Гедеон услышал сон и его толкование, он поклонился Всевышнему. Гедеон возвратился в исроильский лагерь и сказал:

– Вставайте! Вечный отдал в наши руки лагерь мадианитян.

16Разделив триста воинов на три отряда, он дал всем им в руки рога и пустые сосуды с факелами внутри.

17– Смотрите на меня, – сказал он им, – и делайте, как я. Когда я доберусь до края лагеря, делайте то же, что я. 18Когда я и все, кто со мною, затрубим в наши рога, тогда и вы со всех сторон лагеря трубите в свои и кричите: «Меч за Вечного и за Гедеона!»

19Гедеон и с ним сто воинов добрались до края лагеря в одиннадцатом часу ночи, сразу же после того, как сменили часовых. Они затрубили в рога и разбили кувшины, которые были у них в руках. 20Тогда все три отряда затрубили в рога и разбили кувшины. Держа в левой руке факелы, а в правой – рога, в которые они трубили, они закричали: «Меч за Вечного и за Гедеона!» 21Каждый человек стоял на своём месте вокруг лагеря, а все мадианитяне метались, крича на бегу.

22Когда затрубили триста рогов, Вечный сделал так, что все, кто был в лагере, обратили свои мечи друг на друга. Войско бежало до самой Бет-Шитты к Церере, до самой границы Авель-Мехолы близ Таббата. 23Исроильтяне из родов Неффалима, Ошера и из всего рода Манассы погнались за мадианитянами. 24Гедеон послал вестников по всем нагорьям Ефраима:

– Спускайтесь с гор навстречу мадианитянам и захватите прежде них переправы через реки до самой Бет-Бары, а также через Иордан.

Все ефраимиты собрались и захватили переправы через Иордан и через реки до самой Бет-Бары. 25Также они пленили двух мадианских вождей – Орива и Зива. Они убили Орива, когда преследовали мадианитян, у скалы Орива, а Зива – в давильне Зива. Головы Орива и Зива они принесли Гедеону, который находился у Иордана.