Oweruza 5 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 5:1-31

Nyimbo ya Debora

1“Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:

2“Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli;

ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu,

tamandani Yehova:

3“Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu!

Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova,

Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.

4“Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri,

pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu,

dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka

nigwetsa madzi.

5Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova,

Mulungu wa Israeli.

6“Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati,

pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa;

alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.

7Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi

mpaka pamene iwe Debora unafika;

unafika ngati mayi ku Israeli.

8Pamene anasankha milungu ina,

nkhondo inabwera ku zipata za mzinda,

ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke

pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.

9Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli,

uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu.

Tamandani Yehova!

10“Inu okwera pa abulu oyera,

okhala pa zishalo,

ndi inu oyenda pa msewu,

yankhulani. 11Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta;

kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana;

akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli.

“Choncho anthu a Yehova

anasonkhana ku zipata za mzinda.

12Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera;

tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo.

Iwe Baraki! nyamuka

Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’

13“Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo;

anthu a Yehova anapita

kukamenyera Yehova nkhondo

kulimbana ndi adani amphamvu.

14Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu;

akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako.

Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri,

ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.

15Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora;

inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki,

ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira.

Koma pakati pa mafuko a Rubeni

panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.

16Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera

zitoliro zoyitanira nkhosa?

Pakati pa anthu a fuko la Rubeni

panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.

17Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani.

Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi?

Aseri anali pa gombe la Nyanja;

anangokhala mʼmadooko mwawo.

18Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa.

Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.

19“Mafumu anabwera, anachita nkhondo;

mafumu Akanaani anachita nkhondo

ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido,

koma sanatengeko zofunkha zasiliva.

20Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo,

zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.

21Mtsinje wa Kisoni unawakokolola,

chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola.

Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!

22Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu,

akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.

23Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’

‘Tembererani nzika zake mwaukali,

chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova,

kulimbana ndi adani ake amphamvu.’

24“Akhale wodala kupambana akazi onse,

Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni;

inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.

25Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka;

anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.

26Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake,

anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja.

Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake,

ndi kumubowola mu litsipa mwake.

27Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa,

anagwa; iye anagona pamenepo.

Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa;

pamene anagwera, pamenepo anaferapo.

28“Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera;

nafuwula mokweza kuti,

‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika?

Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’

29Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha,

ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,

30‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane;

akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri.

Sisera akumupatsa zofunkha:

zovala zonyikidwa mu utoto,

zoti ndizivala mʼkhosi

zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’

31“Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke,

koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa

pamene lituluka ndi mphamvu zake.”

Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.

Hoffnung für Alle

Richter 5:1-31

Deboras und Baraks Siegeslied

1Am Tag des Sieges sangen Debora und Barak, der Sohn von Abinoam, dieses Lied:

2Preist den Herrn für Israels Helden,

die sich als Führer bewährten,

und für das Volk, das ihnen in den Kampf folgte!

3Hört her, ihr Könige, gebt acht, ihr Herrscher:

Für den Herrn will ich singen,

ja, singen und musizieren will ich

für den Herrn, den Gott Israels!

4Herr, du stiegst herab vom Gebirge Seïr,

aus den Steppen Edoms kamst du herbei.

Da bebte die Erde, und Regen fiel vom Himmel,

das Wasser strömte aus den Wolken nieder.

5Die Berge gerieten ins Wanken, als der Herr kam,

als der Gott Israels sich am Sinai zeigte.

6Zur Zeit Schamgars, des Sohnes von Anat,

und in den Tagen Jaëls

waren die Straßen leer:

Wer auf Reisen war, ging auf gut versteckten Pfaden.

7Felder und Dörfer lagen verwaist,

bis ich mich erhob, ja, bis ich, Debora, aufstand,

die Mutter Israels.

8Mein Volk hatte sich neue Götter erwählt,

und dann brach der Feind durch die Tore herein.

Bei vierzigtausend Männern in Israel

fand sich kein Schild und kein Speer!

9Doch nun bin ich stolz auf die Heerführer Israels

und auf alle Soldaten, die freiwillig kämpften.

Ja, preist den Herrn dafür,

10denkt darüber nach,

die ihr auf weißen Eseln mit kostbaren Satteldecken reitet,

singt auch ihr, die ihr zu Fuß gehen müsst!

11Hört, dort am Brunnen, wo man das Vieh tränkt,5,11 Der hebräische Text ist nicht sicher zu deuten.

rühmen sie die mächtigen Taten des Herrn!

Sie erzählen, wie er seinem Volk geholfen hat.

Israel konnte die Berge wieder verlassen

und ist in seine Städte zurückgekehrt.

12Auf, Debora, auf, sing ein Lied!

Steh auf, Barak, du Sohn Abinoams,

und führe deine Gefangenen fort!

13Die letzten mutigen Soldaten

kamen herab vom Gebirge

und schlossen sich den Führern Israels an.

Das Volk des Herrn kam zu mir, bereit zum Kampf:

14Die Ephraimiter rückten an aus Amaleks Land,

gefolgt von den Männern aus Benjamin.

Machirs Sippe kam mit ihren Oberhäuptern

und Sebulon mit seinen Truppenführern.

15Auch Issachars Fürsten halfen Debora,

und seine Soldaten folgten Barak ins Tal.

Der Stamm Ruben aber blieb in seinem Gebiet

und beriet ohne Ende, ob er mitkommen sollte.

16Warum nur bist du bei deinen Herden geblieben?

Um den Flöten der Hirten zu lauschen?

Doch der Stamm Ruben ließ sich nicht bewegen

und konnte zu keinem Entschluss kommen.

17Die Sippen aus Gilead ruhten sich jenseits des Jordan aus.

Warum ging der Stamm Dan nicht von seinen Schiffen?

Die Soldaten von Asser saßen am Ufer des Meeres,

untätig hockten sie an seinen Buchten.

18Sebulon schließlich wagte sein Leben,

zusammen mit Naftali zog er aufs Schlachtfeld,

ohne Furcht vor dem Tod.

19Könige kamen und kämpften,

Kanaans Könige führten Krieg gegen Israel

bei Taanach am Fluss von Megiddo.

Doch sie brachten kein Silber als Beute zurück.

20Vom Himmel her griffen die Sterne Sisera an,

von ihren Bahnen aus kämpften sie gegen ihn und sein Volk!

21Der Fluss Kischon, der schon seit Urzeiten fließt,

riss die Feinde mit sich fort.

Sei stark, Debora, verlier nicht den Mut!

22Die Pferde der Feinde galoppierten davon,

unter ihren Hufen dröhnte die Erde.

23»Verflucht sei die Stadt Meros!«,

rief der Engel des Herrn.

Ja, Unheil soll ihre Bewohner treffen!

Denn sie kamen dem Herrn nicht zu Hilfe,

sie standen den Soldaten Israels nicht bei.

24Preist Jaël, die Frau des Keniters Heber,

rühmt sie mehr als jede andere Frau!

Möge Gott sie reicher beschenken als alle Frauen,

die in Zelten zu Hause sind.

25Als Sisera um Wasser bat, reichte sie Milch,

gab ihm Sahne im kostbaren Gefäß.

26Doch dann fasste sie mit der Linken den Pflock

und mit der Rechten den wuchtigen Hammer.

Sie erschlug Sisera,

zertrümmerte seinen Schädel

und durchbohrte ihm die Schläfe.5,26 Vgl. Richter 4,17‒21.

27Er krümmte sich zu ihren Füßen,

geschlagen lag er da.

Er krümmte sich zu ihren Füßen und starb.

28Zu Hause hielt seine Mutter Ausschau nach ihm.

Sie blickte aus dem Fenster und rief voller Sorge:

»Warum sehe ich seinen Streitwagen noch nicht?

Was hält seine Pferde bloß auf?«

29Ihre weisen Beraterinnen beruhigten sie,

und auch sie selbst redete sich ein:

30»Unser Volk macht gewiss reiche Beute und teilt sie nun auf:

ein oder zwei Mädchen für jeden Mann

und für Sisera lauter bunt gewebte Gewänder.

Ja, kostbare Kleider bringen sie mit

und zwei schöne Tücher

als Schmuck um meinen Hals5,30 Oder: für die erbeuteten Frauen.

31Herr, mögen all deine Feinde sterben wie Sisera!

Doch wer dich liebt, gleicht der Sonne, die aufgeht und mit aller Kraft strahlt!

Nach Baraks Sieg über die Kanaaniter herrschte vierzig Jahre lang Frieden im Land.