Oweruza 5 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 5:1-31

Nyimbo ya Debora

1“Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:

2“Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli;

ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu,

tamandani Yehova:

3“Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu!

Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova,

Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.

4“Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri,

pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu,

dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka

nigwetsa madzi.

5Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova,

Mulungu wa Israeli.

6“Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati,

pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa;

alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.

7Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi

mpaka pamene iwe Debora unafika;

unafika ngati mayi ku Israeli.

8Pamene anasankha milungu ina,

nkhondo inabwera ku zipata za mzinda,

ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke

pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.

9Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli,

uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu.

Tamandani Yehova!

10“Inu okwera pa abulu oyera,

okhala pa zishalo,

ndi inu oyenda pa msewu,

yankhulani. 11Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta;

kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana;

akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli.

“Choncho anthu a Yehova

anasonkhana ku zipata za mzinda.

12Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera;

tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo.

Iwe Baraki! nyamuka

Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’

13“Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo;

anthu a Yehova anapita

kukamenyera Yehova nkhondo

kulimbana ndi adani amphamvu.

14Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu;

akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako.

Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri,

ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.

15Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora;

inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki,

ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira.

Koma pakati pa mafuko a Rubeni

panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.

16Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera

zitoliro zoyitanira nkhosa?

Pakati pa anthu a fuko la Rubeni

panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.

17Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani.

Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi?

Aseri anali pa gombe la Nyanja;

anangokhala mʼmadooko mwawo.

18Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa.

Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.

19“Mafumu anabwera, anachita nkhondo;

mafumu Akanaani anachita nkhondo

ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido,

koma sanatengeko zofunkha zasiliva.

20Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo,

zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.

21Mtsinje wa Kisoni unawakokolola,

chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola.

Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!

22Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu,

akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.

23Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’

‘Tembererani nzika zake mwaukali,

chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova,

kulimbana ndi adani ake amphamvu.’

24“Akhale wodala kupambana akazi onse,

Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni;

inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.

25Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka;

anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.

26Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake,

anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja.

Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake,

ndi kumubowola mu litsipa mwake.

27Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa,

anagwa; iye anagona pamenepo.

Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa;

pamene anagwera, pamenepo anaferapo.

28“Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera;

nafuwula mokweza kuti,

‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika?

Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’

29Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha,

ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,

30‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane;

akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri.

Sisera akumupatsa zofunkha:

zovala zonyikidwa mu utoto,

zoti ndizivala mʼkhosi

zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’

31“Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke,

koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa

pamene lituluka ndi mphamvu zake.”

Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.

New International Reader’s Version

Judges 5:1-31

The Song of Deborah

1On that day Deborah and Barak sang a song. Barak was the son of Abinoam. Here is what Deborah and Barak sang.

2“The princes in Israel lead the way.

The people follow them just because they want to.

When this happens, praise the Lord!

3“Kings, hear this! Rulers, listen!

I will sing to the Lord.

I will praise the Lord in song. He is the God of Israel.

4Lord, you went out from Seir.

You marched out from the land of Edom.

The earth shook. The heavens poured.

The clouds poured down their water.

5The mountains shook because of the Lord. He was at Mount Sinai.

They shook because of the Lord. He is the God of Israel.

6“The main roads were deserted. So travelers used the winding paths.

That happened in the days of Shamgar, the son of Anath.

It happened in the days of Jael.

7Those who lived in the villages of Israel would not fight.

They held back until I, Deborah, came.

I came as a mother in Israel.

8War came to the city gates. Then God chose new leaders.

But no shields or spears were seen anywhere.

There weren’t any among 40,000 men in Israel.

9My heart is with the princes in Israel.

It’s with the people who follow them just because they want to.

Praise the Lord!

10“Some of you ride on white donkeys.

Some of you sit on your saddle blankets.

Some of you walk along the road.

Think about 11the voices of the singers at the watering places.

They sing about the victories of the Lord.

They sing about the victories of his people who live in Israel’s villages.

“The people of the Lord

went down to the city gates.

12‘Wake up, Deborah! Wake up!’ they said.

‘Wake up! Wake up! Begin to sing!

Barak, get up!

Son of Abinoam, capture your prisoners!’

13“The nobles who were left came down.

The people of the Lord

came down to me against the powerful enemy.

14Some came from the part of Ephraim where some Amalekites lived.

Some from Benjamin were with the people who followed Ephraim.

Captains came down from Makir.

Those who rule like commanders came down from Zebulun.

15The princes of Issachar were with Deborah.

The men of Issachar were with Barak.

They went into the valley under his command.

In the territories of Reuben,

men looked deeply into their hearts.

16Why did they stay among the sheep pens?

Why did they stay to hear shepherds whistling for the flocks?

In the territories of Reuben,

men looked deeply into their hearts.

17Gilead stayed east of the Jordan River.

Why did Dan stay near the ships?

The men of Asher remained on the coast of the Mediterranean Sea.

They stayed in their safe harbors.

18The people of Zebulun put their very lives in danger.

So did Naphtali on the hillside fields.

19“Kings came and fought.

The kings of Canaan fought

at Taanach by the streams of Megiddo.

But they didn’t carry away any silver.

They didn’t take anything at all.

20From the heavens the stars fought.

From the sky they fought against Sisera.

21The Kishon River swept them away.

The Kishon is a very old river.

My spirit, march on! Be strong!

22The hooves of the horses pounded like thunder.

The powerful horses of our enemies galloped away.

23‘Let Meroz be cursed,’ said the angel of the Lord.

‘Let bitter curses fall on its people.

They did not come to help the Lord.

They did not come to help him against our powerful enemies.’

24“May Jael be the most blessed woman of all.

May the wife of Heber, the Kenite, be blessed.

May she be the most blessed woman of all those who live in tents.

25Sisera asked for water. She gave him milk.

In a bowl fit for nobles she brought him buttermilk.

26Her hand reached out for a tent stake.

Her right hand reached for a hammer.

She hit Sisera. She crushed his head.

She drove the stake right through his head.

27He sank down. He fell at her feet.

He was lying there.

At her feet he sank down. He fell.

He fell where he sank down.

That’s where he died.

28“Sisera’s mother looked out through the window.

From behind the wooden screen she cried out.

‘Why is his chariot taking so long to get here?’ she said.

‘Why can’t I hear the noise of his chariots yet?’

29Her wisest ladies answer her.

And here’s what she keeps saying to herself.

30She says, ‘They must be finding riches to bring back.

They must be dividing them up.

Each man is getting a woman or two.

They are giving colorful clothes to Sisera.

The clothes are very beautiful.

He will bring some for me to wear.

The men must be finding many things to bring home.’

31Lord, may all your enemies be destroyed.

But may all who love you be like the morning sun.

May they be like the sun when it shines the brightest.”

So the land was at peace for 40 years.